< مزامیر 55 >

برای رهبر سرایندگان: با همراهی سازهای زهی. قصیدۀ داوود. خدایا، به دعای من گوش فرا ده. هنگامی که نزد تو ناله می‌کنم، خود را پنهان نکن. 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya Davide. Pa zoyimbira za zingwe. Mvetserani pemphero langa, Inu Mulungu, musakufulatire kupempha kwanga,
دعایم را بشنو و آن را مستجاب فرما، زیرا از شدت پریشانی فکر، نمی‌دانم چه کنم. 2
mverani ndipo mundiyankhe. Maganizo anga akundisautsa ndipo ndathedwa nzeru
تهدید دشمنان و ظلم بدکاران، خاطرم را آشفته کرده است. آنان با خشم و نفرت با من رفتار می‌کنند و مرا عذاب می‌دهند. 3
chifukwa cha mawu a adani anga, chifukwa cha kupondereza kwa anthu oyipa; pakuti andidzetsera masautso ndipo akundizunza mu mkwiyo wawo.
ترس بر قلبم چنگ انداخته و مرا بی‌قرار کرده؛ وحشت مرگ سراسر وجودم را فرا گرفته است. 4
Mtima wanga ukupweteka mʼkati mwanga; mantha a imfa andigwera.
از شدت ترس و لرز نزدیک است قالب تهی کنم. 5
Mantha ndi kunjenjemera zandizinga; mantha aakulu andithetsa nzeru.
به خود می‌گویم: «ای کاش همچون کبوتر بال می‌داشتم تا به جایی دور در صحرا پرواز می‌کردم و در آنجا پنهان می‌شدم و استراحت می‌کردم؛ 6
Ndinati, “Ndithu, ndikanakhala ndi mapiko ankhunda! Ndikanawulukira kutali ndi kukapuma.
7
Ndikanathawira kutali ndi kukakhala mʼchipululu.
می‌شتافتم به سوی پناهگاهی و از تندباد و طوفان حوادث در امان می‌ماندم.» 8
Ndikanathamangira kumalo anga a chitetezo; kutali ndi mphepo yaukali ndi yamkuntho.”
خداوندا، این شریران را چنان پریشان کن که زبان یکدیگر را نفهمند، زیرا آنان شهر را از خشونت و ظلم پر ساخته‌اند. 9
Sokonezani maganizo a oyipa, Inu Ambuye, tsutsani mawu awo; pakuti ine ndikuona chiwawa ndi mkangano mu mzinda.
آنان روز و شب شهر را دور می‌زنند و شرارت و جنایت می‌آفرینند. 10
Usana ndi usiku iwo akuzungulirazungulira pa makoma ake; nkhwidzi ndi kuzunza kuli mʼkati mwake.
شهر پر از ظلم و فساد است و حیله و فریب از کوچه‌ها دور نمی‌شود. 11
Mphamvu zowononga zili pa ntchito mu mzinda; kuopseza ndi mabodza sizichoka mʼmisewu yake.
این دشمن من نیست که به من توهین می‌کند، و گرنه تحمل می‌کردم؛ این حریف من نیست که بر من برخاسته، و گرنه خود را از او پنهان می‌کردم. 12
Akanakhala mdani akundinyoza, ine ndikanapirira; akanakhala mdani akudzikweza yekha kutsutsana nane, ndikanakabisala.
این تو هستی ای دوست صمیمی و همکار من! 13
Koma iweyo mnzanga, mnzanga woyenda naye, bwenzi langa la pondaapanʼpondepo, ndi amene ukuchita zimenezi.
ما با یکدیگر رفاقت صادقانه داشتیم، با یکدیگر درد دل می‌کردیم و با هم به خانهٔ خدا می‌رفتیم. 14
Mnzanga amene nthawi ina tinkasangalala pa chiyanjano chokoma ku nyumba ya Mulungu.
باشد که دشمنانم پیش از وقت، زنده به گور شوند، زیرا دلها و خانه‌هایشان پر از شرارت است. (Sheol h7585) 15
Mulole imfa itenge adani anga mwadzidzidzi; alowe mʼmanda ali amoyo pakuti choyipa chili pakati pawo. (Sheol h7585)
اما من از خدا کمک می‌طلبم و او نجاتم خواهد داد. 16
Koma ine ndinafuwulira kwa Mulungu, ndipo Yehova anandipulumutsa.
صبح، ظهر و شب به پیشگاه خدا می‌نالم و شکایت می‌کنم و او صدای مرا خواهد شنید. 17
Madzulo, mmawa ndi masana ndimalira mowawidwa mtima, ndipo Iye amamva mawu anga.
هر چند دشمنان من زیادند، اما او مرا در جنگ با آنها پیروز خواهد ساخت و به سلامت باز خواهد گرداند. 18
Iye amandiwombola ine osavulazidwa pa nkhondo imene yafika kulimbana nane, ngakhale kuti ndi ambiri amene akunditsutsa.
خدایی که از ازل بر تخت فرمانروایی نشسته است دعایم را خواهد شنید و آنها را شکست خواهد داد، زیرا آنها از خدا نمی‌ترسند و نقشه‌های پلید خود را تغییر نمی‌دهند. 19
Mulungu amene ali pa mpando wake kwamuyaya, adzandimenyera nkhondo; adzawatsitsa adani anga, chifukwa safuna kusintha njira zawo zoyipa ndipo saopa Mulungu.
دوست و همکار سابق من دست خود را بر روی دوستانش بلند می‌کند و عهد دوستی خود را می‌شکند. 20
Mnzanga woyenda naye wathira nkhondo abwenzi ake; iye akuphwanya pangano ake.
زبانش چرب است اما در باطنش کینه و نفرت هست. سخنانش از روغن نیز نرمتر است اما همچون شمشیر می‌برد و زخمی می‌کند. 21
Mawu ake ndi osalala kuposa batala komabe nkhondo ili mu mtima mwake; mawu ake ndi osalala kwambiri kuposa mafuta, komatu mawuwo ndi malupanga osololoka.
نگرانی خود را به خدا واگذار و او تو را حفظ خواهد کرد. خداوند هرگز نخواهد گذاشت که عادلان بلغزند و بیفتند. 22
Tulani nkhawa zanu kwa Yehova ndipo Iye adzakulimbitsani; Iye sadzalola kuti wolungama agwe.
اما تو ای خدا، این اشخاص خونخوار و نیرنگ‌باز را پیش از وقت به گور خواهی فرستاد. ولی من بر تو توکل دارم. 23
Koma Inu Mulungu mudzawatsitsa anthu oyipa kulowa mʼdzenje lachiwonongeko; anthu okhetsa magazi ndi anthu achinyengo sadzakhala moyo theka la masiku awo, koma ine ndimadalira Inu.

< مزامیر 55 >