< لاویان 9 >
در روز هشتم، موسی هارون و پسرانش را با مشایخ اسرائیل جمع کرد | 1 |
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli.
و به هارون گفت: «یک گوسالهٔ نر سالم و بیعیب برای قربانی گناه و یک قوچ سالم و بیعیب برای قربانی سوختنی بگیر و آنها را به حضور خداوند تقدیم کن. | 2 |
Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova.
بعد به قوم اسرائیل بگو که یک بزغالهٔ نر برای قربانی گناه خود و یک گوساله و یک بره که هر دو یک ساله و بیعیب باشند برای قربانی سوختنی بیاورند. | 3 |
Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza.
همچنین قوم اسرائیل باید یک گاو و یک قوچ برای قربانی سلامتی، و آرد مخلوط با روغن زیتون برای هدیهٔ آردی به خداوند تقدیم کنند زیرا امروز خداوند بر ایشان ظاهر خواهد شد.» | 4 |
Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’”
پس قوم آنچه را که موسی امر فرموده بود، جلوی خیمۀ ملاقات آوردند و تمام جماعت نزدیک شده، در حضور خداوند ایستادند. | 5 |
Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova.
موسی به ایشان گفت: «خداوند فرموده دستورهای او را انجام دهید تا حضور پرجلال خود را بر شما ظاهر کند.» | 6 |
Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”
آنگاه موسی به هارون گفت: «نزدیک مذبح بیا و همانطور که خداوند فرموده است قربانی گناه و قربانی سوختنی خود را تقدیم کرده، برای خود کفاره کن و سپس قربانیهای قوم را تقدیم نموده، برای آنها کفاره نما.» | 7 |
Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”
بنابراین هارون به مذبح نزدیک شد و گوسالهٔ قربانی گناه خود را ذبح کرد. | 8 |
Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo.
پسرانش خون گوساله را پیش وی آوردند و او انگشت خود را در خون فرو برد و بر شاخهای مذبح مالید و باقیماندهٔ خون را به پای مذبح ریخت. | 9 |
Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo.
بعد همانطور که خداوند به موسی دستور داده بود، چربی، قلوهها و سفیدی روی جگر قربانی گناه را بر مذبح، | 10 |
Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
و گوشت و پوست آن را بیرون از اردوگاه سوزانید. | 11 |
Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.
پس از آن هارون قربانی سوختنی را ذبح کرد و پسرانش خون قربانی را آوردند و هارون آن را بر چهار طرف مذبح پاشید. | 12 |
Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa.
ایشان کله و قطعههای دیگر حیوان را نزد هارون آوردند و او آنها را بر مذبح سوزانید. | 13 |
Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa.
دل و روده و پاچهها را شست و اینها را نیز به عنوان قربانی سوختنی بر مذبح سوزانید. | 14 |
Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.
سپس هارون قربانی قوم اسرائیل را تقدیم کرد. او بز قربانی گناه قوم را ذبح نموده، آن را مانند قربانی گناه خود برای گناه قوم تقدیم کرد. | 15 |
Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.
آنگاه مطابق قوانین، قربانی سوختنی ایشان را به خداوند تقدیم نمود. | 16 |
Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake.
بعد هدیهٔ آردی را آورد و مشتی از آن را گرفت و بر مذبح سوزانید. (این قربانی غیر از قربانی سوختنیای بود که هر روز صبح تقدیم میشد.) | 17 |
Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.
پس از آن هارون گاو و قوچ را به عنوان قربانی سلامتی قوم ذبح کرد. پسران هارون خون قربانی را نزد او آوردند و او آن را بر چهار طرف مذبح پاشید. | 18 |
Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa.
سپس چربی گاو و قوچ را که شامل چربی داخل شکم و قلوهها و سفیدی روی جگر گاو و قوچ میشد، گرفت | 19 |
Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi.
و آنها را روی سینههای حیوان گذاشته، نزدیک مذبح آورد و تمام چربی را روی مذبح سوزانید. | 20 |
Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe.
همانطور که موسی دستور داده بود، هارون سینهها، و رانهای راست حیوان را به عنوان هدیهٔ مخصوص در حضور خداوند تکان داد. | 21 |
Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.
پس از تقدیم قربانیها، هارون دستهای خود را به طرف قوم اسرائیل دراز کرده، ایشان را برکت داد و از مذبح به زیر آمد. | 22 |
Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.
موسی و هارون به خیمۀ ملاقات رفتند. وقتی از آنجا بیرون آمدند قوم اسرائیل را برکت دادند. آنگاه حضور پرجلال خداوند بر تمام جماعت ظاهر شد | 23 |
Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
و از حضور خداوند آتش فرود آمده، قربانی سوختنی و چربی روی مذبح را بلعید. بنیاسرائیل وقتی این را دیدند، فریاد برآورده، در حضور خداوند به خاک افتادند. | 24 |
Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.