< I Królewska 11 >

1 Tedy król Salomon rozmiłował się niewiast obcych wiele: nie tylko córki Faraonowej, ale i Moabitczanek, Ammonitczanek, Edomczanek, Sydończanek, Hetejczanek.
Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti.
2 Z tych narodów, o których powiedział Pan synom Izraelskim: Nie wchodźcie do nich, i one niech nie wchodzą do was; albowiem nakłoniłyby serce wasze za bogi swymi. Do tych przylgnął Salomon miłością.
Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa.
3 Tak iż miał żon królowych siedm set, a założnic trzy sta; i odwróciły żony jego serce jego.
Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa.
4 I stało się, gdy już był Salomon stary, że żony jego nakłoniły serce jego za bogi cudzymi, tak iż nie było serce jego zupełne z Panem, Bogiem jego, jako serce Dawida, ojca jego.
Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake.
5 Ale udał się Salomon za Astarotą, boginią Sydońską, i za Molochem, obrzydliwością Ammonitów.
Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni.
6 I uczynił Salomon, co się nie podobało Panu, ani chodził doskonale za Panem, jako Dawid, ojciec jego.
Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.
7 Tedy zbudował Salomon kaplicę Chamosowi, obrzydliwości Moabskiej, na górze przeciw Jeruzalemowi i Molochowi, obrzydliwości synów Ammonowych.
Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni.
8 I tak uczynił wszystkim żonom swym cudzoziemkom, które kadziły, i ofiarowały bogom swoim.
Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.
9 I rozgniewał się Pan na Salomona, że się odwróciło serce jego od Pana, Boga Izraelskiego, który się mu był ukazał po dwa kroć.
Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse.
10 I zakazał mu tego, aby nie chodził za bogi cudzymi; wszakże nie strzegł tego, co Pan przykazał.
Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova.
11 Przetoż rzekł Pan do Salomona: Ponieważeś się tego dopuścił, nie strzegąc przymierza mego, ani wyroków moich, którem ci przykazał, pewnie oderwę królestwo od ciebie, a dam je słudze twojemu,
Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako.
12 Wszakże za dni twoich nie uczynię tego dla Dawida, ojca twego; ale z ręki syna twego oderwę je.
Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako.
13 Lecz wszystkiego królestwa nie oderwę; pokolenie jedno dam synowi twemu dla Dawida, sługi mego, i dla Jeruzalemu, którem obrał.
Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”
14 Przetoż wzbudził Pan przeciwnika Salomonowi, Adada Edomczyka z nasienia królewskiego, który był w Edom.
Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu.
15 Albowiem stało się, gdy Dawid był w Edom, a Joab, hetman wojska, wyjechał, aby pochował pobite, i pobił wszystkie mężczyzny w Edom;
Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu.
16 (Bo tam sześć miesięcy mieszkał Joab ze wszystkimi Izraelczykami, aż wytracił wszystkie mężczyzny w Edom.)
Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu.
17 Tedy uciekł Adad sam, i niektórzy mężowie Edomscy z sług ojca jego z nim, aby szli do Egiptu; a Adad był chłopcem nie wielkim.
Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake.
18 Którzy wyszedłszy z Madyjan przyszli do Faran, a wziąwszy z sobą niektóre męże z Faran weszli do Egiptu, do Faraona króla Egipskiego, który mu dał dom, i żywność mu naznaczył, dał mu też i ziemię.
Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.
19 I znalazł Adad wielką łaskę w oczach Faraonowych, tak, iż mu dał za żonę siostrę żony swej, siostrę królowej Tafnes.
Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi.
20 I porodziła mu siostra Tafnes Gienubata, syna jego, którego odchowała Tafnes w domu Faraonowym. I był Gienubat w domu Faraonowym między syny Faraonowymi.
Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.
21 A gdy usłyszał Adad w Egipcie, iż zasnął Dawid z ojcy swymi, a iż umarł Joab, hetman wojska, tedy rzekł Adad do Faraona: Puść mię, że pójdę do ziemi mojej.
Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”
22 Któremu odpowiedział Farao: Czegoż ci niedostawa u mnie, że chcesz iść do ziemi twojej? A on rzekł: Niczego; a wszakże puść mię.
Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?” Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”
23 Wzbudził także Bóg nań przeciwnika, Rezona, syna Elijadowego, który był uciekł od Adarezera, króla Soby, Pana swego.
Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba.
24 A zebrawszy do siebie męże, był książęciem roty, gdy je Dawid mordował; przetoż odszedłszy do Damaszku, mieszkali w nim, a królowali nad Damaszkiem.
Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira.
25 I był przeciwnikiem Izraelowi po wszystkie dni Salomonowe, a to oprócz szkód, które mu czynił Adad; bo się brzydził Izraelem, gdy królował w Syryi.
Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.
26 Jeroboam też, syn Nabata Efratejczyka z Saredy, (a imię matki jego Serwa, która była wdową, ) sługa Salomonowy, podniósł przeciwko królowi rękę.
Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.
27 A tać była przyczyna, dla której podniósł rękę swą przeciwko królowi, że Salomon zbudowawszy Mello, zaprawił dziurę w mieście Dawida, ojca swego.
Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake.
28 A Jeroboam był mąż mocny i możny. Przetoż widząc Salomon młodzieńca, że był sprawny, postanowił go nad podatkami wszystkiemi domu Józefowego.
Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.
29 I stało się tegoż czasu, gdy Jeroboam wyszedł z Jeruzalemu, że go znalazł na drodze Achyjasz Sylonitczyk, prorok, będąc odziany płaszczem nowym; a tylko sami dwaj byli na polu.
Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko,
30 Tedy wziąwszy Achyjasz płaszcz nowy, który miał na sobie, rozdarł go na dwanaście sztuk.
ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12.
31 I rzekł do Jeroboama: Weźmij sobie dziesięć sztuk; bo tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Oto Ja oderwę królestwo z rąk Salomonowych, a dam tobie dziesięć pokoleń.
Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
32 Jedno tylko pokolenie zostanie mu dla sługi mego Dawida, i dla miasta Jeruzalem, którem obrał ze wszystkich pokoleń Izraelskich;
Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha.
33 Przeto, że mię opuścili, a kłaniali się Astarocie, bogini Sydońskiej, i Chamosowi, bogu Moabskiemu, i Molochowi, bogu synów Ammonowych, a nie chodzili drogami mojemi, aby czynili to, co się mnie podoba, ani też strzegli wyroków moich, i sądów mo ich, jako Dawid, ojciec jego.
Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.
34 Wszakże nie odejmę wszystkiego królestwa z ręki jego, owszem zostawię go książęciem po wszystkie dni żywota jego dla Dawida, sługi mego, któregom obrał, który strzegł rozkazania mego i wyroków moich.
“‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga.
35 Ale wziąwszy królestwo z ręki syna jego, dam tobie z niego dziesięć pokoleń:
Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi.
36 A synowi jego dam pokolenie jedno, aby została pochodnia Dawidowi, słudze memu, po wszystkie dni przedemną w mieście Jeruzalemie, którem sobie obrał, aby tam przebywało imię moje;
Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa.
37 A ciebie wezmę, abyś królował nad wszystkiem, czego żąda dusza twoja, a będziesz królem nad Izraelem.
Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli.
38 Przetoż jeźli będziesz słuchał wszystkiego, coć przykażę, a będziesz chodził drogami mojemi, czyniąc to, co dobrego jest w oczach moich, strzegąc wyroków moich, i przykazań moich, jako czynił Dawid, sługa mój: tedy będę z tobą, a zbudujęć dom mocny, jakom zbudował Dawidowi, i podam ci Izraela;
Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli.
39 I trapić będę nasienie Dawidowe dla tego; a wszakże nie po wszystkie dni.
Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’”
40 Przetoż Salomon chciał zabić Jaroboama; ale wstawszy Jeroboam uciekł do Egiptu, do Sesaka, króla Egipskiego, i był w Egipcie aż do śmierci Salomonowej.
Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.
41 A inne sprawy Salomonowe, którekolwiek czynił, i mądrość jego, izali nie są wypisane w księgach spraw Salomonowych?
Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni?
42 A dni, których królował Salomon w Jeruzalemie nad wszystkim Izraelem, było czterdzieści lat.
Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi.
43 I zasnął Salomon z ojcy swymi, a pogrzebiony jest w mieście Dawida, ojca swego; i królował Roboam, syn jego, miasto niego.
Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.

< I Królewska 11 >