< I Samuela 10 >

1 Tedy Samuel wziął bańkę oliwy, i wylał na głowę jego, a pocałowawszy go, rzekł: Izali cię nie pomazał Pan nad dziedzictwem swojem za wodza?
Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
2 Gdy dziś odejdziesz ode mnie, znajdziesz dwóch mężów u grobu Racheli, na granicach Benjamin w Selsa, którzyć powiedzą: Nalazły się oślice, którycheś chodził szukać, a oto zaniechawszy ojciec twój starania o oślicach, frasuje się o was, mówiąc; Cóż mam czynić z strony syna mego?
Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
3 Potem odszedłszy stamtąd dalej przyjdziesz aż na pole Tabor; i spotkają cię tam trzej mężowie idący do Boga, do domu Bożego, jeden niesie troje koźląt, a drugi niesie trzy bochny chleba, a trzeci niesie łagiew wina;
“Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
4 I pozdrowią cię w pokoju, i dadząć dwa chleby, które weźmiesz z ręk ich.
Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
5 Potem przyjdziesz na pagórek Boży, kędy jest straż Filistyńska; a gdy tam wnijdziesz do miasta, spotkasz się z gromadą proroków zstępujących z góry, a przed nimi będzie harfa, i bęben, i piszczałka, i lutnia, a oni będą prorokowali.
“Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
6 I zstąpi na cię Duch Pański, i będziesz z nimi prorokował, a odmienisz się w inszego męża.
Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
7 A gdy przyjdą te znaki na cię, czyń cokolwiek znajdzie ręka twoja: bo Bóg jest z tobą.
Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
8 Potem pójdziesz przedemną do Galgal, a oto, ja przyjdę do ciebie dla sprawowania ofiar całopalnych, i dla ofiarowania ofiar spokojnych; przez siedm dni będziesz czekał, aż przyjdę do ciebie i ukażęć, co będziesz miał czynić.
“Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
9 I stało się, gdy się obrócił, aby odszedł od Samuela, odmienił Bóg serce jego w insze; i spełniły się wszystkie one znaki dnia onego.
Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
10 I przyszli tam na pagórek, a oto, gromada proroków spotkała się z nim, i odpoczął na nim Duch Boży, i prorokował w pośrodku nich.
Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
11 Stało się tedy, że wszyscy, którzy go przedtem znali, ujrzeli, a oto, z prorokami prorokował; i mówili wszyscy jeden do drugiego: Cóż się stało synowi Cysowemu? Izali też Saul między prorokami?
Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
12 I odpowiedział mąż niektóry stamtąd, i rzekł: I któż jest ojcem ich? przetoż weszło to w przypowieść: Izali i Saul między prorokami?
Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
13 I przestał prorokować, a przyszedł na górę.
Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
14 Potem rzekł stryj Saula do niego, i do sługi jego: Gdzieżeście chodzili? I odpowiedział: Szukać oślic; a widząc, żeśmy ich nie mogli znaleść, poszliśmy do Samuela.
Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
15 I rzekł stryj Saula: Powiedz mi proszę, co wam powiedział Samuel.
Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
16 I odpowiedział Saul stryjowi swemu: Oznajmił nam za pewne, iż znaleziono oślice; ale o sprawie królestwa, o którem mu Samuel powiedział, nie oznajmił mu.
Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
17 Potem zwołał Samuel ludu do Pana do Masfa,
Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
18 I rzekł do synów Izraelskich: Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Jam wywiódł Izraela z Egiptu, i wybawiłem was z rąk Egipczanów, i z rąk wszystkich królestw, które was trapiły;
Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
19 Aleście wy dziś odrzucili Boga waszego, który was sam wybawia od wszystkiego złego waszego, i od ucisków waszych, i rzekliście mu: Postanów króla nad nami. Przetoż teraz stańcie przed Panem według pokoleń waszych, i wedle tysiąców waszych.
Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
20 A gdy kazał przystąpić Samuel wszystkim pokoleniom Izraelskim, padł los na pokolenie Benjaminowe.
Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
21 Potem kazał przystąpić pokoleniu Benjaminowemu według domów jego, i padł los na dom Metry, a trafił na Saula, syna Cysowego; i szukano go, ale go nie znaleziono.
Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
22 Przetoż pytali się znowu Pana: Przyjdzieli jeszcze sam ten mąż? I odpowiedział Pan: Oto się skrył między sprzętem.
Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
23 Tedy poszedłszy wzięli go stamtąd. I stanął w pośród ludu, i był głową wyższy nad wszystek lud.
Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
24 I rzekł Samuel do wszystkiego ludu: Widzicież, kogo to Pan obrał, że mu niemasz równego między wszystkim ludem? przetoż zakrzyknął wszystek lud, mówiąc: Niech żyje król!
Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
25 Tedy powiedział Samuel ludowi prawo królewskie, i spisał je na księgach, które położył przed Panem. Potem rozpuścił Samuel wszystek lud, każdego do domu swego.
Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
26 Także i Saul szedł do domu swego do Gabaa, i szły za nim wojska, których Bóg serca dotknął.
Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
27 Lecz ludzie niepobożni rzekli: Cóż, tenże nas wybawi? I wzgardzili nim, ani mu przynieśli darów; ale on czynił, jakoby nie słyszał.
Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.

< I Samuela 10 >