< I Samuela 12 >

1 I rzekł Samuel do wszystkiego Izraela: Otom usłuchał głosu waszego we wszystkiem, o coście ze mną mówili, i postanowiłem nad wami króla.
Pambuyo pake Samueli anawuza Aisraeli onse kuti, “Ine ndamvera zonse zimene munandiwuza ndipo ndakupatsani mfumu kuti izikulamulirani.
2 A oto, teraz król chodzi przed wami, a jam się zstarzał i osiwiał; oto, i synowie moi są z wami, a jam też chodził przed wami od młodosci mojej aż do dnia tego.
Tsopano muli ndi mfumu imene izikutsogolerani, koma ine ndakalamba, kumutu kwanga kuli imvi zokhazokha ndipo ana anga ali pamodzi ndi inu. Ndakhala ndili mtsogoleri wanu kuyambira ndili mnyamata mpaka lero.
3 Otom ja tu. Świadczcież przeciwko mnie przed Panem, i przed pomazańcem jego, jeźlim wziął któremu z was wołu, albo jeźlim wziął któremu z was osła, i jeźlim kogo ucisnął, albo gwałt komu uczynił, i jeźlim z ręki czyjej wziął dar, żebym miał kryć o czy swoje dla niego; a nagrodzę wam.
Ine ndili pano. Ngati ndinalakwa chilichonse nditsutseni pamaso pa Yehova ndi wodzozedwa wake. Kodi ndinalanda ngʼombe ya yani? Kodi ndinalanda bulu wa yani? Kodi ndani amene ndinamudyera masuku pa mutu? Kodi ndinazunza yani? Kodi ndinalandira kwa yani chiphuphu choti nʼkundidetsa mʼmaso? Ngati ndinachita chilichonse cha izi, ine ndidzakubwezerani.”
4 I odpowiedzieli: Nie ucisnąłeś nas, aniś nam gwałtu uczynił, aniś wziął z ręki czyjej żadnej rzeczy.
Iwo anayankha kuti, “Inu simunatidyere masuku pamutu kapena kutizunza. Simunalande kanthu kalikonse ka munthu.”
5 Nadto rzekł do nich: Świadkiem Pan przeciwko wam, i świadkiem pomazaniec jego dnia tego, iżeście nic nie znaleźli w ręce mojej. A oni rzekli: Świadkiem.
Samueli anawawuza kuti, “Yehova ndiye mboni pakati pa inu ndi ine, ndiponso wodzozedwa wake ndi mboni kuti lero simunapeze chilichonse mʼdzanja langa.” Iwo anati, “Inde, Yehova ndiye mboni.”
6 I rzekł Samuel do lud: Pan świadkiem, który uczynił Mojżesza i Aarona, i który wywiódł ojce wasze z ziemi Egipskiej.
Samueli anawawuzanso kuti, “Yehova ndiye amene anasankha Mose ndi Aaroni kuti atulutse makolo anu mʼdziko la Igupto.
7 Przetoż teraz stańcie, abym się rozpierał z wami przed Panem, o wszystkie dobrodziejstwa Pańskie, które wam czynił i ojcom waszym.
Nʼchifukwa chake tsopano imani pomwepa kuti ndikufotokozereni pamaso pa Yehova, za ntchito za chipulumutso zimene Yehova anachitira inu ndi makolo anu.
8 Gdy zaszedł Jakób do Egiptu, wołali ojcowie wasi do Pana, i posłał Pan Mojżesza i Aarona, którzy wywiedli ojce wasze z Egiptu, a posadzili je na tem miejscu;
“Yakobo atapita ku dziko la Igupto, Aiguptowo akuwazunza, iwo analirira kwa Yehova kuti awathandize, ndipo Yehova anatumiza Mose ndi Aaroni, amene anatulutsa makolo anu mʼdziko la Igupto ndi kudzawakhazika pa malo ano.
9 A gdy zapomnieli Pana Boga swego, podał je w rękę Sysarze, hetmanowi wojska Hasor, i w rękę Filistynów, także w rękę króla Moabskiego, którzy walczyli przeciwko nim.
“Koma iwo anayiwala Yehova Mulungu wawo, choncho Yehova anawapereka mʼdzanja la Sisera mkulu wa ankhondo wa mzinda wa Hazori, ndiponso mʼmanja mwa Afilisti ndi mfumu ya Mowabu. Mafumu onsewa anathira nkhondo makolo anu.
10 Ale gdy wołali do Pana, i mówili: Zgrzeszyliśmy, żeśmy opuścili Pana, a służyliśmy Baalom i Astarotowi, przetoż teraz wybaw nas z rąk nieprzyjaciół naszych, a będziemyć służyli:
Tsono iwo analira kwa Yehova nati, ‘Ife tachimwa, chifukwa tamusiya Yehova ndi kumatumikira mafano a Baala ndi Asiteroti. Koma tsopano tilanditseni mʼmanja mwa adani athu ndipo tidzakutumikirani.’
11 Tedy posłał Pan Jerubaala, i Bedona, i Jeftego, i Samuela, a wyrwał was z ręki nieprzyjaciół waszych okolicznych, i mieszkaliście bezpiecznie.
Choncho Yehova anatumiza Yeru-Baala, Bedani, Yefita ndi Samueli ndipo anakulanditsani mʼmanja mwa adani anu amene anakuzungulirani, kotero munakhala mwamtendere.
12 Potem widząc, iż Nahas, król synów Ammonowych, przyciągnął przeciwko wam, rzekliście do mnie: Żadnym sposobem; ale król będzie królował nad nami: choć Pan Bóg wasz był królem waszym,
“Koma mutaona kuti Nahasi mfumu ya Amoni inkabwera kudzamenyana nanu, inu munandiwuza kuti, ‘Ayi, ife tikufuna mfumu kuti itilamulire,’ ngakhale kuti Yehova Mulungu wanu ndiye anali mfumu yanu.
13 Teraz tedy oto król, któregoście obrali, któregoście żądali; oto, przełożył Pan króla nad wami.
Tsopano nayi mfumu imene mwayisankha, imene munayipempha. Onani, Yehova wakupatsani mfumu.
14 Jeźli się będziecie bali Pana, a jemu służyli, i słuchali głosu jego a nie rozdraźnicie ust Pańskich, tedy i wy, i król, który króluje nad wami, będziecie szczęśliwie chodzić za Panem, Bogiem waszym.
Ngati muziopa Yehova ndi kumamutumikira ndi kumamumvera, osamupandukira ndiponso ngati inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzatsata Yehova Mulungu wanu, ndiye zinthu zonse zidzakuyenderani bwino.
15 Ale jeźliż nie będziecie słuchać głosu Pańskiego, a rozdraźnicie usta Pańskie, będzie ręka Pańska przeciwko wam, jako i przeciwko ojcom waszym.
Koma mukapanda kumvera Yehova ndi kumupandukira, ndiye adzakulangani pamodzi ndi mfumu yanu yomwe.
16 Jeszcze teraz stójcie, a obaczcie tę rzecz wielką, którą Pan uczyni przed oczyma waszemi.
“Tsono imani pomwepa kuti muone chinthu chachikulu chimene Yehova ali pafupi kuchita pamaso panu!
17 Izali dziś nie pszeniczne żniwa? Będę wzywał Pana, a puści gromy i dżdże, a dowiecie się, i obaczycie, jaka jest wielka złość wasza, którejście się dopuścili przed oczyma Pańskiemi, żądając sobie króla.
Kodi ino si nthawi yokolola tirigu? Komabe ndipemphera kwa Yehova kuti agwetse mvula ya mabingu. Zikatero mudzadziwa kuti tchimo lanu limene mwachita popempha mfumu kwa Yehova ndi lalikulu.”
18 Przetoż wołał Samuel do Pana, i puścił Pan gromy i deszcz dnia onego, i bał się wszystek lud bardzo Pana i Samuela.
Choncho Samueli anapemphera, ndipo Yehova anatumiza mvula ya mabingu tsiku lomwelo. Apo anthu aja anaopa kwambiri Yehova ndi Samueli.
19 I rzekł wszystek lud do Samuela: Módl się za sługami twymi Panu Bogu twemu, żebyśmy nie pomarli: bośmy przydali do wszystkich grzechów naszych tę złość, żeśmy sobie prosili o króla.
Tsono anamupempha Samueli nati, “Chonde mutipempherere kwa Yehova, ife atumiki kuti tingafe pakuti pa machimo athu onse tawonjezapo tchimo lopempha mfumu.”
20 Tedy rzekł Samuel do ludu: Nie bójcie się, aczeście wy to wszystko złe uczynili; wszakże przeto nie odstępujcie od Pana, ale służcie Panu ze wszystkiego serca waszego;
Samueli anayankha kuti, “Musaope, inu mwachitadi tchimo ili, koma musaleke kumutsata Yehova ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse.
21 A nie udawajcie się za próżnościami, które wam nic nie pomogą, ani was wybawią, gdyż próżnościami są.
Ndipo musatsate mafano achabechabe amene alibe phindu ndipo sangakupulumutseni popeza ndi achabechabe.
22 Albowiemci nie opuści Pan ludu swego, dla imienia swego wielkiego, gdyż się upodobało Panu, uczynić was sobie ludem.
Yehova adzakana anthu ake kuopa kuti dzina lake lamphamvu linganyozeke, pakuti chinamukondweretsa Yehova kuti akusandutseni inu kukhala anthu ake.
23 A mnie nie daj Boże, abym miał grzeszyć przeciw Panu, przestawając modlić się za wami; owszem was będę nauczał drogi dobrej i prostej.
Ndiponso kunena za ine, zisachitike kuti ndichimwire Yehova pakulephera kukupemphererani. Ndipo ine ndidzakuphunzitsani njira yabwino ndi yolungama kuti muziyendamo.
24 Jedno się bójcie Pana, a służcie mu w prawdzie ze wszystkiego serca waszego, a to upatrujcie, jako wielmożnie poczynał z wami.
Koma onetsetsani kuti mukuopa Yehova ndi kumutumikira mokhulupirika ndi mtima wanu wonse. Nthawi zonse muziganizira zinthu zazikulu wakhala akukuchitirani.
25 Ale jeźli przecię w złości trwać będziecie, tedy i wy, i król wasz poginiecie.
Komabe mukapitirira kuchita zoyipa, ndiye kuti inu pamodzi ndi mfumu yanu mudzachotsedwa.”

< I Samuela 12 >