< I Królewska 5 >

1 I posłał Hiram, król Tyrski, sługi swe do Salomona, bo usłyszał, że go pomazano za króla miasto ojca jego; albowiem miłował Hiram Dawida po wszystkie dni.
Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse.
2 Salomon też zaś posłał do Hirama, mówiąc:
Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:
3 Ty wiesz, że Dawid, ojciec mój, nie mógł budować domu imieniowi Pana, Boga swego, dla wojen, które go były ogarnęły, aż nieprzyjacioły podał Pan pod stopy nóg jego;
“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo.
4 Ale teraz Pan, Bóg mój, dał mi odpoczynienie zewsząd, i niemam żadnego przeciwnika, ani zabiegu złego.
Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse.
5 A otom umyślił budować dom imieniowi Pana, Boga mego, jako powiedział Pan do Dawida, ojca mego, mówiąc: Syn twój, któremu dam miasto ciebie osiąść stolicę twoję, ten zbuduje dom ten imieniowi memu.
Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’
6 Przetoż teraz rozkaż, aby mi narąbano ceder na Libanie, a słudzy moi będą z sługami twoimi, a zapłatę sług twoich dam tobie tak, jako rzeczesz; albowiem ty wiesz, że niemasz między nami męża, któryby umiał tak rąbać drzewo, jako Sydończycy.
“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”
7 A gdy usłyszał Hiram słowa Salomonowe, uradował się bardzo i rzekł: Błogosławiony Pan dzisiaj, który dał Dawidowi syna mądrego nad tym ludem wielkim.
Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”
8 I posłał Hiram do Salomona, mówiąc: Słyszałem z czemeś posłał do mnie. Uczynię wszystkę wolą twoję około drzewa cedrowego, i około drzewa jodłowego.
Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni: “Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini.
9 Słudzy moi zwiozą je z Libanu do morza, a ja je każę złożyć w tratwy, i spuścić morzem aż do miejsca, o którem mi dasz znać, i tam je rozwiążę, a ty je pobierzesz. Ty też uczynisz wolą moję, a dasz obrok czeladzi mojej.
Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”
10 A tak Hiram dodawał Salomonowi drzewa cedrowego, i drzewa jodłowego, jako wiele chciał.
Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna,
11 Salomon także dawał Hiramowi dwadzieścia tysięcy miar pszenicy na żywność czeladzi jego, i dwadzieścia tysięcy miar oliwy wybijanej; to dawał Salomon Hiramowi na każdy rok.
ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka.
12 A Pan dał mądrość Salomonowi, jako mu był obiecał, i był pokój między Hiramem i między Salomonem, a uczynili przymierze między sobą.
Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.
13 Tedy kazał wybierać król Salomon robotniki ze wszystkiego Izraela, a było wybranych trzydzieści tysięcy mężów.
Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000.
14 Które słał do Libanu po dziesięć tysięcy na każdy miesiąc, na przemiany; po miesiącu mieszkali na Libanie, a po dwa miesiące w domu swym; a Adoniram był przełożony nad tymi wybranymi.
Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo.
15 Miał też Salomon siedmdziesiąt tysięcy tych, którzy nosili ciężary, a ośmdziesiąt tysięcy tych, którzy rąbali na górze;
Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri,
16 Oprócz przedniejszych urzędników Salomonowych, których było nad robotą trzy tysiące i trzy sta, którzy byli przełożeni nad ludem odprawującym robotę.
ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina.
17 Rozkazał też król, aby wożono kamienie wielkie, kamienie drogie, i kamienie ciosane, na założenie gruntów domu.
Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu.
18 Ciosali tedy rzemieślnicy Salomonowi, i rzemieślnicy Hiramowi, i Gimblimczycy. A tak gotowali drzewo i kamienie na budowanie domu.
Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.

< I Królewska 5 >