< مزامیر 8 >

برای رهبر سرایندگان: مزمور داوود، در مایۀ گیتّیت. ای خداوند، ای خداوند ما، شکوه نام تو سراسر زمین را فرا گرفته است! عظمت تو از آسمانها نیز فراتر رفته است. 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
کودکان و شیرخوارگان، زبان به ستایش تو می‌گشایند و دشمنانت را سرافکنده و خاموش می‌سازند. 2
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
وقتی به آسمان تو و به ماه و ستارگانی که آفریده‌ای نگاه می‌کنم، 3
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
می‌گویم انسان چیست که تو به فکرش باشی، و پسر انسان، که او را مورد لطف خود قرار دهی؟ 4
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
تو مقام او را فقط اندکی پایین‌تر از فرشتگان قرار دادی و تاج عزت و احترام را بر سر وی نهادی. 5
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
او را بر تمام خلقت خود گماردی و همه چیز را زیر فرمان او درآوردی: 6
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
گوسفندان و گاوان، حیوانات وحشی، 7
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
پرندگان آسمان، ماهیان دریا و جاندارانی که در آبها زندگی می‌کنند. 8
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
ای یهوه، خداوند ما، شکوه نام تو سراسر زمین را فرا گرفته است. 9
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< مزامیر 8 >