< I Królewska 1 >

1 A gdy się król Dawid zstarzał, i zaszedł w lata, chodź go odziewano szatami, przecię się zagrzać nie mógł.
Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
2 I rzekli mu słudzy jego: Niech poszukają królowi, panu naszemu młodej panienki, któraby stawała przed królem, i opatrowała go, a sypiając na łonie jego, żeby zagrzewała króla, pana naszego.
Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
3 Szukali tedy panienki pięknej po wszystkich granicach Izraelskich, i znaleźli Abisag Sunamitkę, a przywiedli ją do króla.
Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
4 A ta panienka była bardzo piękna, i opatrowała króla, i służyła mu; ale jej król nie uznał.
Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
5 Lecz Adonijasz, syn Haggity, wynosił się, mówiąc: Ja będę królował. I nasprawiał sobie wozów i jezdnych, i pięćdziesiąt mężów, którzy biegali przed nim.
Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
6 A nie gromił go nigdy ojciec jego, mówiąc: Przeczżeś to uczynił? A był i ten bardzo pięknej urody, którego była porodziła Haggita po Absalomie.
(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
7 A miał zmowę z Joabem, synem Sarwii, i z Abijatarem kapłanem, którzy pomagali za Adonijaszem.
Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
8 Ale Sadok kapłan, i Banajas, syn Jojady, i Natan prorok, i Semej, i Rehy i rycerstwo Dawidowe, nie przestawali z Adonijaszem.
Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
9 Tedy nabił Adonijasz owiec, i wołów, i bydła tłustego u kamienia Zohelet, który był nad źródłem Rogiel, i wezwał wszystkich braci swych, synów królewskich, i wszystkich mężów z Juda, sług królewskich.
Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
10 Ale Natana proroka, i Banajasa, i innego rycerstwa, ani Salomona, brata swego, nie wezwał.
koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
11 Tedy rzekł Natan do Betsaby, matki Salomonowej, mówiąc: A nie słyszałaś, iż króluje Adonijasz, syn Haggity, a Dawid, pan nasz, nie wie o tem?
Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
12 Przetoż teraz pójdź proszę, dam ci radę, a zachowasz zdrowie twoje i zdrowie syna twego Salomona.
Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
13 Idź, a wnijdź do króla Dawida, i mów do niego: Izaliś ty królu, panie mój, nieprzysiągł służebnicy twojej, mówiąc: Salomon, syn twój, będzie królował po mnie, a on będzie siedział na stolicy mojej? Przeczże tedy króluje Adonijasz?
Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
14 A gdy ty jeszcze tam będziesz mówiła z królem, ja przyjdę za tobą, i dopełnię słów twoich.
Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
15 A tak weszła Betsaba do króla na pokój; a król się już był bardzo zstarzał, a Abisag Sunamitka posługowała królowi.
Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
16 Tedy nachyliwszy się Betsaba, pokłoniła się królowi, której rzekł król: Czego chcesz?
Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
17 A ona mu odpowiedziała: Panie mój, tyś przysiągł przez Pana, Boga twego, służebnicy twojej, że Salomon, syn twój, będzie królował po mnie, a on będzie siedział na stolicy mojej.
Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
18 A oto, już Adonijasz króluje, a ty teraz, królu, panie mój, o tem nie wiesz.
Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
19 Albowiem nabił wołów i bydła tłustego, i owiec bardzo wiele, i wezwał wszystkich synów królewskich, i Abijatara kapłana, i Joaba, hetmana wojska; ale Salomona, sługi twego, nie wezwał.
Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
20 Lecz ty królu, panie mój, wiesz, iż się oczy wszystkiego Izraela oglądają na cię, abyś im oznajmił, kto będzie siedział na stolicy króla, pana mego, po tobie.
Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
21 Inaczej stanie się, gdy zaśnie król, pan mój, z ojcy swymi, że będziemy ja i Salomon, syn mój, jako grzesznicy.
Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
22 A oto, gdy ona jeszcze mówiła z królem, przyszedł Natan prorok.
Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
23 I opowiedziano to królowi, mówiąc: Oto Natan, prorok; który wszedłszy do króla, pokłonił się królowi twarzą swą ku ziemi.
Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
24 Rzekł zatem Natan: Królu, panie mój, zażeś ty rzekł: Adonijasz będzie królował po mnie, a on usiędzie na stolicy mojej?
Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
25 Albowiem dziś szedłszy nabił wołów i bydła tłustego, i owiec bardzo wiele, i wezwał wszystkich synów królewskich, i hetmanów wojsk, i Abijatara kapłana, a oto oni jedzą z nim i piją, i mówią: Niech żyje król Adonijasz!
Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
26 Ale mnie, sługi twego, i Sadoka kapłana, i Banajasa, syna Jojadowego, i Salomona, sługi twego, nie wezwał.
Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
27 Izali od króla, pana mego, stała się ta rzecz? a nie oznajmiłeś słudze twemu, kto ma siedzieć na stolicy króla, pana mego, po nim?
Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
28 I odpowiedział król Dawid, mówiąc: Zawołajcie do mnie Betsaby; która przyszedłszy przed obliczność królewską, stanęła przed królem.
Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
29 Tedy przysiągł król, mówiąc: Jako żywy Pan, który wybawił duszę moję z każdego ucisku:
Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
30 Iż jakom ci przysiągł przez Pana, Boga Izraelskiego, mówiąc: Że Salomon, syn twój, królować będzie po mnie, a on usiędzie na stolicy mojej miasto mnie, tak dziś uczynię.
ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
31 I nachyliwszy się Betsaba twarzą ku ziemi, ukłoniła się królowi, i rzekła: Niech żyje Dawid król, pan mój, na wieki!
Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
32 Zatem rzekł król Dawid: Zawołajcie do mnie Sadoka kapłana, i Natana proroka, i Banajasa, syna Jojadowego. I weszli do króla.
Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
33 I rzekł im król: Weźmijcie z sobą sługi pana waszego, a wsadźcie Salomona, syna mego, na mulicę moję, i prowadźcie go do Gihonu.
mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
34 A tam go pomaże Sadok kapłan, i Natan prorok za króla nad Izraelem; potem zatrąbicie w trąbę, a rzeczecie: Niech żyje król Salomon!
Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
35 Potem pójdziecie za nim; a on przyszedłszy, siądzie na stolicy mojej, i będzie królował miasto mnie; bom mu ja rozkazał, aby był wodzem nad Izraelem i nad Judą.
Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
36 I odpowiedział Banajas, syn Jojada, królowi, mówiąc: Amen. Niech to stwierdzi Pan, Bóg króla, pana mego.
Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
37 Jako był Pan z królem, panem moim, tak niech będzie z Salomonem, a niechaj wywyższy stolicę jego nad stolicę Dawida króla, pana mego.
Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
38 A tak szedł Sadok kapłan, i Natan prorok, i Banajas, syn Jojada, przytem Cheretczycy, i Feletczycy, i wsadzili Salomona na mulicę króla Dawida, a prowadzili go do Gihonu.
Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
39 Tedy wziął Sadok kapłan róg olejku z namiotu, i pomazał Salomona. Potem trąbili w trąbę, i zakrzyknął wszystek lud: Niech żyje król Salomon!
Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
40 I szedł wszystek lud za nim. Tenże lud grał na piszczałkach, weseląc się weselem wielkiem, tak iż drżała ziemia od głosu ich.
Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
41 Co gdy usłyszał Adonijasz, i wszyscy wezwani, którzy byli z nim, (a już się też była dokończyła uczta, ) słysząc też i Joab głos trąby, rzekł: Cóż to za krzyk miasta huczącego?
Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
42 A gdy on tego domawiał, oto Jonatan, syn Abijatara kapłana, przyszedł. Któremu rzekł Adonijasz: Wnijdź; boś ty mąż stateczny, a powiesz nam co dobrego.
Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
43 Tedy odpowiedział Jonatan, i rzekł Adonijaszowi: Dawid król, pan nasz, postanowił zapewne Salomona królem.
Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
44 Albowiem posłał z nim król Sadoka kapłana, i Natana proroka, i Banajasa, syna Jojadowego, do tego Cheretczyki i Feletczyki, którzy go wsadzili na mulicę królewską;
Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
45 I pomazali go Sadok kapłan, i Natan prorok za króla w Gihonie, i szli stamtąd weseląc się, tak, że zadrżało miasto; tenci jest krzyk, któryście słyszeli;
ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
46 I już usiadł Salomon na stolicy królestwa.
Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
47 Nadto i słudzy królewscy przyszli, aby błogosławili Dawidowi królowi, panu naszemu, mówiąc: Niech sławniejsze uczyni Bóg imię Salomonowe nad imię twoje, a niech wywyższy stolicę jego nad stolicę twoję. I pokłonił się król na łożu swem.
Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
48 Przytem tak rzekł król: Błogosławiony Pan, Bóg Izraelski, który dał dziś siedzącego na stolicy mojej, na co patrzą oczy moje.
inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
49 Zlękli się tedy, i wstali wszyscy wezwani, którzy byli z Adonijaszem, i poszli każdy w drogę swą.
Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
50 Adonijasz także, bojąc się Salomona, wstał, i poszedł, a uchwycił się rogów ołtarza.
Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
51 I oznajmiono Salomonowi, mówiąc: Oto Adonijasz boi się króla Salomona, a oto uchwycił się rogów ołtarza, mówiąc: Niech mi dziś przysięże król Salomon, że nie zabije sługi swego mieczem.
Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
52 Tedy rzekł Salomon: Jeźli będzie mężem statecznym, nie spadnie i włos z niego na ziemię; ale jeźli się w nim znajdzie co złego, pewnie umrze.
Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
53 A tak posłał król Salomon, i przywiedziono go od ołtarza; a gdy przyszedł, ukłonił się królowi Salomonowi, i rzekł mu Salomon: Idź do domu twego.
Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

< I Królewska 1 >