< Ioanes 9 >

1 IESUS lao kotin daulul, ap masani aramas amen me maskun sang a ipwidi.
Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire.
2 Sapwilim a tounpadak kan ap idok re a potoan ong: Rapi, is me wiadar dip, i de sam a in a, pweki a ipwidi maskun?
Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”
3 Iesus kotin sapeng: Kaidik i me wiadar dip, pil kaidik in a de sam a, a pwe en Kot a wiawia kan en kasansal kida i.
Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu.
4 I en kapwaiada wiawia kan en me kadar ia do arain ansaun ran, pwe pong pan kodo, i ansau solar amen kak dodok.
Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito.
5 Arain ai mi sappa, ngai marain en sappa.
Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”
6 A lao kotin masanier met, ap likidi nani pwel, wiakida pwel madak iriski mas a.
Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo.
7 Masani ong i: Kolang pil en Siloa (iet wewe: Pakadarado), opinok ia! I ari kola opinok, ap puredo kilangada wasa.
Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.
8 A men imp a kan, o me iang kilangadar, me a men poekipoek amen mas o, rap indada: Kaidik i, me wonon poekipoeki?
Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?”
9 Akai me inda: I met; a akai me inda: Likamata i, a pein i indada: Ngai i.
Ena ananena kuti anali yemweyo. Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.” Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”
10 Irail ari indang i: Iaduen por en mas om akan a kapad pasang?
Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”
11 A sapeng indada: Aramas amen me adaneki Iesus, me wiadar pwel madak, iriski mas ai, masani ong ia: Kolang pil en Siloa, opinok ia! I ari kola opinok, ap kilangada wasa.
Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”
12 Irail ap idok re a: Ia i? A sapeng: I sasa.
Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?” Iye anati, “Ine sindikudziwa.”
13 Irail ap kalualang ren Parisär akan me maskun mas.
Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi.
14 Ari, ni ran en sapat, me Iesus kotin wiadar pwel, kapad pasang por en mas a kan.
Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu.
15 Parisär akan pil idok duen me a kilang kida wasa. A sapeng irail: A ki ong pwel ni por en mas ai, i ap opinok, ngai ari kilangada wasa.
Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”
16 Parisär kai ap inda: Aramas men et kaidik men ren Kot, aki a sota apwali ran en sapat. Akai indada: Daduen, aramas dipan amen kak wia kilel pukat? Irail ari liak toror pasang.
Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.” Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.
17 Irail pil kalelapok ren me maskun o: Da me koe lamelame duen i? Pwe a kapad pasang mas om? A sapeng: Saukop amen i.
Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?” Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”
18 Men Sus oko ap sota kamelele, me a ipwiki wei maskun, ap kilangada wasa. Irail lao ekeredo sam o in en me kilangada wasa.
Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake.
19 Irail idok re’ra: Nouma ol men et, me komail indinda, me a ipwiki wei maskun? Iaduen a ngarada wasa ansau wet?
Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”
20 Sam a in a sapeng ir indada: Se asa, me nait ol et, me ipwiki wei maskun.
Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona.
21 A se sasa duen a ngarada wasa o me kapad pasang por en mas a. A malar, kainoma re a, a pan pein sakaraki i.
Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.”
22 Sam o in a inda mepukat, pweki ar masak Sus oko. Pwe Sus oko inauki pena, ma meamen pan kadede me i Kristus a pan lokidokila sang nan sinakoke.
Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge.
23 I me sam o in a indada kida: A malar, kainoma re a.
Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”
24 Irail ap eker aramas maskun kariapak indai ong i: Wauneki Kot, se asa, me aramas men et me dipan amen,
Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”
25 A sapeng ir indada: I sasa, ma i me dipan amen de so. I eta me i asa, me ngai me maskun mas o, i ap potoan ngaradar wasa.
Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”
26 Irail ap pil idok re a: Da me a wiai ong uk? Iaduen a kapad pasang mas om?
Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”
27 A sapeng irail: I indai ong komail er, a komail sota rong? Da me komail pil men rongki? Komail pil pan a tounpadak ala?
Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”
28 Irail kaurureki indada: A tounpadak amen koe, a kit tounpadak en Moses akan.
Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose!
29 Kit asa, me Kot masani ong Moses. A lap o se sasa, wasa a ko sang ia.
Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”
30 Aramas o sapeng indang irail: Meid kapuriamui! I me kapad pasang mas ai kat, a komail sasa, wasa a koti sang ia.
Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga.
31 Kitail asa, me Kot sota kin mangi me dipan akan. A meamen, me lan Kot, o dadaurata kupur a, iei me a kin kotin mangi.
Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake.
32 Sang mas kokodo sota me rongadar, me meamen kapad pasang mas en me ipwiki wei maskun. (aiōn g165)
Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. (aiōn g165)
33 Ma men et sota me ren Kot, a sota pan kak wia meakot.
Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”
34 Irail sapeng indang i: Koe me ipwiki wei dip akan a koe ap padaki ong kit? Irail ari kasela i.
Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.
35 Iesus lao kotin mangidar, me re kasela i, a lao masani i, ap kotin masani ong i: Koe kin poson Nain Kot?
Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”
36 A sapeng potoan ong: Maing, is i pwe i en poson i?
Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”
37 Iesus kotin masani ong i: Koe me kilang i. A iet i, me kasokasoi ong uk.
Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”
38 A sapeng i: Maing, i posonlar, i ari kaudok ong i.
Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.
39 Iesus kotin masani: I kodon kadeik nan sappa et, pwe me so kilang wasa, en kilangada, a me kilang wasa, en maskunla.
Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”
40 A Parisär akan, me mi re a, rongadar a masan pukat, re ap peidok re a: Da, kit me pil maskun?
Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”
41 Iesus kotin masani ong irail: Ma komail maskun, sota pan dip omail. A komail indada: Se kilekilang wasa, iei me omail dip pan mimietaki.
Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

< Ioanes 9 >