< I Królewska 14 >

1 Tegoż czasu rozniemógł się Abijas, syn Jeroboama.
Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
2 I rzekł Jeroboam do żony swej: Wstań teraz, a odmień się, aby nie poznano, żeś ty żoną Jeroboamową, a idź do Sylo; oto tam jest Achyjasz prorok, który mi powiedział, żem miał zostać królem nad tym ludem.
ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 A wziąwszy z sobą dziesięcioro chleba, i placków, i faskę miodu, idź do niego; on ci oznajmi, co się stanie dziecięciu.
Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
4 I uczyniła tak żona Jeroboamowa, a wstawszy poszła do Sylo, i weszła do domu Achyjaszowego; ale Achyjasz nie mógł już widzieć, bo mu były zaszły oczy dla starości jego.
Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
5 A Pan rzekł do Achyjasza: Oto żona Jeroboamowa wchodzi, aby się od ciebie czego wywiedziała o synu swym, przeto że choruje; ale tak a tak rzeczesz jej, a stanie się, gdy będzie wchodziła, zmyśli się być inszą.
Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
6 Przetoż gdy usłyszał Achyjasz tupanie nóg jej, wchodzącej we drzwi, rzekł: Wnijdź żono Jeroboamowa; przecz się zmyślasz być inszą? Jam bowiem srogim posłem do ciebie.
Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
7 Idź, powiedz Jeroboamowi: Tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Ponieważem cię wywyższył z pośrodku ludu, a postanowiłem cię książęciem nad ludem moim Izraelskim;
Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
8 I oderwałem królestwo od domu Dawidowego, a dałem je tobie, tyś jednak nie był jako sługa mój Dawid, który strzegł rozkazania mego, i który chodził za mną całem sercem swojem, to tylko czyniąc, co jest dobrego w oczach moich;
Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
9 Aleś czynił złe nad wszystkie, którzy byli przed tobą; albowiem odszedłszy, poczyniłeś sobie bogi cudze, i lane, abyś mię pobudził do gniewu, a mnieś zarzucił w tył sobie:
Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
10 Przetoż oto Ja przywiodę złe na dom Jeroboamowy, i wytracę z Jeroboama aż do najmniejszego szczenięcia, więźnia, i opuszczonego w Izraelu, i wymiotę ostatki domu Jeroboamowego, jako wymiatają gnój, aż do czysta.
“‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
11 Tego, który z domu Jeroboamowego umrze w mieście, zjedzą psy, a który umrze na polu, zjedzą ptaki powietrzne, ponieważ Pan wyrzekł.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
12 A ty wstawszy idź do domu twego a gdy wchodzić będziesz do miasta, tedy umrze dziecię.
“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
13 I będzie go płakał wszystek Izrael, i pochowają go; bo ten sam z domu Jeroboamowego wnijdzie do grobu, przeto iż się znalazło o nim samym słowo dobre od Pana, Boga Izraelskiego w domu Jeroboamowym.
Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
14 Wszakże postanowi sobie Pan króla nad Izraelem, który wykorzeni dom Jeroboamowy dnia tego; a co mówię, wzbudzi? I owszem już wzbudził.
“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
15 I uderzy Pan Izraela, i zachwieje nim, jako się chwieje trzcina na wodach, a wykorzeni Izraela z ziemi tej dobrej, którą dał ojcom ich, i rozproszy je za rzekę, przeto iż sobie poczynili gaje, wzruszając Pana ku gniewu.
Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
16 A tak wyda Izraela dla grzechu Jeroboamowego, który grzeszył, i który do grzechu przywiódł Izraela.
Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
17 Tedy wstała żona Jeroboamowa, i poszła, a przyszła do Tersa; a gdy wstępowała na próg domu, umarło dziecię.
Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
18 I pochowali je, a płakał go wszystek Izrael według słowa Pańskiego, które opowiedział przez sługę swego Achyjasza proroka.
Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
19 A inne sprawy Jeroboamowe, jako walczył, i jako królował, oto spisane są w kronikach o królach Izraelskich.
Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
20 A dni, których królował Jeroboam, było dwadzieścia i dwa lat, i zasnął z ojcy swymi, a Nadab, syn jego, królował miasto niego.
Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 Roboam też, syn Salomona, królował w Judzie. A było Roboamowi czterdzieści lat i jeden, gdy począł królować, a siedmnaście lat królował w mieście Jeruzalemie, które Pan obrał ze wszystkich pokoleń Izraelskich, aby tam przebywało imię jego. A imię matki jego było Naama, Ammonitka.
Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
22 I czynił Juda złe przed Panem, a wzruszyli go ku gniewu grzechami swemi, któremi grzeszyli nad wszystko, co czynili ojcowie ich.
Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
23 Albowiem i oni pobudowali sobie wyżyny, i słupy, i gaje na każdym pagórku wysokim, i pod każdem drzewem zielonem.
Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
24 Byli też i Sodomczycy w onej ziemi, sprawujący się według wszystkich obrzydliwości poganów, które wyrzucił Pan od obliczności synów Izraelskich.
Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
25 I stało się roku piątego królowania Roboama, że wyciągnął Sesak, król Egipski, przeciw Jeruzalemowi.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
26 I pobrał skarby domu Pańskiego, i skarby domu królewskiego, wszystko to pobrał; wziął też wszystkie tarcze złote, które był sprawił Salomon;
Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
27 Miasto których król Roboam sprawił tarcze miedziane, i poruczył je przełożonym nad piechotą, którzy strzegli drzwi domu królewskiego.
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
28 A gdy wchodził król do domu Pańskiego, brała je piechota, i zasię odnosiła do komor swoich.
Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
29 A inne sprawy Roboamowe, i wszystko co czynił, azaż nie są napisane w kronikach o królach Judzkich?
Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
30 I była wojna między Roboamem i między Jeroboamem po wszystkie dni.
Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
31 I zasnął Roboam z ojcy swymi, a pochowany jest z nimi w mieście Dawidowem; a imię matki jego było Naama, Ammonitka. I królował Abijam, syn jego, miasto niego.
Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.

< I Królewska 14 >