< I Kronik 16 >

1 A gdy przynieśli skrzynię Bożą, i postawili ją w pośród namiotu, który był Dawid rozbił, tedy sprawowali całopalenia i ofiary spokojne przed Bogiem.
Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu.
2 A gdy dokończył Dawid ofiarować całopalenia, i ofiar spokojnych, błogosławił ludowi w imię Pańskie.
Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova.
3 I rozdzielił wszystkim mężom Izraelskim, od męża aż do niewiasty, każdemu po bochenku chleba, i po sztuce mięsa, i po łagiewce wina.
Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.
4 A postanowił przed skrzynią Pańską z Lewitów sługu, aby wspominali, i wyznawali, i chwalili Pana, Boga Izraelskiego.
Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli.
5 Asaf był przedniejszy, a wtóry po nim Zacharyjasz, Jehyjel, i Semiramot, i Jechyjel i Matytyjasz, i Elijab, i Benajasz, i Obededom, i Jechyjel; ci na instrumentach, na lutniach, na harfach, ale Asaf na cymbałach, grali.
Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga,
6 Benajasz zaś i Jachazyjel kapłani z trąbami ustawiczne byli przed skrzynią przymierza Bożego.
ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.
7 Dopiero dnia onego najpierwej postanowił Dawid, aby tym psalmem chwalony był Pan przez Asafa i braci jego:
Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:
8 Wysławiajcie Pana, wzywajcie imienia jego, a opowiadajcie między narodami sprawy jego.
Yamikani Yehova, itanani dzina lake; lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.
9 Śpiewajcie mu, grajcie mu, rozmawiajcie o wszystkich cudach jego.
Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando; nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.
10 Chlubcie się w imieniu świętem jego, a niech się rozraduje serce szukających Pana.
Nyadirani dzina lake loyera; ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.
11 Szukajcie Pana, i mocy jego; szukajcie oblicza jego zawżdy.
Dalirani Yehova ndi mphamvu zake; funafunani nkhope yake nthawi zonse.
12 Wspominajcie dziwne sprawy jego, które czynił, i cuda jego, i sądy ust jego.
Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita, zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,
13 O nasienie Izraelskie, słudzy jego! O synowie Jakóbowi, wybrani jego!
inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake, inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.
14 On jest Pan, Bóg nasz; po wszystkiej ziemi sądy jego.
Iye ndiye Yehova Mulungu wathu; chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.
15 Pamiętajcie aż na wieki na przymierze jego, na słowow, które przykazał do tysiącznego pokolenia;
Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse, mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,
16 Które postanowił z Abrahamem, i na przysięgę jego z Izaakiem;
pangano limene anachita ndi Abrahamu, lonjezo limene analumbira kwa Isake.
17 I postanowił to Jakóbowi za prawo, a Izraelowi za przymierze wieczne,
Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo, kwa Israeli monga pangano lamuyaya.
18 Mówiąc: Tobie dam ziemię Chananejską za sznur dziedzictwa waszego.
“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani monga cholowa chimene udzachilandira.”
19 Choć was była mała liczba, a przez krótki czas byliście przychodniami w niej;
Ali anthu owerengeka, ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,
20 I przechodzili od narodu do narodu, i od królestwa do innego ludu:
iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina, ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.
21 Nie dopuścił nikomu, aby ich uciskać miał, i karał dla nich królów,
Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze; chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:
22 Mówiąc: Nie tykajcie pomazańców moich, a prorokom moim nie czyńcie nic złego.
“Musakhudze odzozedwa anga; musawachitire choyipa aneneri anga.”
23 Śpiewajcie Panu wszystka ziemio; opowiadajcie ode dnia do dnia zbawienie jego.
Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi; lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
24 Opowiadajcie między narodami chwałę jego, i między wszystkimi ludźmi dziwne sprawy jego;
Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse, ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.
25 Bo wielki jest Pan, i chwalebny bardzo, i straszniejszy nad wszystkich bogów;
Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda; Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.
26 Gdyż bogowie pogańscy są bałwanami; ale Pan niebiosa uczynił.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake, koma Yehova analenga kumwamba.
27 Sława i zacność przed nim, moc i wesele na miejscu jego.
Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake; mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.
28 Przynieście Panu pokolenia narodów, przynieście Panu chwałę i moc.
Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,
29 Przynieście Panu chwałę imienia jego, przynieście dary, a przychodźcie przed obliczności jego; kłaniajcie się Panu w ozdobie świętobliwości.
perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake. Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake; pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.
30 Bójcie się oblicza jego wszystka ziemio, a będzie utwierdzony okrąg ziemi, aby się nie poruszył.
Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi! Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.
31 Niech się rozradują niebiosa, a niech się rozweseli ziemia, a niech mówią w narodach: Pan króluje!
Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere; anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”
32 Niech zaszumi morze, i ze wszystkiem, co w niem jest; niech się rozraduje pole, i wszystko, co na niem jest.
Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo; minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!
33 Tedy się rozweselą drzewa leśne przed Panem; albowiem przyszedł sądzić ziemię.
Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba, idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova, pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.
34 Wysłwiajcie Pana; albowiem dobry, bo na wieki trwa miłosierdzie jego.
Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino; chikondi chake chikhala mpaka muyaya.
35 A mówcie: Zachowaj nas, Boże zbawienia naszego! i zgromadź nas, a wyrwij nas od pogan, abyśmy wielbili imię święte twoje, i chlubili się w chwale twojej.
Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu, mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina, kuti tiyamike dzina lanu loyera, kuti tikutamandeni.”
36 Błogosławiony Pan, Bóg Izraelski, od wieków aż na wieki. I rzekł wszystek lud Amen, i chwalił Pana.
Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli, kuyambira muyaya mpaka muyaya. Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”
37 I zostawił tam Dawid przed skrzynią przymierza Pańskiego Asafa i braci jego, aby służyli przed skrzynią ustawicznie według potrzeby dnia każdego.
Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse.
38 Lecz Obededoma i braci ich sześdziesiąt i ośm, Obededoma mówię, syna Jedytunowego, i Hosę, uczynił odźwiernymi.
Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.
39 A Sadoka kapłana, i braci jego kapłanów postawił przed przybytkiem Pańskim na wyżynie, która była w Gabaon,
Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni
40 Aby ofiarowali całopalenia Panu na ołtarzu całopalenia ustawicznie rano i w wieczór, a to według wszystkiego, co napisano w zakonie Pańskim, który przykazał Izraelowi.
kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli.
41 A z nimi Hemana i Jedytuna, i innych na to obranych, którzy byli z imienia mianowani, aby chwalili Pana, przeto iż na wieki trwa miłosierdzie jego.
Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.”
42 A między nimi Heman i Jedytun, trąbili i grali na trąbach, na cymbałach, i na innych instrumentach muzycznych Bogu; ale synów Jedytunowych postawił u wrót.
Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.
43 A tak rozszedł się wszystek lud, każdy do domu swego. Dawid się też wrócił, aby błogosławił domowi swemu.
Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

< I Kronik 16 >