< مزامیر 83 >

سرود. مزمور آساف. ای خدا، خاموش نباش! هنگامی که دعا می‌کنیم، ساکت و آرام ننشین. 1
Nyimbo. Salimo la Asafu. Inu Mulungu musakhale chete; musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
ببین چگونه دشمنانت شورش می‌کنند و آنانی که از تو نفرت دارند به مخالفت و دشمنی برخاسته‌اند. 2
Onani adani anu akuchita chiwawa, amene amadana nanu autsa mitu yawo.
آنها بر ضد قوم خاص تو نقشه‌های پلید می‌کشند و برای کسانی که به تو پناه آورده‌اند، توطئه می‌چینند. 3
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu; Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
می‌گویند: «بیایید قوم اسرائیل را نابود کنیم تا نامش برای همیشه محو شود.» 4
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”
همهٔ دشمنان با نقشهٔ نابودی ما موافقت نموده‌اند و بر ضد تو همدست شده‌اند: 5
Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu; Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
ادومیان، اسماعیلیان، موآبیان، هاجریان، 6
Matenti a Edomu ndi Aismaeli, Mowabu ndi Ahagiri,
مردمان سرزمینهای جِبال، عمون، عمالیق، فلسطین و صور. 7
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki, Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
آشور نیز با آنها متحد شده و از عمون و موآب که از نسل لوط هستند حمایت می‌کند. 8
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo kupereka mphamvu kwa ana a Loti. (Sela)
خداوندا، همان بلایی را که در درهٔ قیشون بر سر مدیان و سیسرا و یابین آوردی، بر سر این دشمنان نیز بیاور. 9
Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani, monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
همان‌گونه که مخالفان ما را در «عین دور» از بین بردی و جنازه‌هایشان در روی زمین ماند و کود زمین شد، این دشمنان متحد را نیز نابود کن. 10
Amene anawonongedwa ku Endori ndi kukhala ngati zinyalala.
فرماندهان این دشمنان را به سرنوشت غراب و ذئب دچار ساز. همهٔ بزرگان آنان را مانند ذبح و صلمونع هلاک ساز 11
Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
همان کسانی که قصد داشتند ملک خدا را تصاحب کنند. 12
amene anati, “Tiyeni tilande dziko la msipu la Mulungu.”
ای خدا، دشمنان ما را همچون کاه و غبار در برابر باد، پراکنده ساز. 13
Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga, ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
چنانکه آتش در جنگل و در کوهستان افروخته می‌شود و همه چیز را می‌سوزاند، 14
Monga moto umatentha nkhalango, kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
همچنان، ای خدا، آنها را با تندباد غضب خود بران و با طوفان خشم خویش آنها را آشفته و پریشان کن. 15
kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho, ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
خداوندا، آنها را چنان رسوا کن تا تسلیم تو شوند. 16
Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.
آنها را در انجام نقشه‌هایشان با شکست مواجه ساز. بگذار در ننگ و رسوایی جان بسپارند 17
Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse; awonongeke mwa manyazi.
و بدانند که تنها تو که نامت یهوه است، در سراسر جهان متعال هستی. 18
Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova, ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

< مزامیر 83 >