< I Kronik 22 >

1 I rzekł Dawid: Toć jest miejsce domu Pana Boga, i to ołtarz na całopalenie Izraelowi.
Ndipo Davide anati, “Nyumba ya Yehova Mulungu idzakhala pano, ndiponso guwa lansembe zopsereza za Israeli.”
2 Przetoż rozkazał Dawid, aby zgromadzono cudzoziemców, którzy byli w ziemi Izraelskiej; i postanowił z nich kamienników, aby ciosali kamienie czworograniaste na budowanie domu Bożego.
Choncho Davide analamula kuti asonkhanitse alendo onse amene amakhala mu Israeli ndipo kuchokera pakati pawo anasankha amisiri a miyala kuti aseme miyala yomangira nyumba ya Mulungu.
3 Żelaza taż bardzo wiele na gwoździe, i na drzwi w bramach, i na spajanie nagotował Dawid, i miedzi wagę niezliczoną.
Ndipo anapereka zitsulo zambiri zopangira misomali ya zitseko za pa zipata ndi zolumikiza zake. Anaperekanso mkuwa wochuluka wokanika kuwuyeza.
4 Drzewa taż cedrowego bez liczby, albowiem nawieźli Dawidowi Sydończycy i Tyryjczycy drzewa cedrowego bardzo wiele.
Iye anaperekanso mitengo yambiri ya mkungudza, yosawerengeka, pakuti anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo anabweretsa yambiri kwa Davide.
5 Bo rzekł był Dawid: Salomon, syn mój, jest młodzieńczykiem małym, a dom ma być zbudowany Panu wielki i znamienity, któregoby imię i sława po wszystkiej ziemi była; przetoż teraz nagotuję mu potrzeb. I nagotował Dawid przed śmiercią swą bardzo wiele potrzeb.
Davide anati, “Mwana wanga Solomoni ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Koma nyumba yomwe timangire Yehova iyenera kukhala yaulemerero, yotchuka ndi yokongola pamaso pa anthu a mitundu yonse. Choncho ndikonzekeratu zambiri.” Motero Davide anayikonzekera kwambiri asanamwalire.
6 Tedy zawołał Salomona, syna swego, a przykazał mu, aby zbudował dom Panu, Bogu Izraelskiemu.
Tsono iye anayitana Solomoni mwana wake ndipo anamulamula kuti adzamangire nyumba Yehova Mulungu wa Israeli.
7 I rzekł Dawid do Salomona: Synu mój! Umyśliłem był w sercu mojem, zbudować dom imieniowi Pana Boga mego.
Davide anati kwa Solomoni, “Mwana wanga, ine ndinali ndi maganizo oti ndimangire nyumba Dzina la Yehova Mulungu wanga.
8 Ale się stało do mnie słowo Pańskie, mówiąc: Wieleś krwi rozlał, i wielkieś wojny prowadził; nie będziesz budował domu imieniowi memu, przeto żeś wiele krwi rozlał na ziemię przedemną,
Koma Yehova anandiyankhula kuti, ‘Iwe wapha anthu ambiri ndiponso wachita nkhondo zambiri. Sumangira dzina langa nyumba chifukwa wapha anthu ambiri pa dziko lapansi pamaso panga.
9 Oto syn, któryć się urodzi, będzie mężem spokojnym; bo mu dam odpocznienie od wszystkich nieprzyjaciół jego zewsząd. Przetoż Salomon będzie imię jego; albowiem pokój i odpocznienie dam Izraelowi za dni jego.
Koma udzabala mwana wamwamuna amene adzakhala munthu wamtendere ndi wabata ndipo ndidzamupatsa mpumulo kuchokera kwa adani ake onse a mbali zonse. Dzina lake adzatchedwa Solomoni ndipo Ine ndidzapereka mtendere ndi bata kwa Israeli pa nthawi ya ulamuliro wake.
10 On zbuduje dom imieniowi memu; on mi będzie za syna, a ja mu będę za ojca, i utwierdzę stolicę królestwa jego nad Izraelem aż na wieki.
Iye ndiye adzandimangire nyumba. Adzakhala mwana wanga ndipo Ine ndidzakhala abambo ake. Ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake waufumu mʼdziko la Israeli mpaka muyaya.’”
11 Przetoż Pan będzie z tobą, synu mój! I będzieć się szczęściło, i zbudujesz dom Pana, Boga twego, jako mówił o tobie.
“Tsopano mwana wanga, Yehova akhale nawe ndipo upambane ndi kumanga Nyumba ya Yehova Mulungu wako, monga momwe Iye ananenera kuti udzatero.
12 Wszakże niech ci da Pan roztropność, i zmysł, a niech cię postanowi nad Izraelem, abyś strzegł zakonu Pana Boga twego.
Yehova akupatse nzeru ndi kumvetsetsa pamene Iye adzakuyika kukhala wolamulira Israeli, kuti udzasunge malamulo a Yehova Mulungu wako.
13 Tedy szczęśliwym będziesz, jeźli strzedz i czynić będziesz przykazania i sądy, które rozkazał Pan przez Mojżesza Izraelowi. Zmacniajże się, a bądź mężem, nie bój się ani się lękaj.
Ndipo udzapambana ngati udzamvera mosamala malangizo ndi malamulo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kudzera mwa Mose. Khala wamphamvu ndi wolimba mtima. Usachite mantha kapena kutaya mtima.
14 A otom ja w utrapieniu mojem nagotował na dom Pański złota sto tysięcy talentów, i srebra tysiąc tysięcy talentów do tego miedzi i żelaza bez wagi, bo tego wiele jest: drzewa także, i kamienia nagotowałem, a ty do tego przyczynisz.
“Ine movutikira kwambiri ndapereka ku Nyumba ya Mulungu matani 3,400 agolide, matani 34,000 asiliva, ndiponso mkuwa ndi chitsulo, matabwa ndi miyala. Ndipo iwe utha kuwonjezerapo pa zimenezi.
15 Masz też u siebie wiele rzemieślników, kamiennikówi i murarzy, i cieśli, i wszelkich biegłych w każdem rzemieśle.
Iwe uli ndi antchito ambiri: osema miyala, amisiri a miyala, ndi amisiri a matabwa, komanso anthu ambiri aluso la ntchito zosiyanasiyana,
16 Złota, srebra, i miedzi, i żelaza niemasz liczby; wstańże a czyń, a Pan będzie z tobą.
zagolide ndi zasiliva, zamkuwa, zazitsulo, amisiri osawerengeka. Tsopano yamba ntchito, ndipo Yehova akhale nawe.”
17 I przykazał Dawid wszystkim książętom Izraelakim, aby pomagali Salomonowi synowi jego;
Tsono Davide analamula atsogoleri onse a Israeli kuti athandize Solomoni mwana wake.
18 Mówiąc: Izali Pan Bóg wasz nie jest z wami, który wam dał odpocznienie zewsząd? Bo dał w rękę moję obywateli tej ziemi, i poddane jest ta ziemia Panu i ludowi jego.
Iye anawawuza kuti, “Kodi Yehova Mulungu, sali nanu? Ndipo Iye siwakupatsani mpumulo mbali zonse? Pakuti Iyeyo wapereka eni nthaka kwa inu ndipo dziko lili pa ulamuliro wa Yehova ndi anthu ake.
19 Teraz tedy oddajcie serce swe i duszę swoję, abyście szukali Pana, Boga waszego; i wstańcie, a budujcie świątnicę Panu Bogu, żebyście tam wnieśżli skrzynię przymierza Pańskiego, i naczynia święte Boże, do domu, który będzie zbudowany imieniowi Pańskiemu.
Tsono perekani mtima wanu ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu. Yambani kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti mubweretse Bokosi la Chipangano la Yehova ndi zinthu zopatulika za Mulungu mʼNyumba ya Mulungu imene idzamangidwa chifukwa cha dzina la Yehova.”

< I Kronik 22 >