< ناحوم 1 >
خداوند این رؤیا را که دربارهٔ نینوا است به ناحوم القوشی نشان داد: | 1 |
Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
یهوه خدایی غیور است و از کسانی که با وی مخالفت ورزند، انتقام میگیرد و با خشم شدید آنان را مجازات میکند. | 2 |
Yehova ndi Mulungu wansanje ndiponso wobwezera; Yehova amabwezera ndipo ndi waukali. Yehova amabwezera adani ake ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
خداوند دیر خشمگین میشود ولی گناه را هرگز بیسزا نمیگذارد. قدرت او عظیم است و آن را میتوان در گردبادهای وحشتناک و طوفانهای شدید مشاهده کرد. ابرها خاک زیر پای او هستند! | 3 |
Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu; ndipo sadzalola kuti munthu wolakwa asalangidwe. Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe, ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
به فرمان خداوند دریاها و رودها خشک میشوند، چراگاههای سبز و خرم باشان و کرمل از بین میروند و جنگلهای سرسبز لبنان طراوت و خرمی خود را از دست میدهند. | 4 |
Amalamulira nyanja ndipo imawuma; amawumitsa mitsinje yonse. Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
در حضور او کوهها میلرزند، تپهها گداخته میشوند، زمین متلاشی میگردد و ساکنانش نابود میشوند. | 5 |
Mapiri amagwedera pamaso pake ndipo zitunda zimasungunuka. Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake, dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
کیست که بتواند در برابر خشم خدا ایستادگی کند؟ غضب او مانند آتش فرو میریزد و کوهها در برابر خشم او خرد میشوند. | 6 |
Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa? Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa? Ukali wake ukuyaka ngati moto; matanthwe akunyeka pamaso pake.
خداوند نیکوست و در روز بلا و سختی پناهگاه میباشد. او از کسانی که به او توکل میکنند مراقبت مینماید، | 7 |
Yehova ndi wabwino, ndiye kothawirako nthawi ya masautso. Amasamalira amene amamudalira,
ولی دشمنان خود را با سیلابی شدید از بین میبرد و آنها را به ظلمت مرگ روانه میکند. | 8 |
koma ndi madzi achigumula choopsa Iye adzawononga adani ake (Ninive); adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
ای نینوا، چرا به فکر مخالفت با خداوند هستی؟ او با یک ضربه تو را از پای در خواهد آورد، به طوری که دیگر نخواهی توانست مقاومت کنی. | 9 |
Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova adzachiwononga kotheratu; msautso sudzabweranso kachiwiri.
دشمنانش را همچون خارهای به هم پیچیده و مانند کسانی که از مستی تلوتلو میخورند به داخل آتش میاندازد و آنها همچون کاه در شعلههای آتش سوخته شده دود میشوند. | 10 |
Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo; adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
این پادشاه تو کیست که جرأت میکند بر ضد خداوند توطئه کند؟ | 11 |
Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa, wofuna kuchitira Yehova chiwembu, amene amapereka uphungu woyipa.
خداوند میفرماید: «سپاه آشور هر قدر هم قوی و بزرگ باشد، محو و نابود خواهد شد. «ای قوم من، به اندازۀ کافی شما را تنبیه کردهام، اما بار دیگر تنبیهتان نخواهم کرد. | 12 |
Yehova akuti, “Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi, kaya iwowo ndi ambiri, koma adzawonongedwa ndi kutheratu. Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda, sindidzakuzunzanso.
اینک زنجیرهای شما را پاره میکنم و شما را از قید اسارت پادشاه آشور آزاد میسازم.» | 13 |
Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
خداوند به پادشاه آشور میفرماید: «نسل تو را از بین میبرم تا نام و نشانی از تو باقی نماند. بتها و بتخانههای تو را نابود خواهم کرد و قبرت را خواهم کند، زیرا تو نفرتانگیزی.» | 14 |
Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti, “Sudzakhala ndi zidzukulu zimene zidzadziwike ndi dzina lako. Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba amene ali mʼnyumba ya milungu yako. Ine ndidzakukumbira manda chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
ببینید، قاصدی از کوهها سرازیر شده، خبر خوش پیروزی را ندا میدهد. ای یهودا، عیدهای خود را برگزار نما و نذرهای خود را به خدا وفا کن، چون دشمن، دیگر هرگز برنمیگردد. او برای همیشه ریشهکن شده است! | 15 |
Taonani, pa phiripo, mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino, amene akulengeza za mtendere! Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu ndipo kwaniritsani malumbiro anu. Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo; iwo adzawonongedwa kotheratu.