< Rzymian 3 >

1 Na czym więc polega przewaga Żyda nad poganinem? I jaką korzyść daje obrzezanie?
Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe?
2 Ogromną i to pod każdym względem! Należy pamiętać, że to Żydom Bóg przekazał swoje słowa.
Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 Co z tego, że niektórzy z nich nie dochowali im wierności? Czy z tego powodu Bóg przestaje dotrzymywać swoich obietnic?
Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu?
4 Oczywiście, że nie! Bóg bowiem jest prawdomówny, a każdy człowiek jest kłamcą, jak mówi Pismo: „Boże, Twoje słowa okażą się sprawiedliwe i oddalisz od siebie wszelkie oskarżenia”.
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti, “Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi kupambana pamene muweruza.”
5 Jeśli poprzez naszą nieprawość objawiona zostaje prawość Boga, to jaki stąd wniosek? Czy Bóg jest niesprawiedliwy, gdy okazuje gniew? Tak rozumują ludzie.
Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira).
6 Oczywiście, że nie jest niesprawiedliwy, bo gdyby tak było, to jak Bóg mógłby sądzić świat?
Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi?
7 Zapytasz może: „Skoro moje kłamstwo sprawia, że objawiona zostaje Boża prawda i Bóg odbiera z tego chwałę, to dlaczego ja mam być sądzony za grzech?”.
Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?”
8 Czy mamy twierdzić: „Popełniajmy zło, aby pojawiło się dobro”? Niektórzy oskarżają nas, że tak mówimy. Nie unikną jednak kary.
Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
9 Czy wobec tego my, Żydzi, jesteśmy lepsi od pogan? Oczywiście, że nie. Wykazaliśmy już, że zarówno Żydzi, jak i poganie, są grzesznikami.
Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa.
10 Potwierdza to zresztą Pismo: „Nie ma człowieka, który byłby prawy,
Monga kwalembedwa kuti, “Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 nie ma takiego, który byłby rozumny, ani takiego, który szukałby Boga.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira, palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Wszyscy zbłądzili i upadli. Nie ma nikogo, ani jednego, kto by dobrze postępował.
Onse apatukira kumbali, onse pamodzi asanduka opandapake. Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino, palibe ngakhale mmodzi.”
13 Słowa ludzi są jak grób, a ich język jest pełen kłamstw; w ustach mają jad węża.
“Kummero kwawo kuli ngati manda apululu; ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.” “Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 Wypowiadają przekleństwa i gorzkie słowa.
“Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 Są skłonni do morderstwa,
“Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 zostawiają za sobą zniszczenie i nędzę.
Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 Nigdy nie weszli na ścieżkę pokoju
ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 i nie odczuwają nawet lęku przed Bogiem”.
“Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Wiemy dobrze, że Prawo Mojżesza obowiązuje tych, którzy mu podlegają. I dlatego każde usta muszą zamilknąć i cały świat musi się uniżyć przed Bogiem.
Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu.
20 On bowiem nie uniewinni żadnego człowieka ze względu na to, że przestrzegał on Prawa Mojżesza. Prawo uświadamia nam tylko nasz grzech.
Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
21 Teraz jednak Bóg wskazał inny sposób uniewinnienia—bez przestrzegania Prawa Mojżesza, ale poświadczony przez to Prawo i przez proroków.
Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni.
22 Uniewinnienie to pochodzi od Boga i obejmuje tych, którzy wierzą Jezusowi Chrystusowi. Jest ono dostępne dla wszystkich, którzy Mu wierzą. Bo nie ma żadnej różnicy:
Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina,
23 wszyscy ludzie zgrzeszyli i daleko im do Bożego ideału.
pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu
24 A zostają uniewinnieni za darmo, dzięki Bożej łasce i dzięki odkupieniu, jakiego dokonał Jezus Chrystus.
ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola.
25 To Jego Bóg uczynił narzędziem przebłagania za grzechy. Aby dostąpić tego uniewinnienia, musimy uwierzyć, że Jego przelana krew może nas pojednać z Bogiem. Bóg ogłosił uniewinnienie, odpuszczając grzechy przeszłości. Cierpliwie czekał bowiem, aż Chrystus—w obecnym czasie—zgładzi je. Okazał się więc sprawiedliwy i uniewinnia każdego, kto uwierzy Jezusowi.
Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale.
Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Gdzie jest więc powód do dumy? Został uchylony! Czy przez Prawo uczynków? Nie, przez prawo wiary!
Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro.
28 Jesteśmy bowiem przekonani, że człowiek zostaje uniewinniony dzięki wierze, a nie dzięki spełnianiu uczynków wymaganych przez Prawo.
Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo.
29 Czy Bóg przygotował to tylko dla Żydów? A może i dla pogan? Oczywiście, że również dla pogan!
Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso,
30 Bóg jest jeden i w ten sam sposób—dzięki wierze!—uniewinnia zarówno Żydów, jak i pogan.
popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho.
31 Czy więc z powodu uniewinnienia, otrzymanego dzięki wierze, lekceważymy Prawo Mojżesza? Absolutnie nie! Umieszczamy je tylko we właściwym miejscu.
Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.

< Rzymian 3 >