< مزامیر 78 >

قصیدۀ آساف. ای قوم من، به تعالیم من گوش فرا دهید و به آنچه می‌گویم توجه نمایید. 1
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
زیرا می‌خواهم با مَثَلها سخن گویم. می‌خواهم معماهای قدیمی را برایتان شرح دهم. 2
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
می‌خواهم آنچه را که از نیاکان خود شنیده‌ام تعریف کنم. 3
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
اینها را باید تعریف کنیم و مخفی نسازیم تا فرزندان ما نیز بدانند که خداوند با قدرت خود چه کارهای شگفت‌انگیز و تحسین برانگیزی انجام داده است. 4
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
خدا احکام و دستورهای خود را به قوم اسرائیل داد و به ایشان امر فرمود که آنها را به فرزندانشان بیاموزند 5
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
و فرزندان ایشان نیز به نوبهٔ خود آن احکام را به فرزندان خود تعلیم دهند تا به این ترتیب هر نسلی با احکام و دستورهای خدا آشنا گردد. 6
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
به این ترتیب آنها یاد می‌گیرند که بر خدا توکل نمایند و کارهایی را که او برای نیاکانشان انجام داده است، فراموش نکنند و پیوسته مطیع دستورهایش باشند. 7
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
در نتیجه آنها مانند نیاکان خود مردمی سرکش و یاغی نخواهند شد که ایمانی سست و ناپایدار داشتند و نسبت به خدا وفادار نبودند. 8
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
افراد قبیلهٔ افرایم با وجود اینکه به تیر و کمان مجهز بودند و در تیراندازی مهارت خاص داشتند، هنگام جنگ پا به فرار نهادند. 9
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
آنان پیمان خود را که با خدا بسته بودند، شکستند و نخواستند مطابق دستورهای او زندگی کنند. 10
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
کارها و معجزات او را که برای ایشان و نیاکانشان در مصر انجام داده بود، فراموش کردند، 11
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
کارهای شگفت‌انگیزی که برای نیاکانشان در دشت صوعن در سرزمین مصر انجام داده بود. 12
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
خدا دریای سرخ را شکافت و آبها را مانند دیوار بر پا نگه داشت تا ایشان از آن عبور کنند. 13
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
بنی‌اسرائیل را در روز به‌وسیلۀ ستون ابر راهنمایی می‌کرد و در شب توسط روشنایی آتش! 14
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
در بیابان صخره‌ها را شکافت و برای آنها آب فراهم آورد. 15
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
بله، از صخره چشمه‌های آب جاری ساخت! 16
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
ولی با وجود این، ایشان بار دیگر نسبت به خدای متعال گناه ورزیدند و در صحرا از فرمان او سر پیچیدند. 17
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
آنها خدا را امتحان کردند و از او خوراک خواستند. 18
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
حتی بر ضد خدا حرف زدند و گفتند: «آیا خدا می‌تواند در این بیابان برای ما خوراک تهیه کند؟ 19
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
درست است که او از صخره آب بیرون آورد و بر زمین جاری ساخت، ولی آیا می‌تواند نان و گوشت را نیز برای قوم خود فراهم کند؟» 20
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
خداوند چون این را شنید غضبناک شد و آتش خشم او علیه اسرائیل شعله‌ور گردید، 21
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
زیرا آنها ایمان نداشتند که خدا قادر است احتیاج آنها را برآورد. 22
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
با وجود این، خدا درهای آسمان را گشود 23
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
و نان آسمانی را برای ایشان بارانید تا بخورند و سیر شوند. 24
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
بله، آنها خوراک فرشتگان را خوردند و تا آنجا که می‌توانستند بخورند خدا به ایشان عطا فرمود. 25
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
سپس با قدرت الهی خود، بادهای شرقی و جنوبی را فرستاد 26
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
تا پرندگان بی‌شماری همچون شنهای ساحل دریا برای قوم او بیاورند. 27
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
پرندگان در اردوی اسرائیل، اطراف خیمه‌ها فرود آمدند. 28
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
پس خوردند و سیر شدند؛ آنچه را که خواستند خدا به ایشان داد. 29
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
اما پیش از آنکه هوس آنها ارضا شود، در حالی که هنوز غذا در دهانشان بود، 30
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
غضب خدا بر ایشان افروخته شد و شجاعان و جوانان اسرائیل را کشت. 31
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
با وجود این همه معجزات، بنی‌اسرائیل باز نسبت به خدا گناه کردند و به کارهای شگفت‌انگیز او ایمان نیاوردند. 32
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
بنابراین خدا کاری کرد که آنها روزهایشان را در بیابان تلف کنند و عمرشان را با ترس و لرز بگذرانند. 33
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
هنگامی که خدا عده‌ای از آنان را کشت بقیه توبه کرده، به سوی او بازگشت نمودند 34
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
و به یاد آوردند که خدای متعال پناهگاه و پشتیبان ایشان است. 35
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
اما توبهٔ آنها از صمیم قلب نبود؛ آنها به خدا دروغ گفتند. 36
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
دل بنی‌اسرائیل از خدا دور بود و آنها نسبت به عهد او وفادار نماندند. 37
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
اما خدا باز بر آنها ترحم فرموده، گناه ایشان را بخشید و آنها را از بین نبرد. بارها غضب خود را از بنی‌اسرائیل برگردانید، 38
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
زیرا می‌دانست که ایشان بشر فانی هستند و عمرشان دمی بیش نیست. 39
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
بنی‌اسرائیل در بیابان چندین مرتبه سر از فرمان خداوند پیچیدند و او را رنجاندند. 40
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
بارها و بارها خدای مقدّس اسرائیل را آزمایش کردند و به او بی‌حرمتی نمودند. 41
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
قدرت عظیم او را فراموش کردند و روزی را که او ایشان را از دست دشمن رهانیده بود به یاد نیاوردند. 42
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
بلاهایی را که او در منطقهٔ صوعن بر مصری‌ها نازل کرده بود، فراموش کردند. 43
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
در آن زمان خدا آبهای مصر را به خون تبدیل نمود تا مصری‌ها نتوانند از آن بنوشند. 44
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
انواع پشه‌ها را به میان مصری‌ها فرستاد تا آنها را بگزند. خانه‌های آنها را پر از قورباغه کرد. 45
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
محصولات و مزارع ایشان را به‌وسیلۀ کرم و ملخ از بین برد. 46
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
تاکستانها و درختان انجیرشان را با تگرگ درشت خراب کرد. 47
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
رمه‌ها و گله‌هایشان را با رعد و برق و تگرگ تلف کرد. 48
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
او آتش خشم خود را همچون فرشتگان مرگ به جان ایشان فرستاد. 49
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
او غضب خود را از ایشان باز نداشت بلکه بلایی فرستاد و جان آنها را گرفت. 50
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
همهٔ پسران نخست‌زادهٔ مصری را کشت. 51
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
آنگاه بنی‌اسرائیل را از مصر بیرون آورد و آنها را همچون گلهٔ گوسفند به بیابان هدایت کرد. 52
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
ایشان را به راههای امن و بی‌خطر راهنمایی کرد تا نترسند؛ اما دشمنان آنها در دریای سرخ غرق شدند. 53
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
سرانجام خدا اجداد ما را به این سرزمین مقدّس آورد، یعنی همین کوهستانی که با دست توانای خود آن را تسخیر نمود. 54
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
ساکنان این سرزمین را از پیش روی ایشان بیرون راند؛ سرزمین موعود را بین قبایل اسرائیل تقسیم نمود و به آنها اجازه داد که در خانه‌های آنجا سکونت گزینند. 55
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
اما با این همه، خدای متعال را امتحان کردند و از فرمان او سر پیچیدند و دستورهایش را اجرا نکردند. 56
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
مانند اجداد خود از خدا روی برتافتند و به او خیانت کردند و همچون کمانی کج، غیرقابل اعتماد شدند. 57
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
بتکده‌ها ساختند و به پرستش بتها پرداختند و به این وسیله خشم خداوند را برانگیختند. 58
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
وقتی خدا چنین بی‌وفایی از اسرائیل دید، بسیار غضبناک گردید و آنها را به کلی طرد کرد. 59
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
خیمهٔ عبادت را که در شیلوه بر پا ساخته بود ترک کرد 60
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
و صندوق مقدّس را که مظهر قدرت و حضورش در بین اسرائیل بود، به دست دشمن سپرد. 61
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
بر قوم برگزیدهٔ خویش غضبناک گردید و آنها را به دم شمشیر دشمنان سپرد. 62
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
جوانانشان در آتش جنگ سوختند و دخترانشان لباس عروسی بر تن نکردند. 63
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
کاهنانشان به دم شمشیر افتادند و زنهایشان نتوانستند برای آنها سوگواری کنند. 64
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
سرانجام خداوند همچون کسی که از خواب بیدار شود، و مانند شخص نیرومندی که از باده سرخوش گردد، به یاری اسرائیل برخاست. 65
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
دشمنان قوم خود را شکست داده، آنها را برای همیشه رسوا ساخت. 66
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
او فرزندان یوسف و قبیلهٔ افرایم را طرد نمود 67
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
اما قبیلهٔ یهودا و کوه صهیون را که از قبل دوست داشت، برگزید. 68
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
در آنجا خانهٔ مقدّس خود را مانند کوههای محکم و پابرجای دنیا، جاودانه بر پا نمود. 69
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
سپس خدمتگزار خود داوود را که گوسفندان پدرش را می‌چرانید، برگزید. 70
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
او را از چوپانی گرفت و به پادشاهی اسرائیل نصب نمود. 71
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
داوود با صمیم قلب از اسرائیل مراقبت نمود و با مهارت کامل ایشان را رهبری کرد. 72
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.

< مزامیر 78 >