< مزامیر 14 >

برای رهبر سرایندگان. مزمور داوود. کسی که فکر می‌کند خدایی نیست، ابله است. چنین شخصی فاسد است و دست به کارهای پلید می‌زند و هیچ نیکی در او نیست. 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Chitsiru chimati mu mtima mwake, “Kulibe Mulungu.” Oterewa ndi oyipa ndipo ntchito zawo ndi zonyansa; palibe amene amachita zabwino.
خداوند از آسمان به انسانها نگاه می‌کند تا شخص فهمیده‌ای بیابد که طالب خدا باشد. 2
Yehova kumwamba wayangʼana pansi, kuyangʼana anthu onse kuti aone ngati alipo wina wanzeru, amene amafunafuna Mulungu.
اما همه گمراه شده‌اند، همه فاسد گشته‌اند، نیکوکاری نیست، حتی یک نفر. 3
Onse atembenukira kumbali, onse pamodzi asanduka oyipa; palibe amene amachita zabwino, palibiretu ndi mmodzi yemwe.
آیا این بدکاران شعور ندارند؟ آنها که قوم مرا مانند نان می‌بلعند و می‌خورند و هرگز خداوند را نمی‌طلبند؟ 4
Kodi anthu ochita zoyipawa sadziwa chilichonse? Akudya anthu anga ngati chakudya chawo ndipo satamanda Yehova?
ولی وحشت، آنها را فرا می‌گیرد زیرا خدا با درستکاران است. 5
Awo ali apowo, agwidwa ndi mantha aakulu, pakuti Mulungu ali mʼgulu la olungama.
بله، وقتی بدکاران امید آدم بیچاره را نقش بر آب می‌کنند، خداوند او را در پناه خود می‌گیرد. 6
Inu ochita zoyipa mumalepheretsa chikonzero cha anthu osauka, koma Yehova ndiye pothawirapo pawo.
کاش که نجات برای اسرائیل از صهیون فرا می‌رسید و خداوند سعادت گذشته را به قوم خود باز می‌گردانید! بگذار یعقوب شادی کند و اسرائیل به وجد آید! 7
Ndithu, chipulumutso cha Israeli chidzachokera ku Ziyoni! Pamene Yehova abwezeretsa ufulu wa anthu ake, Yakobo akondwere ndipo Israeli asangalale!

< مزامیر 14 >