< I Kronik 12 >

1 A cić są, co byli przyszli do Dawida do Sycelegu, gdy się jeszcze krył przed Saulem, synem Cysowym; a ci byli między mocarzami posiłek dawający w bitwie,
Nawa anthu amene anabwera kwa Davide ali ku Zikilagi pamene iye anathamangitsidwa ndi Sauli mwana wa Kisi (iwowo anali mʼgulu la asilikali amene ankamuthandiza pa nkhondo.
2 Noszący łuk, a prawą i lewą ręką ciskający kamieńmi, i strzelający z łuku, a byli z braci Saulowych z pokolenia Benjaminowego:
Iwo anali ndi mauta ndipo amadziwa kuponya mivi komanso miyala, ndipo amatha kuponyera dzanja lamanja kapena lamanzere. Iwo anali abale ake a Sauli ochokera ku fuko la Benjamini.
3 Książe Achyjezer, i Joaz, synowie Semmai Gabatczyka, i Jezyjel, i Falet, synowie Azmawetowi, i Baracha, i Jehu Anatotczyk;
Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri ndi Yowasi ana a Semaya wa ku Gibeya; Yezieli ndi Peleti ana a Azimaveti; Beraka, Yehu wa ku Anatoti,
4 Ismajasz też Gabaończyk, mężny między trzydziestoma, a był przełożony nad trzydziestoma; i Jeremijasz, i Jahazyjel, Johanan, i Jozabad Gliederatczyk;
ndi Isimaiya wa ku Gibiyoni, munthu wamphamvu mʼgulu la anthu makumi atatu aja, yemwenso anali mtsogoleri wawo; Yeremiya, Yahazieli, Yohanani, Yozabadi wa ku Gederi,
5 Eluzaj, i Jerymot, i Bealijasz, i Semaryjasz, i Sefatyjasz Harufitszyk;
Eluzai, Yerimoti, Bealiya, Semariya ndi Sefatiya Mharufi;
6 Elkana, i Jesyjasz, i Asareel i Joezer, i Jasobam Korchytczyk;
Elikana, Isiya, Azareli, Yowezeri ndi Yasobeamu a ku banja la Kora;
7 I Joela, i Zebadyjasz, synowie Jerohamowi z Giedor.
ndi Yowela ndi Zebadiya ana a Yerohamu wa ku Gedori.
8 A z pokolenia Gadowego zbiegli byli do Dawida na miejsce obronne na puszczę mężowie duży, mężowie sposobni do boju, noszący tarcz i kopiję, których twarze były jako lwie tarze, a jako sarny po górach prędcy;
Asilikali ena a fuko la Gadi anathawira kwa Davide ku linga lake ku chipululu. Iwo anali asilikali olimba mtima, okonzekera nkhondo ndipo amadziwa kugwiritsa ntchito chishango ndi mkondo. Iwowo anali woopsa ngati mikango ndipo anali aliwiro ngati ngoma zamʼmapiri.
9 Eser przedniejszy, Obadyjasz wtóry, Elijab trzeci,
Mtsogoleri wawo anali Ezeri, wotsatana naye anali Obadiya, wachitatu anali Eliabu,
10 Mismanna czwarty, Jeremijasz piąty,
wachinayi anali Misimana, Yeremiya anali wachisanu,
11 Ataj szósty, Eliel siódmy,
wachisanu ndi chimodzi anali Atai, Elieli anali wachisanu ndi chiwiri,
12 Jochanan ósmy, Elzebad dziewiąty,
wachisanu ndi chitatu anali Yohanani, Elizabadi anali wachisanu ndi chinayi,
13 Jeremijasz dziesiąty, Machbanajasz jedenasty.
wakhumi anali Yeremiya ndipo Makibanai anali wa 11.
14 Cić byli z synów Gadowych, hetmani wojska, jeden nad stem mniejszy, a większy nad tysiącem.
Anthu a fuko la Gadi amenewa anali atsogoleri; angʼonoangʼono amalamulira anthu 100 pamene akuluakulu amalamulira anthu 1,000.
15 Cić są, którzy przeszli Jordan miesiąca pierwszego, który był wylał ze wszystkich brzegów swoich; i wygnali wszystkich mieszkających w dolinach na wschód i na zachód słońca.
Awa ndi amene anawoloka Yorodani mwezi woyamba pamene mtsinje unali utasefukira mbali zonse, ndipo anathamangitsa aliyense amene amakhala mʼchigwa, mbali ya kumadzulo ndi kummawa.
16 Przyszli także niektórzy z synów Benjaminowych i z Judowych, do miejsca obronnego, do Dawida.
Anthu ena a fuko la Benjamini ndi ena ochokera ku Yuda anabweranso kwa Davide pamene anali ku linga lake.
17 I wyszedł Dawid przeciwko nim a odpowiadając, rzekł im: Jeźliście spokojnie przyszli do mnie, abyście mię ratowali, serce też moje złączy się z wami; ale jeźliście przyszli, abyście mię wydali nieprzyjaciołom moim, (choć nie masz nieprawości przy mnie) niech w to wejrzy Bóg ojców naszych, a niech sądzi.
Davide anapita kukakumana nawo ndipo anati, “Ngati mwabwera kwa ine mwamtendere, kuti mundithandize, ndakonzeka kugwirizana nanu. Koma ngati mwabwera kudzandipereka kwa adani anga, ngakhale kuti sindinalakwe, Mulungu wa makolo anthu aone izi ndipo akuweruzeni.”
18 Tedy Duch przyoblekł Amazyjasza, przedniejszego między hetmanami, i rzekł: Twoiśmy, o Dawidzie! a z tobą przestajemy, synu Isajego. Pokój, pokój tobie, i pokój pomocnikom twoim! gdyż ci pomaga Bóg twój. A tak przyjął ich Dawid, i postanowił ich hetmanami wojska.
Kenaka Mzimu anabwera pa Amasai, mtsogoleri wa anthu makumi atatu aja ndipo anati: “Inu Davide, ife ndife anu! Tili nanu limodzi, inu mwana wa Yese! Kupambana, Kupambana kwa inu, ndiponso kupambana kukhale kwa iwo amene akukuthandizani pakuti Mulungu wanu adzakuthandizani.” Kotero Davide anawalandira ndipo anawayika kukhala atsogoleri a magulu ake a ankhondo.
19 A z pokolenia Manasesowego odpadli niektórzy do Dawida, gdy ciągnął z Filistynami przeciwko Saulowi na wojnę; ale im nie byli na pomocy, gdyż naradziwszy się książęta Filistyńscy odesłali go, mówiąc: Ten z niebezpieczeństwem głów naszych odpadnie do Saula, pana swego.
Anthu ena a fuko la Manase anathawira kwa Davide pamene anapita ndi Afilisti kukamenyana ndi Sauli. (Iye ndi anthu ake sanathandize Afilisti chifukwa, atsogoleri awo atakambirana, anamubweza Davide. Iwo anati, “Ife tidzawonongedwa ngati uyu adzabwerera kwa mbuye wake Sauli).”
20 Gdy tedy szedł do Syceleu, uciekli do niego niektórzy z pokolenia Manasesowego: Adnach i Josabad, i Jediael, i Michael, i Jozabad i Elihu, i Sylletaj, i hetmani nad tysiącami w pokoleniu Manasesowem.
Davide atapita ku Zikilagi, anthu a fuko la Manase amene anathawira kwa iye anali awa: Adina, Yozabadi, Yediaeli, Mikayeli, Yozabadi, Elihu ndi Ziletai; atsogoleri a magulu a anthu 1,000 a ku Manase.
21 A ci posiłkowali Dawida przeciw onemu hufowi; bo mężni byli wszyscy, przetoż byli hetmanami w wojsku jego.
Iwowa anathandiza Davide kulimbana ndi magulu achifwamba, pakuti onsewa anali asilikali olimba mtima ndipo anali atsogoleri mʼgulu lake la ankhondo.
22 Nawet na każdy dzień ściągali się do Dawida na pomoc jemu, aż było wojsko wielkie jako wojsko Boże.
Tsiku ndi tsiku anthu amabwera kudzathandiza Davide, mpaka anakhala ndi gulu lalikulu la ankhondo, ngati gulu la ankhondo a Mulungu.
23 A tać jest liczba przedniejszych gotowych do boju, którzy przyszli do Dawida do Hebronu, aby przenieśli królestwo Saulowe do niego według słowa Pańskiego.
Nachi chiwerengero cha magulu a anthu ankhondo amene anabwera kwa Davide ku Hebroni kudzapereka ufumu wa Sauli kwa iye, monga momwe ananenera Yehova:
24 Z synów Judowych, noszących tarcz i włócznię, sześć tysięcy i ośm set gotowych do boju.
Anthu a fuko la Yuda onyamula chishango ndi mkondo analipo 6,800;
25 Z synów Symeonowych, mężnych do boju, siedm tysięcy i sto.
Anthu a fuko la Simeoni, asilikali okonzekera nkhondo analipo 7,100;
26 Z synów Lewiego cztery tysiące i sześć set.
Anthu a fuko la Levi analipo 4,600,
27 Jojada także przedniejszy z synów Aaronowych, a z nim trzy tysiące i siedm set.
mtsogoleri Yehoyada wa banja la Aaroni anabweranso ndi anthu 3,700,
28 A Sadok młodzieniec, rycerz mężny, i z domu ojca jego książąt dwadzieścia i dwóch.
ndi Zadoki, mnyamata wankhondo wolimba mtima, anabwera ndi akuluakulu 22 ochokera mʼbanja lake;
29 A z synów Benjaminowych, braci Saulowych, trzy tysiące; bo jeszcze wielka część ich przestawała z domem Saulowym.
Anthu a fuko la Benjamini, abale ake a Sauli analipo 3,000 ndipo ambiri anali ndi Sauli ku nyumba yake pa nthawiyi;
30 A z synów Efraimowych dwadzieścia tysięcy i ośm set, ludzi mężnych, mężów sławnych w domach ojców ich.
Anthu a fuko la Efereimu, asilikali olimba mtima, otchuka pa mabanja awo analipo 20,800;
31 A z połowy pokolenia Manasesowego ośmnaście tysięcy, którzy byli mianowani według imion, aby przyszli i postanowili Dawida królem.
Anthu a fuko latheka la Manase amene anawayitana kuti adzakhazikitse nawo ufumu wa Davide analipo 18,000;
32 A z synów Isascharowych, umiejących rozeznawać czasy, tak iż wiedzieli, co kiedy czynić miał Izrael, książąt ich dwieście; a wszyscy bracia ich przestawali na radzie ich.
Anthu a fuko la Isakara amene ankazindikira nthawi ndipo amadziwa zimene Israeli ankayenera kuchita, analipo atsogoleri 200 pamodzi ndi abale awo onse amene amawatsogolera.
33 Z pokolenia Zabulonowego, którzy wychodzili na wojnę, gotowych do boju z każdym orężem wojennym, pięćdziesiąt tysięcy, stawających w szyku jednostajnem sercem.
Anthu a fuko la Zebuloni, analipo 5,000. Iwowa anali asilikali odziwa bwino nkhondo, okhala ndi zida za mtundu uliwonse, okonzekera kudzathandiza Davide ndi mtima umodzi.
34 A z pokolenia Neftalimowego książąt tysiąc, a z nimi z tarczami i z kopijami trzydzieści i siedm tysięcy.
Anthu a fuko la Nafutali, analipo atsogoleri 1,000 pamodzi ndi anthu 37,000 onyamula zishango ndi mikondo;
35 A z pokolenia Danowego, gotowych do boju, dwadzieścia i ośm tysięcy i sześć set.
Anthu a fuko la Dani, okonzekera nkhondo analipo 28,600.
36 A z pokolenia Aserowego, którzy wychodzili na wojnę, i umieli się szykować do bitwy, czterdzieści tysięcy.
Anthu a fuko la Aseri, asilikali odziwa bwino nkhondo, okonzekeradi nkhondo analipo 40,000;
37 A z Za-Jordania z pokolenia Rubenowego i Gadowego, i z połowy pokolenia Manasesowego ze wszystkim orężemwojennym sto i dwadzieścia tysięcy.
Ndipo kuchokera kummawa kwa Yorodani, anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase, amene anali ndi zida za mtundu uliwonse analipo 120,000.
38 Ci wszyscy mężowie waleczni sprawni ku bitwie, sercem uprzejmem przyszl do Hebronu, aby postanowili Dawida królem nad wszystkim Izraelem. Nadto i wszyscy inni z Izraela jednego serca byli, aby postanowili królem Dawida.
Onsewa anali anthu odziwa kumenya nkhondo amene anadzipereka ku magulu awo. Iwo anabwera ku Hebroni ali otsimikiza kudzamuyika Davide kukhala mfumu ya Aisraeli. Aisraeli ena onse anali ndi mtima umodzinso womuyika Davide kukhala mfumu.
39 I byli tam z Dawidem przez trzy dni jedząc i pijąc: bo im byli nagotowali bracia ich.
Anthuwa anakhala ndi Davide masiku atatu akudya ndi kumwa pakuti mabanja awo anawapatsa zakudya.
40 Także i którzy blisko ich byli aż do Isaschar i Zabulon i Neftalim, przynosili chleby na osłach, i na wielbłądach, i na mułach, i na wołach, potrawy, mąki, figi, rodzynki, i wino, i oliwę, i wołów, i owiec wielkim dostatkiem; bo była radość w Izraelu.
Komanso anthu oyandikana nawo ochokera ku Isakara, Zebuloni ndi Nafutali anabweretsa zakudya pa abulu, ngamira, nyulu ndi ngʼombe. Panali ufa wambiri, makeke ankhuyu, ntchintchi za mphesa, vinyo, mafuta, ngʼombe, nkhosa ndi mbuzi, popeza munali chimwemwe mu Israeli.

< I Kronik 12 >