< ملاکی 4 >

خداوند لشکرهای آسمان می‌فرماید: «روز داوری مثل تنوری شعله‌ور فرا می‌رسد و همهٔ اشخاص مغرور و بدکار را مانند کاه می‌سوزاند. آنها مانند درخت تا ریشه خواهند سوخت و خاکستر خواهند شد. 1
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi.
«اما برای شما که ترس مرا در دل دارید، آفتاب عدالت با پرتو شفابخش خود طلوع خواهد کرد، و شما شاد و سبکبال مثل گوساله‌هایی که به چراگاه می‌روند، جست و خیز خواهید نمود. 2
Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola.
و خداوند لشکرهای آسمان می‌گوید: در آن روزی که من تعیین کرده‌ام، بدکاران را مثل خاکستر زیر پای خود له خواهید کرد. 3
Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
«دستورها و قوانینی را که بر کوه سینا توسط خدمتگزار خود موسی به همهٔ قوم اسرائیل دادم به یاد داشته باشید و از آنها اطاعت کنید. 4
Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.
«پیش از فرا رسیدن روز بزرگ و هولناک داوری خداوند، من ایلیای نبی را برای شما می‌فرستم. 5
“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
او دل پدران را به سوی فرزندان، و دل فرزندان را به سوی پدران متمایل خواهد ساخت، و این باعث خواهد شد که من سرزمین شما را ویران نکنم.» 6
Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”

< ملاکی 4 >