< مزامیر 55 >
برای رهبر سرایندگان: با همراهی سازهای زهی. قصیدۀ داوود. خدایا، به دعای من گوش فرا ده. هنگامی که نزد تو ناله میکنم، خود را پنهان نکن. | 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
دعایم را بشنو و آن را مستجاب فرما، زیرا از شدت پریشانی فکر، نمیدانم چه کنم. | 2 |
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
تهدید دشمنان و ظلم بدکاران، خاطرم را آشفته کرده است. آنان با خشم و نفرت با من رفتار میکنند و مرا عذاب میدهند. | 3 |
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
ترس بر قلبم چنگ انداخته و مرا بیقرار کرده؛ وحشت مرگ سراسر وجودم را فرا گرفته است. | 4 |
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
از شدت ترس و لرز نزدیک است قالب تهی کنم. | 5 |
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
به خود میگویم: «ای کاش همچون کبوتر بال میداشتم تا به جایی دور در صحرا پرواز میکردم و در آنجا پنهان میشدم و استراحت میکردم؛ | 6 |
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
میشتافتم به سوی پناهگاهی و از تندباد و طوفان حوادث در امان میماندم.» | 8 |
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
خداوندا، این شریران را چنان پریشان کن که زبان یکدیگر را نفهمند، زیرا آنان شهر را از خشونت و ظلم پر ساختهاند. | 9 |
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
آنان روز و شب شهر را دور میزنند و شرارت و جنایت میآفرینند. | 10 |
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
شهر پر از ظلم و فساد است و حیله و فریب از کوچهها دور نمیشود. | 11 |
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
این دشمن من نیست که به من توهین میکند، و گرنه تحمل میکردم؛ این حریف من نیست که بر من برخاسته، و گرنه خود را از او پنهان میکردم. | 12 |
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
این تو هستی ای دوست صمیمی و همکار من! | 13 |
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
ما با یکدیگر رفاقت صادقانه داشتیم، با یکدیگر درد دل میکردیم و با هم به خانهٔ خدا میرفتیم. | 14 |
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
باشد که دشمنانم پیش از وقت، زنده به گور شوند، زیرا دلها و خانههایشان پر از شرارت است. (Sheol ) | 15 |
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol )
اما من از خدا کمک میطلبم و او نجاتم خواهد داد. | 16 |
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
صبح، ظهر و شب به پیشگاه خدا مینالم و شکایت میکنم و او صدای مرا خواهد شنید. | 17 |
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
هر چند دشمنان من زیادند، اما او مرا در جنگ با آنها پیروز خواهد ساخت و به سلامت باز خواهد گرداند. | 18 |
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
خدایی که از ازل بر تخت فرمانروایی نشسته است دعایم را خواهد شنید و آنها را شکست خواهد داد، زیرا آنها از خدا نمیترسند و نقشههای پلید خود را تغییر نمیدهند. | 19 |
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
دوست و همکار سابق من دست خود را بر روی دوستانش بلند میکند و عهد دوستی خود را میشکند. | 20 |
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
زبانش چرب است اما در باطنش کینه و نفرت هست. سخنانش از روغن نیز نرمتر است اما همچون شمشیر میبرد و زخمی میکند. | 21 |
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
نگرانی خود را به خدا واگذار و او تو را حفظ خواهد کرد. خداوند هرگز نخواهد گذاشت که عادلان بلغزند و بیفتند. | 22 |
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
اما تو ای خدا، این اشخاص خونخوار و نیرنگباز را پیش از وقت به گور خواهی فرستاد. ولی من بر تو توکل دارم. | 23 |
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.