< زکریا 9 >
خداوند مجازات قومها را اعلام نموده است، چون او نه فقط قوم اسرائیل را زیر نظر دارد، بلکه مراقب همهٔ قومهای جهان نیز میباشد. او حدراخ، دمشق و حمات را که در نزدیکی دمشق است مجازات خواهد کرد. حتی صور و صیدون هم با وجود مهارتشان از مجازات او در امان نخواهند ماند. | 1 |
Mawu a Yehova odzudzula dziko la Hadiraki ndi mzinda wa Damasiko pakuti maso a anthu ndiponso mafuko onse a Israeli ali pa Yehova—
ndiponso mzinda wa Hamati, umene ukuchita malire ndi dzikoli, komanso pa Turo ndi Sidoni, ngakhale kuti iwo ndi anzeru kwambiri.
هر چند صور برای خود استحکاماتی ساخته و آنقدر ثروت جمع کرده که نقره و طلا برای او چون ریگ بیابان است، | 3 |
Ndipo Turo anadzimangira linga; wadziwunjikira siliva ngati fumbi, ndi golide ngati zinyalala za mʼmisewu.
ولی خداوند همهٔ این چیزها را از او خواهد گرفت. استحکاماتش را به دریا خواهد ریخت و او را به آتش کشیده با خاک یکسان خواهد کرد. | 4 |
Taonani Ambuye adzamulanda chuma chakecho ndi kuwononga mphamvu zake mʼnyanja, ndipo adzapserera ndi moto.
وقتی اشقلون این واقعه را ببیند وحشتزده خواهد شد. غزه از درد به خود خواهد پیچید و عقرون از ترس خواهد لرزید، زیرا وقتی ببینند صور قادر نیست جلوی پیشروی دشمنان را بگیرد، امیدشان بر باد خواهد رفت. غزه شکست خواهد خورد و پادشاهش کشته خواهد شد، و اشقلون خالی از سکنه خواهد شد. | 5 |
Mzinda wa Asikeloni udzaona zimenezi, nʼkuchita mantha; Gaza adzanjenjemera ndi ululu, chimodzimodzinso Ekroni, chifukwa chiyembekezo chake chidzatheratu. Mfumu ya ku Gaza idzaphedwa ndipo Asikeloni adzakhala opanda anthu.
اجنبیان شهر اَشدود را تسخیر خواهند کرد، و من غرور فلسطینیان را در هم خواهم شکست. | 6 |
Mu Asidodi mudzakhala mlendo, ndipo ndidzathetsa kunyada kwa Afilisti.
آنها دیگر گوشت حرام و گوشتی که هنوز خون در آن هست، نخواهند خورد. فلسطینیهایی که باقی بمانند مرا عبادت خواهند کرد و به عنوان یکی از طوایف یهودا در میان قوم من پذیرفته خواهند شد. فلسطینیهای عقرون نیز به قوم من خواهند پیوست، همانطور که یبوسیها سالها پیش این کار را کردند. | 7 |
Ndidzachotsa nyama ya magazi mʼkamwa mwawo, chakudya choletsedwa mʼmano mwawo. Amene atsala adzakhala anthu a Mulungu wathu, adzasanduka atsogoleri mu Yuda, ndipo Ekroni adzakhala ngati Ayebusi.
من در اطراف سرزمین خود نگهبانی خواهم داد تا از ورود سپاهیان مهاجم به خاک اسرائیل جلوگیری کنم. به دقت حرکات دشمن را زیر نظر میگیرم و اجازه نمیدهم ستمگران بیگانه بار دیگر سرزمین قوم مرا مورد تاخت و تاز قرار دهند. | 8 |
Koma Ine ndidzalondera Nyumba yanga ndi kuyiteteza kwa ankhondo osakaza. Palibenso mdani amene adzagonjetse anthu anga, pakuti tsopano ndikuwayangʼanira.
«ای دختر صهیون، شادی کن! ای اورشلیم فریاد پیروزی برآور! اینک پادشاهت نزد تو میآید؛ او عادل و پیروزمند است، اما فروتن و سوار بر الاغ، بر کرّه الاغ. | 9 |
Sangalala kwambiri, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni! Fuwula, mwana wamkazi wa Yerusalemu! Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe, yolungama ndi yogonjetsa adani, yodzichepetsa ndi yokwera pa bulu, pa mwana wamphongo wa bulu.
ارابههای جنگی را از اسرائیل و اسبهای جنگی را از اورشلیم برخواهم داشت، و کمانهای جنگ شکسته خواهند شد، زیرا پادشاه شما در میان تمام قومها صلح برقرار خواهد کرد. قلمرو حکومت او از دریا تا دریا و از رود فرات تا دورترین نقطهٔ زمین خواهد بود. | 10 |
Ndidzachotsa magaleta ankhondo ku Efereimu ndi akavalo ankhondo ku Yerusalemu, ndipo uta wankhondo udzathyoka. Mfumuyo idzabweretsa mtendere pakati pa mitundu ya anthu. Ulamuliro wake udzayambira ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina, ndipo kuchokera ku Mtsinje (Yufurate) mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
به خاطر عهدی که با شما بستم و آن را با خون مهر کردم، اسیران شما را از چاه هلاکت خواهم رهانید. | 11 |
Tsono kunena za iwe, chifukwa cha magazi a pangano lako ndi Ine, ndidzamasula amʼndende ako, ndidzawatulutsa mʼdzenje lopanda madzi.
ای اسیرانی که در انتظار آزادی هستید، به شهر امن خود بازگردید. امروز به شما قول میدهم که سختیهایی را که کشیدهاید دو برابر جبران کنم! | 12 |
Bwererani ku malo anu otetezedwa, inu amʼndende achiyembekezo; ngakhale tsopano ndikulengeza kuti ndidzakubwezerani zabwino mowirikiza.
ای یهودا، تو کمان من و ای اسرائیل، تو تیر من هستی. اورشلیم را همچون شمشیر سربازی شجاع بر ضد مردان یونان به حرکت درمیآورم.» | 13 |
Ndidzakoka Yuda monga ndimakokera uta wanga, ndipo Efereimu ndiye muvi wake. Ndidzadzutsa ana ako iwe Ziyoni, kulimbana ndi ana ako iwe Grisi, ndipo ndidzakusandutsa iwe lupanga la munthu wankhondo.
خداوند قوم خود را هنگام جنگ رهبری خواهد کرد. تیرهایش را مثل برق آسمان خواهد انداخت. خداوند یهوه شیپور جنگ را به صدا در خواهد آورد و مانند گردبادی که از صحرای جنوب بلند میشود، به جنگ دشمن خواهد رفت. | 14 |
Pamenepo Yehova adzaonekera kwa anthu ake; mivi yake idzangʼanima ngati chingʼaningʼani. Ambuye Yehova adzaliza lipenga; ndipo adzayenda mu mkuntho wochokera kummwera,
خداوند لشکرهای آسمان از قوم خود دفاع خواهد کرد و ایشان دشمنان خود را با سنگهای فلاخُن شکست خواهند داد. ایشان مانند مردان مست، در جنگ فریاد خواهند زد و خون دشمنانشان را خواهند ریخت، مانند خون قربانی که از پیاله بر مذبح ریخته میشود. | 15 |
ndipo Yehova Wamphamvuzonse adzawateteza. Iwo adzawononga ndipo adzagonjetsa ndi miyala ya legeni. Adzamwa magazi ndi kubangula ngati amwa vinyo; magazi adzayenderera ngati a mʼmbale yowazira magazi pa ngodya za guwa lansembe.
در آن روز، یهوه خدایشان آنها را خواهد رهانید، درست مانند چوپانی که گوسفندانش را میرهاند. ایشان مانند نگینهای تاج، در سرزمین او خواهند درخشید. | 16 |
Tsiku limenelo Yehova Mulungu wawo adzawapulumutsa pakuti anthu ake ali ngati nkhosa. Adzanyezimira mʼdziko lake ngati miyala yokongola pa chipewa chaufumu.
ببینید چه عالی و زیبا هستند! گندم، مردان جوان را شکوفا خواهد ساخت و شراب تازه، دوشیزگان را. | 17 |
Taonani chikoka ndi kukongola kwawo! Tirigu adzasangalatsa anyamata, ndi vinyo watsopano anamwali.