< I Samuela 11 >

1 Tedy przyciągnął Nahas, Ammończyk, i położył się obozem przeciw Jabes Galaadskiemu. I rzekli wszyscy mężowie Jabes do Nahasa: Uczyń z nami przymierze a będziemyć służyli.
Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
2 I rzkł do nich Nahas, Ammończyk: W ten sposób uczynię z wami przymierze, jeźli wyłupię z was każdemu oko prawe, a włożę to obelżenie na wszystkiego Izraela.
Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
3 I rzekli do niego starsi z Jabes: Pozwól nam siedm dni, że roześlemy posły po wszystkich granicach Izraelskich; a jeźli nie będzie, ktoby nas ratował, tedy wynijdziemy do ciebie.
Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
4 I przyszli posłowie do Gabaa Saulowego, a powiedzieli te słowa, gdzie słyszał lud; i podniósł wszystek lud głos swój, a płakał.
Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
5 A oto, Saul szedł za wołami z pola, i rzekł Saul: Cóż się stało ludowi, iż płacze? I powiedzieli mu wszystkie słowa mężów z Jabes.
Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
6 Tedy zstąpił Duch Boży na Saula, gdy usłyszał słowa te, i zapalił się gniew jego bardzo.
Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
7 A wziąwszy parę wołów, rozrąbał je na sztuki, i rozesłał po wszystkich granicach Izraelskich przez też posły, mówiąc: Ktokolwiek nie wynijdzie za Saulem i za Samuelem, tak się stanie wołom jego. I padł strach Pański na lud, i wyszli jako mąż jeden.
Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
8 I obliczył je w Bezeku; a było synów Izraelskich trzy kroć sto tysięcy, a mężów Juda trzydzieści tysięcy.
Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
9 I rzekli posłom, którzy byli przyszli: Tak powiedzcie mężom w Jabes Galaad: Jutro będziecie wybawieni, gdy ogrzeje słońce. I wrócili się posłowie, i oznajmili to mężom w Jabes, którzy się uweselili.
Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
10 Tedy rzekli mężowie Jabese Ammonitom: Jutro wynijdziemy do was, a uczynicie z nami wszystko, co dobrego będzie w oczach waszych.
Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
11 Nazajutrz tedy rozszykował Saul lud na trzy hufy; i wtargnął w pośrodek obozu przed świtaniem; i bił Ammonity, aż się dzień ogrzał; a którzy pozostali, rozpierzchnęli się, tak, iż nie zostało z nich i dwóch pospołu.
Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
12 I rzekł lud do Samuela: Któż jest ten, co mówił: Saulże będzie królował nad nami? Wydajcie męże te, abyśmy je pobili.
Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
13 I rzekł Saul: Nie będzie nikt zabity dnia tego; bo dziś Pan uczynił wybawienie w Izraelu.
Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
14 Zatem rzekł Samuel do ludu: Pójdźcie, a idźmy do Galgal, a tam odnowimy królestwo.
Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
15 Szedł tedy wszystek lud do Galgal, i postanowili tam Saula królem przed Panem w Galgal, tamże sprawowali ofiary spokojne przed Panem. I weselił się tam Saul, i wszyscy mężowie Izraelscy bardzo.
Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.

< I Samuela 11 >