< زکریا 5 >
بار دیگر به آسمان چشم دوختم و طوماری را در حال پرواز دیدم. | 1 |
Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.
فرشته از من پرسید: «چه میبینی؟» جواب دادم: «طوماری میبینم به طول ده متر و عرض پنج متر که در حال پرواز است.» | 2 |
Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”
گفت: «این طومار لعنتهای خدا را در بردارد و آنها را به سراسر جهان میبرد. نوشتهٔ روی آن نشان میدهد که تمام دزدان و دروغگویان محکوم به مرگ هستند.» | 3 |
Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso.
خداوند لشکرهای آسمان میفرماید که این لعنتها را به خانهٔ کسانی که دزدی میکنند و آنهایی که به نام او قسم دروغ میخورند، میفرستد تا بر خانههایشان قرار بگیرد و آنها را به کلی نابود کند. | 4 |
Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’”
فرشته بار دیگر ظاهر شد و گفت: «بالا را نگاه کن. چیز دیگری در حال پرواز است.» | 5 |
Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”
پرسیدم: «آن چیست؟» جواب داد: «یک بشکهٔ بزرگ است. این بشکه پر است از گناهانی که سراسر زمین را فرا گرفتهاند.» | 6 |
Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?” Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”
ناگهان سرپوش سنگین سربی بشکه کنار رفت و من توانستم زنی را که در بشکه نشسته بود ببینم! | 7 |
Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi.
فرشته گفت: «آن زن نشانهٔ فساد و شرارت است.» آنگاه زن را به داخل بشکه هل داد و دوباره سرپوش سربی را روی آن گذاشت. | 8 |
Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.
سپس دو زن دیگر دیدم که بالهایی شبیه بالهای لکلک داشتند و پرواز میکردند. آنها آمده، بشکه را برداشتند و پروازکنان با خود بردند. | 9 |
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.
از فرشته پرسیدم: «بشکه را کجا میبرند؟» | 10 |
Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”
جواب داد: «آن را به بابِل میبرند تا جایگاهی برای آن بسازند و بشکه را در آن قرار دهند.» | 11 |
Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”