< متی 26 >
چون عیسی همۀ این سخنان را به پایان رساند، به شاگردانش گفت: | 1 |
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
«همانطور که میدانید، دو روز دیگر عید پِسَح آغاز میشود. در این عید مرا دستگیر کرده، بر صلیب خواهند کشت.» | 2 |
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
در این هنگام، کاهنان اعظم و مشایخ قوم در خانهٔ قیافا، کاهن اعظم، گرد آمدند، | 3 |
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
و با یکدیگر مشورت کردند که با چه حیلهای عیسی را دستگیر کرده، بکشند؛ | 4 |
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
ولی تصمیم گرفتند این کار را به هنگام عید نکنند تا آشوبی به راه نیفتد. | 5 |
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
در آن هنگام عیسی در بیتعنیا در خانهٔ شمعون جذامی بود. | 6 |
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
سر سفره، زنی با یک شیشه عطر گرانبها وارد شد و عطر را بر سر عیسی ریخت. | 7 |
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
شاگردانش وقتی این را دیدند، اوقاتشان تلخ شد و گفتند: | 8 |
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
«حیف از این عطر که تلف شد. میشد آن را به سیصد سکۀ نقره بفروشیم و پولش را به فقرا بدهیم.» | 9 |
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
عیسی که میدانست به یکدیگر چه میگویند، گفت: «چرا این زن را آزار میدهید؟ او کار نیکویی در حق من کرده است. | 10 |
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
فقرا را همیشه با خود دارد، ولی مرا همیشه با خود نخواهید داشت. | 11 |
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
این زن در واقع با ریختن این عطر روی من، بدن مرا برای دفن آماده کرد. | 12 |
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
براستی به شما میگویم، در هر نقطهٔ جهان که انجیل موعظه شود، خدمتی نیز که این زن به من کرد، ذکر خواهد شد.» | 13 |
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
آنگاه یهودای اسخریوطی که یکی از دوازده شاگرد بود، نزد کاهنان اعظم رفت | 14 |
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
و گفت: «چقدر به من میدهید تا عیسی را به شما تسلیم کنم؟» آنان سی سکهٔ نقره به او دادند. | 15 |
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
از آن هنگام، او به دنبال فرصت مناسبی بود تا عیسی را به ایشان تسلیم کند. | 16 |
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
روز اول عید فطیر فرا رسید. شاگردان عیسی نزد او آمده، پرسیدند: «کجا میخواهی برایت تدارک ببینیم تا شام پِسَح را بخوری؟» | 17 |
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
او در جواب گفت که به شهر نزد فلان شخص رفته، بگویند: «استاد ما میگوید:”وقت من فرا رسیده است. میخواهم با شاگردانم در منزل شما شام پسَح را بخوریم.“» | 18 |
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
شاگردان طبق گفتۀ عیسی عمل کرده، شام پسَح را در آنجا تدارک دیدند. | 19 |
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
شب، عیسی با دوازده شاگرد خود بر سر سفره نشست. | 20 |
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
هنگام خوردن شام او به ایشان گفت: «براستی به شما میگویم که یکی از شما به من خیانت خواهد کرد.» | 21 |
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
همه از این سخن غمگین شدند و یکی پس از دیگری از او پرسیدند: «سرورم، من که آن شخص نیستم؟» | 22 |
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
او در پاسخ فرمود: «آن که دستش را با دست من به سوی بشقاب دراز کرد، همان کسی است که به من خیانت میکند. | 23 |
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
پسر انسان باید بمیرد، همانطور که در کتب مقدّس دربارۀ او نوشته شده است. اما وای به حال آنکه او را تسلیم دشمن میکند. برای او بهتر میبود که هرگز به دنیا نمیآمد.» | 24 |
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
یهودا نیز که بعد به او خیانت کرد، از او پرسید: «استاد، آیا آن شخص منم؟» عیسی جواب داد: «بله، خودت گفتی!» | 25 |
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
وقتی شام میخوردند، عیسی نان را برداشت و شکر نمود؛ سپس آن را تکهتکه کرد و به شاگردان داد و فرمود: «بگیرید بخورید، این بدن من است.» | 26 |
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
پس از آن، جام شراب را برداشت، شکر کرد و به ایشان داده، گفت: «هر یک از شما از این جام بنوشید. | 27 |
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
این خون من است که با آن، پیمان جدید میان خدا و قومش را مهر میکنم. خون من برای آمرزش گناهان بسیاری ریخته میشود. | 28 |
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
به شما میگویم که من دیگر از این محصول انگور نخواهم نوشید تا روزی که آن را با شما در ملکوت پدرم، تازه بنوشم.» | 29 |
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
سپس سرودی خواندند و به سوی کوه زیتون به راه افتادند. | 30 |
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
آنگاه عیسی به ایشان فرمود: «امشب همهٔ شما مرا تنها میگذارید. چون در کتب مقدّس نوشته شده که خدا چوپان را میزند و گوسفندان گله پراکنده میشوند. | 31 |
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
اما پس از زنده شدنم، به جلیل خواهم رفت و شما را در آنجا خواهم دید.» | 32 |
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
پطرس گفت: «اگر حتی همه تو را تنها بگذارند، من از کنارت دور نخواهم شد.» | 33 |
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
عیسی به او گفت: «باور کن که همین امشب، پیش از بانگ خروس، تو سه بار مرا انکار کرده، خواهی گفت که مرا نمیشناسی!» | 34 |
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
ولی پطرس گفت: «حتی اگر لازم باشد، با تو خواهم مرد، ولی هرگز تو را انکار نخواهم کرد!» بقیه شاگردان نیز چنین گفتند. | 35 |
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
پس عیسی با شاگردان خود به یک باغ زیتون رسیدند، که به باغ جتسیمانی معروف بود. او به ایشان گفت: «شما اینجا بنشینید تا من کمی دورتر رفته، دعا کنم.» | 36 |
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
سپس پطرس و دو پسر زبدی یعنی یعقوب و یوحنا را نیز با خود برد و در حالی که اندوه و اضطراب وجود او را فرا گرفته بود، | 37 |
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
به ایشان گفت: «از شدت حزن و اندوه، در آستانۀ مرگ هستم. شما همینجا بمانید و با من بیدار باشید.» | 38 |
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
سپس کمی دورتر رفت و بر زمین افتاد و چنین دعا کرد: «پدر، اگر ممکن است، این جام رنج و عذاب را از مقابل من بردار؛ اما نه به خواهش من، بلکه به خواست تو.» | 39 |
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
آنگاه نزد آن سه شاگرد برگشت و دید که در خوابند. پس به پطرس گفت: «نتوانستید حتی یک ساعت با من بیدار بمانید؟ | 40 |
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
بیدار بمانید و دعا کنید تا وسوسه بر شما غلبه نکند. روحْ تمایل دارد، اما جسم ضعیف است.» | 41 |
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
باز ایشان را گذاشت و رفت و چنین دعا کرد: «پدر، اگر ممکن نیست این جام از مقابل من برداشته شود، پس آن را مینوشم. آنچه خواست توست بشود.» | 42 |
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
وقتی بازگشت، دید که هنوز در خوابند، چون نمیتوانستند پلکهایشان را باز نگاه دارند. | 43 |
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
پس برای بار سوم رفت و همان دعا را کرد. | 44 |
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
سپس، نزد شاگردان بازگشت و گفت: «آیا هنوز در خوابید و استراحت میکنید؟ اکنون زمان مقرر فرا رسیده است و پسر انسان در چنگ بدکاران گرفتار میشود. | 45 |
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
برخیزید، باید برویم. نگاه کنید، این هم تسلیم کنندۀ من!» | 46 |
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
سخن عیسی هنوز به پایان نرسیده بود که یهودا، از راه رسید. همراه او عدهای با شمشیر و چوب و چماق نیز آمده بودند. آنان از سوی کاهنان اعظم و مشایخ قوم فرستاده شده بودند. | 47 |
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
تسلیمکنندۀ او یهودا، به همراهان خود گفته بود: «هر که را ببوسم، همان است؛ او را بگیرید.» | 48 |
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
پس یهودا مستقیم به سوی عیسی رفت و گفت: «سلام استاد!» و او را بوسید. | 49 |
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
عیسی گفت: «دوست من، کار خود را انجام بده!» پس آن عده جلو رفتند و عیسی را گرفتند. | 50 |
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
در این لحظه یکی از همراهان عیسی شمشیر خود را کشید و با یک ضربه، گوش غلام کاهن اعظم را برید. | 51 |
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
عیسی به او فرمود: «شمشیرت را غلاف کن. هر که شمشیر بکشد، با شمشیر نیز کشته خواهد شد. | 52 |
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
مگر نمیدانی که میتوانم از پدرم درخواست کنم تا هزاران فرشته به کمک من بفرستد؟ | 53 |
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
ولی اگر چنین کنم، چگونه پیشگوییهای کتب مقدّس جامۀ عمل خواهند پوشید که میفرمایند چنین وقایعی باید رخ دهند؟» | 54 |
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
آنگاه رو به آن عده کرد و گفت: «مگر من دزد فراری هستم که با چوب و چماق و شمشیر به سراغم آمدهاید؟ من هر روز در برابر چشمانتان در معبد بودم و به مردم تعلیم میدادم؛ چرا در آنجا مرا نگرفتید؟ | 55 |
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
بله، میبایست اینطور میشد، چون تمام این وقایع را انبیا در کتب مقدّس پیشگویی کردهاند.» در این گیرودار، تمام شاگردان، او را تنها گذاشته، فرار کردند. | 56 |
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
پس آن گروه، عیسی را به خانهٔ قیافا، کاهن اعظم بردند. در آنجا تمام علمای دین و مشایخ یهود جمع بودند. | 57 |
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
در ضمن، پطرس هم از دور به دنبال عیسی رفت تا وارد حیاط خانهٔ کاهن اعظم شد و کنار سربازان نشست تا ببیند بر سر عیسی چه میآید. | 58 |
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
کاهنان اعظم، و در واقع، تمام اعضای شورای عالی یهود جمع شده بودند و به دنبال شاهدانی میگشتند که به دروغ به عیسی تهمت بزنند، تا بتوانند به مرگ محکومش کنند. | 59 |
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
ولی با این که چند نفر را یافتند و آنان نیز شهادت دروغ دادند، ولی سخنان ایشان با هم یکی نبود. سرانجام دو نفر را پیدا کردند که | 60 |
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
میگفتند: «این مرد میگفت من میتوانم معبد را خراب کنم، و آن را ظرف سه روز باز بنا نمایم.» | 61 |
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
آنگاه کاهن اعظم برخاست و به عیسی گفت: «خوب، چه میگویی؟ آیا آنچه میگویند صحت دارد؟» | 62 |
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
ولی عیسی خاموش ماند. کاهن اعظم به او گفت: «به نام خدای زنده از تو میخواهم جواب بدهی. آیا تو مسیح، پسر خدا هستی یا نه؟» | 63 |
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
عیسی جواب داد: «تو خودت میگویی! و من هم به شما میگویم که از این پس پسر انسان را خواهید دید که به دست راست خدا نشسته، بر ابرهای آسمان میآید.» | 64 |
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
آنگاه کاهن اعظم یقۀ لباس خود را درید و فریاد زد: «کفر گفت! دیگر چه نیاز به شاهد داریم؟ خودتان شنیدید که کفر گفت. | 65 |
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
چه رأی میدهید؟» همه فریاد زدند: «باید بمیرد!» | 66 |
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
آنگاه به صورتش آب دهان انداخته، او را زدند. بعضی نیز به او سیلی زده، | 67 |
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
با ریشخند میگفتند: «ای مسیح، نبوّت کن! بگو ببینیم چه کسی تو را زد؟» | 68 |
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
اما پطرس هنوز بیرون خانه، در حیاط نشسته بود که یکی از کنیزان کاهن اعظم نزد او آمد و گفت: «به گمانم تو نیز با عیسای جلیلی بودی!» | 69 |
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
ولی پطرس در حضور همه منکر شد و گفت: «نمیدانم چه میگویی!» | 70 |
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
اندکی بعد، در کنار در، کنیز دیگری به او برخورد و به آنانی که در آنجا بودند گفت: «این مرد نیز با عیسای ناصری بود.» | 71 |
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
پطرس دوباره انکار کرد، و حتی این بار قسم خورده، گفت: «من اصلاً این مرد را نمیشناسم.» | 72 |
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
ولی کمی بعد، کسانی که آنجا ایستاده بودند پیش پطرس آمده، به او گفتند: «تو حتماً یکی از شاگردان او هستی، چون لهجهات جلیلی است!» | 73 |
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
پطرس این بار به لعنت کردن و قسم خوردن شروع کرد و گفت: «من اصلاً این مرد را نمیشناسم.» درست در همین هنگام خروس بانگ زد، | 74 |
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
و پطرس گفتهٔ عیسی را به یاد آورد که گفته بود: «پیش از بانگ خروس، تو سه بار مرا انکار خواهی کرد.» پس بیرون رفت و به تلخی گریست. | 75 |
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.