< I Kronik 10 >

1 A gdy Filistynowie walczyli z Izraelem, uciekli mężowie Izraelscy przed Filistynami a polegli, będąc porażeni na górze Gielboe.
Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
2 I gonili Filistynowie Saula i synów jego; i zabili Filistynowie Jonatana, i Abinadaba, i Melchisuego, synów Saulowych.
Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
3 A gdy się zmocniła bitwa przeciw Saulowi, trafili na niego strzelcy, i z łuku zraniony jest od strzelców.
Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 Rzekł tedy Saul do sługi swego, co za nim broń nosił: Dobądź miecza twego, a przebij mię nim, by snać nie przyszli ci nieobrzezańcy, a nie pośmiewali się ze mnie. Ale nie chciał sługa, który nosił broń jego; bo się bardzo bał. Przetoż porwawszy Saul miech, padł nań.
Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
5 A widząc sługa, co nosił broń jego, że umarł Saul, padłszy też i sam na miecz umarł.
Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa.
6 A tak umarł Saul, i trzej synowie jego, i wszystek dom jego z nim pospołu zginął.
Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 Co gdy ujrzeli wszyscy mężowie Izraelscy, którzy mieszkali na dolinie, iż uciekli Izraelczycy, a iż pomarli Saul i synowie jego, opuściwszy miasta swe także uciekli. I przyszli Filistynowie, i mieszkali w nich.
Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 A gdy nazajutrz przyszli Filistynowie brać łupy z pobitych, znaleźli Saula, i synów jego, leżących na górze Gielboe;
Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa.
9 A złupiwszy go wzięli głowę jego, i zbroję jego, i posłali po ziemi Filistyńskiej w około, aby to ogłoszone było przed bałwany ich, i przed ludem.
Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
10 I położyli zbroję jego w domu boga swego, a głowę jego zawiesili w domu Dagonowym.
Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Usłyszawszy tedy wszyscy mężowie Jabes Galaad wszystko, co uczynili Filistynowie Saulowi,
Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
12 Powstali wszyscy mężowie mocni, i wzięli ciało Saulowe, i ciało synów jego, a przyniósłszy do Jabes pogrzebli kości ich pod dębem w Jabes, i pościli przez siedm dni.
anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 A tak umarł Saul dla przestępstwa swego, którem był wystąpił przeciwko Panu, i przeciwko słowu Pańskiemu, któego nie przestrzegał, iż się radził ducha wieszczego, pytając się go;
Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa,
14 A iż się nie radził Pana, zabił go, a przeniósł królestwo na Dawida, syna Isajego.
sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.

< I Kronik 10 >