< اعداد 16 >

یک روز قورح پسر یصهار نوهٔ قهات از قبیلهٔ لاوی، با داتان و ابیرام پسران الیاب و اون پسر فالت که هر سه از قبیلهٔ رئوبین بودند با هم توطئه کردند که علیه موسی شورش کنند. دویست و پنجاه نفر از سران معروف اسرائیل که توسط مردم انتخاب شده بودند در این توطئه شرکت داشتند. 1
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
ایشان نزد موسی و هارون رفته گفتند: «شما از حد خود تجاوز می‌کنید! شما از هیچ‌کدام از ما بهتر نیستید. همهٔ قوم اسرائیل مقدّسند و خداوند با همگی ما می‌باشد؛ پس چه حقی دارید خود را در رأس قوم خداوند قرار دهید؟» 3
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
موسی وقتی سخنان ایشان را شنید به خاک افتاد. 4
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
سپس به قورح و آنانی که با او بودند گفت: «فردا صبح خداوند به شما نشان خواهد داد چه کسی به او تعلق دارد و مقدّس است. خداوند فقط به کسانی که خود برگزیده است اجازه خواهد داد به حضور او وارد شوند. 5
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
ای قورح، تو و تمام کسانی که با تو هستند فردا صبح، آتشدانها گرفته، آتش در آنها بگذارید و در حضور خداوند بخور در آنها بریزید. آنگاه خواهیم دید خداوند چه کسی را انتخاب کرده است. ای پسران لاوی، این شما هستید که از حد خود تجاوز می‌کنید!» 6
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
موسی به قورح و آنانی که با او بودند گفت: «ای لاویان گوش دهید. آیا به نظر شما این امر کوچکی است که خدای اسرائیل شما را از میان تمام قوم اسرائیل برگزیده است تا در خیمهٔ مقدّس خداوند کار کنید و به او نزدیک باشید و برای خدمت به قوم در حضور آنها بایستید؟ 8
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
آیا این وظیفه را که خداوند فقط به شما لاویان داده است ناچیز می‌دانید که اکنون خواهان مقام کاهنی هم هستید؟ 10
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
با این کار در واقع بر ضد خداوند قیام کرده‌اید. مگر هارون چه کرده است که از او شکایت می‌کنید؟» 11
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
بعد موسی به دنبال داتان و ابیرام پسران الیاب فرستاد، ولی آنها نیامدند 12
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
و در جواب گفتند: «مگر این امر کوچکی است که تو ما را از سرزمین حاصلخیز مصر بیرون آوردی تا در این بیابان بی‌آب و علف از بین ببری و حالا هم خیال داری بر ما حکومت کنی؟ 13
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
از این گذشته، هنوز که ما را به سرزمین حاصلخیزی که وعده داده بودی نرسانیده‌ای و مزرعه و تاکستانی به ما نداده‌ای. چه کسی را می‌خواهی فریب دهی؟ ما نمی‌خواهیم بیاییم.» 14
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
پس موسی بسیار خشمناک شده، به خداوند گفت: «قربانیهای ایشان را قبول نکن! من حتی الاغی هم از ایشان نگرفته‌ام و زیانی به یکی از آنها نرسانیده‌ام.» 15
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
موسی به قورح گفت: «تو و تمامی یارانت فردا صبح به حضور خداوند بیایید، هارون نیز اینجا خواهد بود. 16
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
فراموش نکنید آتشدانها را با خودتان آورده، بخور بر آنها بگذارید. هر کس یک آتشدان، یعنی جمعاً دویست و پنجاه آتشدان با خودتان بیاورید. هارون هم با آتشدان خود به حضور خداوند بیاید.» 17
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
آنها همین کار را کردند. همگی آتشدانهای خود را آورده، روشن کردند و بخور بر آنها گذاشتند و با موسی و هارون کنار مدخل خیمهٔ ملاقات ایستادند. 18
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
در این بین، قورح تمامی قوم اسرائیل را علیه موسی و هارون تحریک کرده بود و همگی آنها نزد در خیمۀ ملاقات جمع شده بودند. آنگاه حضور پرجلال خداوند بر تمام قوم اسرائیل نمایان شد. 19
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
خداوند به موسی و هارون فرمود: 20
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
«از کنار این قوم دور شوید تا بی‌درنگ آنها را هلاک کنم.» 21
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
ولی موسی و هارون رو به خاک نهاده، عرض کردند: «ای خدایی که خدای تمام افراد بشر هستی، آیا به خاطر گناه یک نفر، نسبت به تمامی قوم خشمگین می‌شوی؟» 22
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
خداوند به موسی فرمود: «پس به بنی‌اسرائیل بگو که از کنار خیمه‌های قورح و داتان و ابیرام دور شوند.» 23
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
24
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
پس موسی در حالی که مشایخ اسرائیل او را همراهی می‌کردند به سوی خیمه‌های داتان و ابیرام شتافت. 25
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
او به قوم اسرائیل گفت: «از اطراف خیمه‌های این مردان بدکار دور شوید و به چیزی که مال آنهاست دست نزنید مبادا شریک گناهان ایشان شده، با ایشان هلاک شوید.» 26
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
پس قوم اسرائیل از اطراف خیمه‌های قورح و داتان و ابیرام دور شدند. داتان و ابیرام با زنان و پسران و اطفال خود از خیمه‌هایشان بیرون آمده، دم در ایستادند. 27
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
موسی گفت: «حال خواهید دانست که خداوند مرا فرستاده است تا تمامی این کارها را انجام بدهم و اینکه به ارادهٔ خودم کاری نکرده‌ام. 28
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
اگر این مردان به مرگ طبیعی یا در اثر تصادف یا بیماری بمیرند، پس خداوند مرا نفرستاده است. 29
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
اما اگر خداوند معجزه‌ای نموده، زمین باز شود و ایشان را با هر چه که دارند ببلعد و زنده به گور شوند، آنگاه بدانید که این مردان به خداوند اهانت کرده‌اند.» (Sheol h7585) 30
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
به محض اینکه سخنان موسی تمام شد، ناگهان زمین زیر پای قورح و داتان و ابیرام دهان گشود 31
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
و آنها را با خانواده‌ها و همدستانی که با آنها ایستاده بودند، همراه با دار و ندارشان، فرو برد. 32
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
پس به این ترتیب، زمین بر ایشان به هم آمد و ایشان زنده به گور شدند و از بین رفتند. (Sheol h7585) 33
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
اسرائیلی‌هایی که نزدیک آنها ایستاده بودند از فریاد آنها پا به فرار گذاشتند، چون ترسیدند زمین، ایشان را هم به کام خود فرو برد. 34
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
سپس آتشی از جانب خداوند فرود آمد و آن دویست و پنجاه نفری را که بخور تقدیم می‌کردند، سوزانید. 35
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
خداوند به موسی فرمود: «به العازار پسر هارون کاهن بگو که آن آتشدانها را از داخل آتش بیرون آورد، چون آنها وقف خداوند شده، مقدّس می‌باشند. او باید خاکستر آتشدانهای این مردانی را که به قیمت جان خود گناه کردند دور بریزد. بعد آتشدانها را در هم کوبیده، از آن ورقه‌ای برای پوشش مذبح درست کند، زیرا این آتشدانها مقدّسند. این پوشش مذبح برای قوم اسرائیل، خاطرهٔ عبرت‌انگیزی خواهد بود.» 36
Yehova anawuza Mose kuti,
37
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
پس العازار کاهن، آن آتشدانهای مفرغین را گرفته، در هم کوبید و از آن ورقه‌ای فلزی برای پوشش مذبح ساخت، 39
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
تا برای قوم اسرائیل عبرتی باشد که هیچ‌کس، غیر از نسل هارون، جرأت نکند در حضور خداوند بخور بسوزاند، مبادا همان بلایی بر سرش آید که بر سر قورح و طرفدارانش آمد. بدین ترتیب آنچه خداوند به موسی فرموده بود، عملی گردید. 40
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
اما فردای همان روز، بنی‌اسرائیل دوباره علیه موسی و هارون زبان به شکایت گشودند و گفتند: «شما قوم خداوند را کشته‌اید!» 41
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
ولی وقتی آنها دور موسی و هارون را گرفته بودند ناگهان ابر، خیمۀ ملاقات را پوشاند و حضور پرجلال خداوند نمایان شد. 42
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
موسی و هارون آمدند و کنار در خیمهٔ ملاقات ایستادند و خداوند به موسی فرمود: 43
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
«از کنار این قوم دور شوید تا بی‌درنگ آنها را هلاک کنم.» ولی موسی و هارون در حضور خداوند به خاک افتادند. 45
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
موسی به هارون گفت: «آتشدان خود را برداشته، آتش از روی مذبح در آن بگذار و بخور بر آن بریز و فوراً به میان قوم ببر و برای ایشان کفاره کن تا گناهانشان آمرزیده شود، زیرا خشم خداوند بر ایشان افروخته و بلا شروع شده است.» 46
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
هارون مطابق دستور موسی عمل کرد و به میان قوم شتافت، زیرا بلا شروع شده بود، پس بخور بر آتش نهاد و برای ایشان کفاره نمود. 47
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
او بین زندگان و مردگان ایستاد و بلا متوقف شد. 48
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
با این حال، علاوه بر آنانی که روز پیش با قورح به هلاکت رسیده بودند چهارده هزار و هفتصد نفر دیگر هم مردند. 49
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
هارون نزد موسی به در خیمهٔ ملاقات بازگشت و بدین ترتیب بلا رفع شد. 50
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

< اعداد 16 >