< مزامیر 83 >
سرود. مزمور آساف. ای خدا، خاموش نباش! هنگامی که دعا میکنیم، ساکت و آرام ننشین. | 1 |
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
ببین چگونه دشمنانت شورش میکنند و آنانی که از تو نفرت دارند به مخالفت و دشمنی برخاستهاند. | 2 |
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
آنها بر ضد قوم خاص تو نقشههای پلید میکشند و برای کسانی که به تو پناه آوردهاند، توطئه میچینند. | 3 |
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
میگویند: «بیایید قوم اسرائیل را نابود کنیم تا نامش برای همیشه محو شود.» | 4 |
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
همهٔ دشمنان با نقشهٔ نابودی ما موافقت نمودهاند و بر ضد تو همدست شدهاند: | 5 |
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
ادومیان، اسماعیلیان، موآبیان، هاجریان، | 6 |
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
مردمان سرزمینهای جِبال، عمون، عمالیق، فلسطین و صور. | 7 |
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
آشور نیز با آنها متحد شده و از عمون و موآب که از نسل لوط هستند حمایت میکند. | 8 |
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
خداوندا، همان بلایی را که در درهٔ قیشون بر سر مدیان و سیسرا و یابین آوردی، بر سر این دشمنان نیز بیاور. | 9 |
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
همانگونه که مخالفان ما را در «عین دور» از بین بردی و جنازههایشان در روی زمین ماند و کود زمین شد، این دشمنان متحد را نیز نابود کن. | 10 |
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
فرماندهان این دشمنان را به سرنوشت غراب و ذئب دچار ساز. همهٔ بزرگان آنان را مانند ذبح و صلمونع هلاک ساز | 11 |
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
همان کسانی که قصد داشتند ملک خدا را تصاحب کنند. | 12 |
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
ای خدا، دشمنان ما را همچون کاه و غبار در برابر باد، پراکنده ساز. | 13 |
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
چنانکه آتش در جنگل و در کوهستان افروخته میشود و همه چیز را میسوزاند، | 14 |
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
همچنان، ای خدا، آنها را با تندباد غضب خود بران و با طوفان خشم خویش آنها را آشفته و پریشان کن. | 15 |
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
خداوندا، آنها را چنان رسوا کن تا تسلیم تو شوند. | 16 |
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
آنها را در انجام نقشههایشان با شکست مواجه ساز. بگذار در ننگ و رسوایی جان بسپارند | 17 |
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
و بدانند که تنها تو که نامت یهوه است، در سراسر جهان متعال هستی. | 18 |
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.