< امثال 28 >

شریران می‌گریزند، در حالی که کسی آنها را تعقیب نمی‌کند! ولی خداشناسان چون شیر، شجاع هستند. 1
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
وقتی مملکتی گرفتار فساد شود، دولتش به آسانی سرنگون می‌گردد، اما رهبران درستکار و عاقل مایهٔ ثبات مملکت هستند. 2
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
حاکمی که بر فقرا ظلم می‌کند مانند باران تندی است که محصول را از بین می‌برد. 3
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
بی‌توجهی نسبت به قانون، ستایش بدکاران است ولی اطاعت از آن، مبارزه با بدی می‌باشد. 4
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
عدالت برای بدکاران بی‌معنی است، اما پیروان خداوند اهمیت آن را خوب می‌دانند. 5
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
انسان بهتر است فقیر و درستکار باشد تا ثروتمند و کلاهبردار. 6
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
پسری که از قوانین اطاعت می‌کند داناست، اما کسی که رفیق عیاشان است مایهٔ ننگ پدرش می‌باشد. 7
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
مالی که از راه رباخواری و بهره‌کشی از فقرا حاصل شود عاقبت به دست کسی می‌افتد که بر فقرا رحم می‌کند. 8
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
خدا از دعای کسانی که احکام او را اطاعت نمی‌کنند، کراهت دارد. 9
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
هر که دام بر سر راه شخص درستکار بنهد و او را به راه بد بکشاند، عاقبت به دام خود گرفتار خواهد شد، ولی اشخاص نیک پاداش خوبی خواهند یافت. 10
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
ثروتمندان خود را دانا می‌پندارند، اما فقیر خردمند از واقعیت درون آنها باخبر است. 11
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
وقتی نیکان پیروز می‌شوند، همه شادی می‌کنند، اما هنگامی که بدکاران به قدرت می‌رسند، مردم خود را پنهان می‌کنند. 12
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
هر که گناه خود را بپوشاند، هرگز کامیاب نخواهد شد، اما کسی که آن را اعتراف کند و از آن دست بکشد خدا بر او رحم خواهد کرد. 13
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
خوشا به حال کسی که ترس خدا را در دل دارد، زیرا هر که نسبت به خدا سرسخت باشد گرفتار بلا و بدبختی می‌شود. 14
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
مردم بیچاره‌ای که زیر سلطهٔ حاکم ظالمی هستند، مانند کسانی می‌باشند که گرفتار شیر غران یا خرس گرسنه شده باشند. 15
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
سلطان نادان به قوم خود ظلم می‌کند. پادشاهی که از نادرستی و رشوه‌خواری نفرت داشته باشد، سلطنتش طولانی خواهد بود. 16
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
عذاب وجدان یک جنایتکار او را به سوی مجازات خواهد برد، پس تو سعی نکن از او حمایت کنی. 17
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
هر که در راه راست ثابت قدم باشد در امان خواهد ماند، اما کسی که به راههای کج برود خواهد افتاد. 18
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
هر که در زمین خود زراعت کند نان کافی خواهد داشت، اما کسی که وقت خود را به بطالت بگذراند فقر گریبانگیر او خواهد شد. 19
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
اشخاص درستکار کامیاب خواهند شد، اما کسانی که برای ثروتمند شدن عجله می‌کنند بی‌سزا نخواهند ماند. 20
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
طرفداری، کار درستی نیست؛ اما هستند قضاتی که به خاطر یک لقمه نان، بی‌انصافی می‌کنند. 21
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
آدم خسیس فقط به فکر جمع‌آوری ثروت است غافل از اینکه فقر در انتظار اوست. 22
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
اگر اشتباه کسی را به او گوشزد کنی، در آخر از تو بیشتر قدردانی خواهد کرد تا از کسی که پیش او چاپلوسی کرده است. 23
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
کسی که والدین خود را غارت می‌کند و می‌گوید: «کار بدی نکرده‌ام»، دست کمی از یک آدمکش ندارد. 24
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
حرص و طمع باعث جنگ و جدال می‌شود؛ اما توکل نمودن به خداوند انسان را کامیاب می‌کند. 25
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
هر که بر نقشه‌های خود تکیه می‌کند نادان است، ولی آنانی که از تعالیم خدا پیروی می‌نمایند، در امان می‌باشند. 26
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
اگر به فقرا کمک کنی، هرگز محتاج نخواهی شد؛ ولی اگر روی خود را از فقیر برگردانی، مورد لعنت قرار خواهی گرفت. 27
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
هنگامی که بدکاران به قدرت می‌رسند، مردم خود را پنهان می‌کنند، اما وقتی بدکاران سقوط کنند درستکاران دوباره قدرت را به دست خواهند گرفت. 28
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< امثال 28 >