< امثال 19 >

بهتر است انسان فقیر باشد و درستکار تا اینکه بدکار باشد و نادان. 1
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
داشتن دل و جرأت بدون حکمت بی‌فایده است و عجله باعث اشتباه می‌شود. 2
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
انسان با حماقتش زندگی خود را تباه می‌کند و بعد تقصیر را به گردن خداوند می‌اندازد. 3
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
شخص ثروتمند دوستان بسیار پیدا می‌کند، اما وقتی کسی فقیر می‌شود هیچ دوستی برایش باقی نمی‌ماند. 4
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
شاهد دروغگو بی‌سزا نمی‌ماند و کسی که دائم دروغ می‌بافد جان به در نخواهد برد. 5
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
مردم دوست دارند پیش بزرگان، خود شیرینی کنند و با کسانی دوست شوند که بذل و بخشش می‌کنند. 6
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
وقتی انسان فقیر شود حتی برادرانش او را ترک می‌کنند چه رسد به دوستانش، و تلاش او برای بازیافتن آنها به جایی نمی‌رسد. 7
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
هر که در پی حکمت است جانش را دوست دارد و آنکه برای حکمت ارزش قائل شود سعادتمند خواهد شد. 8
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
شاهد دروغگو بی‌سزا نمی‌ماند و هر که دائم دروغ می‌بافد هلاک خواهد شد. 9
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
شایسته نیست که آدم نادان در ناز و نعمت زندگی کند و یا یک برده بر امیران حکومت راند. 10
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
کسی که خشم خود را فرو می‌نشاند عاقل است و آنکه از تقصیرات دیگران چشم‌پوشی می‌کند سرافراز خواهد شد. 11
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
غضب پادشاه مانند غرش شیر است، اما خشنودی او مثل شبنمی است که بر سبزه می‌نشیند. 12
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
فرزند نادان بلای جان پدرش است و غرغرهای زن بهانه‌گیر مثل قطرات آبی است که دائم در حال چکیدن می‌باشد. 13
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
خانه و ثروت از اجداد به ارث می‌رسد، اما زن عاقل بخشش خداوند است. 14
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
کسی که تنبل است و زیاد می‌خوابد، گرسنه می‌ماند. 15
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
احکام خدا را نگه دار تا زنده بمانی، زیرا هر که آنها را خوار بشمارد خواهد مرد. 16
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
وقتی به فقیر کمک می‌کنی مثل این است که به خداوند قرض می‌دهی و خداوند است که قرض تو را پس خواهد داد. 17
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
فرزند خود را تا دیر نشده تربیت کن؛ اگر غفلت نمایی زندگی او را تباه خواهی کرد. 18
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
اگر کسی تندخویی می‌کند بگذار عواقبش را ببیند و مانع او نشو، چون در غیر این صورت او به تندخویی خود ادامه خواهد داد. 19
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
اگر به پند و اندرز گوش دهی تا آخر عمرت از حکمت برخوردار خواهی بود. 20
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
انسان نقشه‌های زیادی در سر می‌پروراند، اما نقشه‌هایی که مطابق با خواست خدا باشد اجرا خواهد شد. 21
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
آنچه مهم است محبت و وفاداری است. بهتر است شخص فقیر باشد تا اینکه با نادرستی زندگی کند. 22
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
خداترسی به انسان حیات می‌بخشد و او را کامیاب گردانده از هر بلایی محفوظ می‌دارد. 23
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
آدم تنبل دستش را به طرف بشقاب دراز می‌کند، ولی از فرط تنبلی لقمه را به دهان خود نمی‌گذارد. 24
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
مسخره کننده را تنبیه کن تا مایهٔ عبرت جاهلان شود. اشتباهات شخص فهمیده را به او گوشزد نما تا فهمیده‌تر شود. 25
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
پسری که با پدرش بدرفتاری می‌کند و مادرش را از خانه بیرون می‌راند، مایه ننگ و رسوایی است. 26
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
پسرم، از گوش دادن به تعلیمی که تو را از حکمت دور می‌کند خودداری نما. 27
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
شاهد پست و فرومایه عدالت را به بازی می‌گیرد و از گناه کردن لذت می‌برد. 28
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
مسخره‌کنندگان و احمقان، به شدت مجازات خواهند شد. 29
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< امثال 19 >