< I Królewska 18 >

1 Potem po wielu dniach, mianowicie po onym roku trzecim, stało się słowo Pańskie do Elijasza, mówiąc: Idź, ukaż się Achabowi; bo spuszczę deszcz na ziemię.
Patapita masiku ambiri, mʼchaka chachitatu cha chilala, Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, “Pita ukadzionetse kwa Ahabu ndipo ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi.”
2 Szedł tedy Elijasz, aby się ukazał Achabowi; a był głód gwałtowny w Samaryi.
Choncho Eliya anapita kukadzionetsa kwa Ahabu. Tsono nthawi imeneyi njala inakula kwambiri mu Samariya,
3 I zawołał Achab Abdyjasza, który był sprawcą domu jego. (A Abdyjasz się bardzo Pana bał;
ndipo Ahabu anayitana Obadiya amene ankayangʼanira nyumba yake yaufumu. (Obadiya ankaopa Yehova kwambiri.
4 Bo gdy mordowała Jezabel proroki Pańskie, tedy wziął Abdyjasz sto proroków, i skrył ich po pięćdziesiąt do jaskini, i żywił je chlebem i wodą.)
Pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova, Obadiya anatenga aneneri 100 ndi kuwabisa mʼmapanga awiri, phanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ankawapatsa chakudya ndi madzi).
5 I rzekł Achab do Abdyjasza: Idź przez ziemię do wszystkich źródeł wód, i do wszystkich potoków, aza gdzie znajdziemy trawę, żebyśmy żywo zachowali konie i muły, i żebyśmy nie zgubili bydła.
Ahabu anawuza Obadiya kuti, “Pita mʼdziko kulikonse kumene kuli zitsime za madzi ndi ku zigwa zonse. Mwina mwake tingapeze udzu oti nʼkumadyetsa akavalo ndi abulu kuti akhale ndi moyo, kuti tisaphe chiweto chilichonse.”
6 I rozdzielili sobie ziemię, którą przejść mieli. Achab sam szedł jedną drogą, Abdyjasz też szedł drugą drogą osobno.
Choncho anagawana dziko loti apiteko, Ahabu anapita mbali ina, Obadiya nʼkupita ina.
7 A gdy Abdyjasz był w drodze, oto się z nim Elijasz spotkał, który gdy go poznał, upadł na oblicze swoje, i rzekł: A tyżeś jest pan mój Elijasz?
Obadiya akuyenda mʼnjira anakumana ndi Eliya. Ndipo taonani, Obadiya anamuzindikira Eliyayo, naweramira pansi ndipo anati, “Kodi ndinu, mbuye wanga Eliya?”
8 I odpowiedział mu: Jam jest. Idź, powiedz panu twemu: Oto Elijasz tu jest.
Eliya anayankha kuti, “Inde. Pita kawuze mbuye wako kuti, ‘Eliya wabwera.’”
9 Do którego on rzekł: Cóżem zgrzeszył, iż wydawasz sługę twego w ręce Achabowe, aby mię zabił?
Obadiya anafunsa kuti, “Kodi ndalakwa chiyani kuti inu mupereke mtumiki wanu kwa Ahabu kuti akaphedwe?
10 Jako żywy Pan, Bóg twój, że niemasz narodu, i królestwa, gdzieby nie posłał Pan mój, aby cię szukano; a gdy powiedziano, iż cię niemasz, tedy obowiązał przysięgą królestwa i narody, jako cię znaleść nie mogą.
Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, kulibe mtundu wa anthu kapena ufumu uliwonse kumene mbuye wanga sanatumeko anthu okakufunafunani. Ndipo pamene mtundu wa anthu kapena ufumu unena kuti kuno kulibe, Ahabu ankawalumbiritsa kuti atsimikizedi kuti inuyo kulibe kumeneko.
11 A ty mi teraz mówisz: Idź, a powiedz panu twemu: Oto Elijasz.
Koma tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’
12 I stałoby się, gdybym ja odszedł od ciebie, żeby cię Duch Pański zaniósł, gdziebym nie wiedział; a ja szedłszy opowiedziałbym Achabowi, a gdyby cię nie znalazł, zabiłby mię; a sługa twój boi się Pana od dzieciństwa swego.
Ine sindikudziwa kumene Mzimu wa Yehova udzakupititsani ine ndikachoka. Ngati ndipita kukamuwuza Ahabu ndipo iye wosadzakupezani, adzandipha. Komatu ine mtumiki wanu ndakhala ndi kupembedza Yehova kuyambira ubwana wanga.
13 Azaż nie powiedziano panu memu, com uczynił, gdy mordowała Jezabel proroki Pańskie? żem skrył z proroków Pańskich sto mężów, po pięćdziesiąt mężów w jaskini, i żywiłem je chlebem i wodą?
Mbuye wanga, kodi simunamve zimene ndinachita pamene Yezebeli ankapha aneneri a Yehova? Ine ndinabisa aneneri 100 a Yehova mʼmapanga awiri, mʼphanga lililonse aneneri makumi asanu, ndipo ndinkawapatsa chakudya ndi madzi akumwa.
14 A ty teraz mówisz: Idź, powiedz panu twemu: Oto Elijasz; i zabije mię.
Ndiye inu tsopano mukundiwuza kuti ndipite kwa mbuye wanga ndi kukanena kuti, ‘Eliya wabwera.’ Iyeyo adzandipha ndithu!”
15 I odpowiedział Elijasz: Jako żywy Pan zastępów, przed którego oblicznością stoję, że mu się dziś ukażę.
Eliya anati, “Pali Yehova Wamphamvuzonse wamoyo, amene ndimamutumikira, ine lero ndidzaonekera ndithu pamaso pa Ahabu.”
16 A tak szedł Abdyjasz przeciw Achabowi, i oznajmił mu to. Przetoż szedł Achab przeciw Elijaszowi.
Choncho Obadiya anapita kukakumana ndi Ahabu, namuwuza, ndipo Ahabu anapita kukakumana ndi Eliya.
17 A ujrzawszy Achab Elijasza, rzekł Achab do niego: Azaż nie ty jesteś, który czynisz zamięszanie w Izraelu?
Pamene Ahabu anaona Eliya, anati kwa iye, “Kodi ndiwedi, munthu wovutitsa Israeli uja?”
18 Na co mu odpowiedział: Nie jać czynię zamięszanie w Izraelu, ale ty i dom ojca twego, gdyż opuściwszy rozkazania Pańskie naśladujecie Baalów.
Eliya anayankha kuti, “Ine sindinavutitse Israeli, koma ndinuyo ndi banja lanu. Mwasiya malamulo a Yehova ndipo mwatsatira Abaala.
19 Przetoż teraz poślij, a zbierz do mnie wszystkiego Izraela na górę Karmel, i proroków Baalowych cztery sta i pięćdziesiąt, przytem proroków gajowych cztery sta, którzy jadają z stołu Jezabeli.
Tsopano sonkhanitsani anthu a mʼdziko lonse la Israeli kuti akumane nane pa Phiri la Karimeli. Ndipo mubwere nawo aneneri a Baala 450 ndi aneneri a fano la Asera 400, amene amadya pa tebulo la Yezebeli.”
20 Posłał tedy Achab do wszystkich synów Izraelskich, i zebrał te proroki na górę Karmel.
Choncho Ahabu anatumiza mawu mʼdziko lonse la Israeli, ndipo anasonkhanitsa aneneri a Baala ku Phiri la Karimeli.
21 A przystąpiwszy Elijasz do wszystkiego ludu, rzekł: I długoż będziecie chramać na obie strony? Jeźli Pan jest Bogiem, idźcież za nim; a jeźli Baal, idźcież za nim. I nie odpowiedział mu lud i słowa.
Eliya anapita patsogolo pa anthuwo ndipo anati, “Kodi mudzakhala anthu a mitima iwiri mpaka liti? Ngati Yehova ndi Mulungu, mutsateni; koma ngati Baala ndi Mulungu, mutsateni.” Koma anthu aja sanayankhe.
22 Tedy rzekł Elijasz do ludu: Jam tylko sam został prorok Pański; a proroków Baalowych cztery sta i pięćdziesiąt mężów.
Pamenepo Eliya ananena kwa iwo kuti, “Ine ndilipo ndekha mneneri wa Yehova, koma Baala ali ndi aneneri 450.
23 Niech nam dadzą dwóch cielców, a niech sobie obiorą cielca jednego, a porąbią go na sztuki, i włożą na drwa; ale ognia niech nie podkładają: ja też przygotuję drugiego cielca, którego włożę na drwa, a ognia nie podłożę.
Tibweretsereni ngʼombe zazimuna ziwiri. Iwo asankhepo okha ngʼombe imodzi, ndipo ayidule nthulinthuli ndi kuziyika pa nkhuni nthulizo, koma osakolezapo moto. Ndipo ine ndidzadula nthulinthuli ngʼombe inayo ndi kuyika pa nkhuni koma sindikolezapo moto.
24 Potem wzywajcie imienia bogów waszych, a ja będę wzywał imienia Pańskiego, a Bóg, który się ozwie przez ogień, ten niech będzie Bogiem. Na co odpowiadając wszystek lud rzekł: Dobrześ powiedział.
Kenaka inu muyitane dzina la mulungu wanu, ndipo ine ndidzayitana dzina la Yehova. Mulungu amene ati ayankhe potumiza moto, iyeyo ndiye Mulungu.” Pamenepo anthu onse anati, “Izi mwanena zamveka bwino.”
25 I rzekł Elijasz do proroków Baalowych: Obierzcie sobie cielca jednego, a zgotujcie go pierwej, bo was jest więcej; wzywajcież imienia bogów waszych, ale ognia nie podkładajcie.
Eliya anawuza aneneri a Baala kuti, “Yambani ndinu. Sankhani ngʼombe yayimuna imodzi, muyikonze, popeza mulipo ambiri. Muyitane dzina la mulungu wanu, koma musakoleze moto.”
26 A tak wzięli cielca, którego im dał, a zgotowawszy wzywali imienia Baalowego od poranku aż do południa, mówiąc: O Baalu, wysłuchaj nas! Ale nie było głosu, ani ktoby odpowiedział. I skakali koło ołtarza, który byli uczynili.
Choncho iwo anatenga ngʼombe yayimunayo imene anawapatsa, nayikonza. Kenaka anayitana dzina la Baala kuyambira mmawa mpaka masana. Iwo anafuwula kuti, “Inu Baala, tiyankheni ife.” Koma panalibe yankho; palibe amene anayankha. Ndipo anavinavina mozungulira guwa lansembe limene anapanga.
27 A gdy było południe, naśmiewał się z nich Elijasz, mówiąc: Wołajcie większym głosem, ponieważ jest bóg; tylko że się albo zamyślił, albo jest zabawny, albo też jest w drodze; albo też śpi, aza ocuci.
Nthawi yamasana Eliya anayamba kuwanyogodola ndipo anati, “Fuwulani kwambiri. Ndithudi, iye ndi mulungu! Mwinatu akulingalira kwambiri, kapena watanganidwa, kapena ali paulendo. Mwina wagona ndipo nʼkofunika kuti adzutsidwe.”
28 A tak wołali głosem wielkim, i rzezali się według zwyczaju swego nożami i włóczenkami, aż się krwią oblewali.
Choncho iwo anafuwula kwambiri ndi kudzichekacheka ndi malupanga ndi mikondo, potsata miyambo yawo, mpaka kutuluka magazi.
29 I stało się, gdy minęło południe, że prorokowali aż do czasu ofiarowania ofiary śniednej; ale nie było głosu, ani ktoby odpowiedział, ani ktoby wysłuchał.
Nthawi yamasana inadutsa, ndipo anapitiriza kunenera mwakhama mpaka nthawi yopereka nsembe ya madzulo. Koma panalibe yankho. Palibe amene anayankha, kapena kulabadira zimenezo.
30 Zatem rzekł Elijasz do wszystkiego ludu: Przystąpcie do mnie. I przystąpił wszystek lud do niego. Tedy naprawił ołtarz Pański, który był rozwalony.
Pamenepo Eliya anati kwa anthu onse, “Senderani pafupi ndi ine.” Ndipo anthu onsewo anasendera pafupi ndi iye, ndipo iye anakonza guwa lansembe la Yehova limene linali litawonongeka.
31 Albowiem wziął Elijasz dwanaście kamieni; (według liczby pokolenia synów Jakóbowych, do którego się stało słowo Pańskie, mówiąc: Izrael będzie imię twoje.)
Eliya anatenga miyala 12, mwala uliwonse kuyimira fuko lililonse la Yakobo, amene Yehova anamuwuza kuti, “Dzina lako lidzakhala Israeli.”
32 I zbudował z tego kamienia ołtarz w imię Pańskie, a uczynił około ołtarza szeroki rów, coby mógł dwie miary zboża wysiać.
Ndi miyala imeneyo anamanga guwa mʼdzina la Yehova, ndipo anakumba ngalande yayikulu yolowa malita 15 a madzi kuzungulira guwalo.
33 Potem ułożył drwa, i na sztuki porąbał cielca, i kładł go na drwa.
Anayika nkhuni zija mʼmalo mwake nadula nthulinthuli ngʼombe yayimuna ija ndi kuyika nthulizo pa nkhunipo. Pamenepo Eliya anati, “Dzazani mitsuko inayi ndi madzi ndipo muwathire pa nyama ya nsembeyo ndi nkhunizo.”
34 I rzekł: Napełnijcie cztery wiadra wodą, a wylijcie na całopalenie i na drwa. Rzekł nadto: Powtórzcie, i powtórzyli; rzekł jeszcze: Uczyńcie po trzecie, i uczynili po trzecie,
Eliya anati, “Thiraninso kachiwiri.” Anthu aja anathiranso madziwo kachiwiri. Iye analamula kuti, “Thiraninso kachitatu.” Ndipo iwo anathiranso kachitatu.
35 Tak że płynęły wody około ołtarza, aż i rów był napełniony wodą.
Madziwo anayenderera pansi kuzungulira guwa lansembe, nadzaza ngalande yonse.
36 I stało się, gdy był czas sprawowania ofiary śniednej, przystąpił Elijasz prorok, i rzekł: Panie, Boże Abrahama, Izaaka, i Izraela! dziś niech poznają, żeś ty jest Bogiem w Izraelu, a jam sługa twój, a żem według słowa twego uczynił to wszystko.
Pa nthawi yopereka nsembe, mneneri Eliya anasendera pafupi ndi guwa lansembe, napemphera kuti, “Inu Yehova, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, lero zidziwike kuti ndinu Mulungu mu Israeli ndipo kuti ine ndine mtumiki wanu, kuti ine ndachita zonsezi chifukwa mwalamula ndinu.
37 Wysłuchaj mię Panie, wysłuchaj mię, aby poznał ten lud, żeś ty Panie jest Bogiem, gdybyś zaś nawrócił serca ich.
Ndiyankheni, Inu Yehova, ndiyankheni, kuti anthu awa adziwe Inu Yehova, kuti ndinu Mulungu, ndipo kuti mutembenuziranso mitima yawo kwa Inu.”
38 Tedy spadł ogień Pański, i pożarł całopalenie, i drwa, i kamienie, i proch; a wodę, która była w rowie, wysuszył.
Pamenepo moto wa Yehova unagwa, nunyeketsa nsembe yopserezayo, nkhuni, miyala ndi dothi lomwe. Unawumitsanso madzi amene anali mʼngalande.
39 Co gdy ujrzał wszystek lud, upadli na oblicze swe, i rzekli: Pan jest Bogiem, Panci jest Bogiem.
Anthu onse ataona zimenezi, anaweramitsa nkhope zawo pansi, nafuwula kuti, “Yehova ndiye Mulungu! Yehova ndiye Mulungu!”
40 Tedy rzekł Elijasz do nich: Pojmajcie proroki Baalowe, a żaden niech z nich nie uchodzi. I pojmano je. A tak odwiódł je Elijasz do potoku Cyson, i tamże je pobił.
Pamenepo Eliya analamula anthuwo kuti, “Gwirani aneneri a Baala. Musalole kuti wina aliyense athawe!” Anagwira onsewo ndipo Eliya anabwera nawo ku Chigwa cha Kisoni, nawapha kumeneko.
41 Potem rzekł Elijasz do Achaba: Idź, jedz, a pij; albowiem oto szum dżdżu wielkiego.
Ndipo Eliya anati kwa Ahabu, “Pitani, kadyeni ndi kumwa, pakuti kukumveka mkokomo wa mvula.”
42 Tedy szedł Achab, aby jadł i pił; a Elijasz wstąpił na wierzch Karmelu, i położył się na ziemię, a włożył twarz swoję między kolana swoje.
Choncho Ahabu anapita kukadya ndi kumwa, koma Eliya anakwera pamwamba pa Phiri la Karimeli, ndipo anawerama mpaka pansi, nayika mutu wake pakati pa mawondo ake.
43 Potem rzekł do sługi swego: Idź teraz, a spojrzyj ku morzu. Który poszedł, a spojrzawszy rzekł: Niemasz nic. Zasię rzekł: Idź, a wracaj się po siedm kroć.
Eliya anawuza mtumiki wake kuti, “Pita kayangʼane ku nyanja.” Ndipo iye anapita nakayangʼana. Mtumikiyo anati, “Kulibe kanthu.” Kasanu nʼkawiri Eliya anati, “Pitanso.”
44 A za siódmym razem rzekł: Oto obłok mały jako dłoń człowiecza występuje z morza. Tedy on rzekł: Idź, a powiedz Achabowi: Zaprzęgaj, a ujeżdżaj, aby cię deszcz nie zastał.
Ulendo wachisanu ndi chiwiri mtumikiyo anafotokoza kuti, “Taonani, kamtambo kakangʼono kokhala ngati dzanja la munthu kakutuluka ku nyanja.” Pamenepo Eliya anati, “Pita, kamuwuze Ahabu kuti, ‘Konzani galeta lanu ndipo mutsike mvula isanakutsekerezeni.’”
45 I stało się między tem, że się niebiosa obłokami i wiatrem zaćmiły, skąd był deszcz wielki. A tak wsiadłszy Achab, jechał do Jezreela.
Nthawi imeneyi nʼkuti kuthambo kutayamba kusonkhana mitambo yakuda, mphepo inawomba, mvula yamphamvu inagwa ndipo Ahabu anakwera galeta napita ku Yezireeli.
46 A ręka Pańska była nad Elijaszem; i przepasał biodra swe, i bieżał przed Achabem, aż przyszedł do Jezreela.
Dzanja la Yehova linali pa Eliya ndipo atamangira lamba chovala chake, anathamanga ndi kumupitirira Ahabu mpaka kukhala woyamba kukafika ku Yezireeli.

< I Królewska 18 >