< لاویان 23 >

خداوند به موسی فرمود: 1
Yehova anawuza Mose kuti,
«این دستورها را به بنی‌اسرائیل بده. برای برگزاری این اعیاد، تمام قوم باید برای عبادت خداوند جمع شوند. 2
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
(در روز شَبّات نیز که هفتمین روز هفته می‌باشد، قوم باید برای عبادت خداوند جمع شوند. در هر جا که ساکن باشند باید در این روز دست از کار کشیده، استراحت کنند.) 3
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
«اعیاد خداوند، یعنی محفلهای مقدّس که باید هر سال جشن گرفته شوند از این قرارند: 4
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
«در غروب روز چهاردهم اولین ماه هر سال مراسم عید پِسَح را به احترام خداوند بجا آورید. 5
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
از روز پانزدهم همان ماه، عید فطیر برای خداوند آغاز می‌شود و تا هفت روز باید فقط نان بدون خمیرمایه خورده شود. 6
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
در روز اول این عید برای عبادت جمع شوید و از همهٔ کارهای معمول خود دست بکشید. 7
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
هفت روز هدایای سوختنی به خداوند تقدیم نمایید و در روز هفتم نیز از کارهای معمول خود دست کشیده برای عبادت جمع شوید.» 8
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
خداوند به موسی فرمود: 9
Yehova anawuza Mose kuti,
«این دستورها را به بنی‌اسرائیل بده: وقتی به سرزمینی که من به شما می‌دهم داخل شدید و اولین محصول خود را درو کردید، بافه‌ای از نوبر محصول خود را نزد کاهن بیاورید. 10
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
فردای روز شبّات، کاهن بافه را در حضور خداوند تکان دهد تا خداوند شما را بپذیرد. 11
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
همان روز یک برهٔ یک سالهٔ سالم و بی‌عیب به عنوان قربانی سوختنی به خداوند تقدیم کنید. 12
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
برای هدیهٔ آردی آن، دو کیلو آرد مرغوب مخلوط با روغن زیتون آورده، بر آتش به خداوند تقدیم کنید. این هدیه، هدیه‌ای مخصوص و خوشبو برای خداوند خواهد بود. یک لیتر شراب هم به عنوان هدیهٔ نوشیدنی تقدیم نمایید. 13
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
تا این هدایا را به خدایتان تقدیم نکرده‌اید، نباید نان یا حبوبات تازه یا برشته بخورید. این قانونی است همیشگی برای تمام نسلهای شما در هر جایی که زندگی کنید. 14
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
«هفت هفته بعد از روزی که اولین بافهٔ خود را به من تقدیم کردید، 15
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
یعنی در روز پنجاهم که روز بعد از هفتمین شَبّات است هدیهٔ دیگری از محصول تازهٔ خود به حضور خداوند بیاورید. 16
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
هر خانواده‌ای دو قرص نان که از دو کیلو آرد مرغوب همراه با خمیرمایه پخته شده باشد، بیاورد تا در حضور خداوند تکان داده شود و به عنوان هدیه‌ای از آخرین برداشت محصول به من تقدیم شود. 17
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
همراه با این نانها، هفت برهٔ یک سالهٔ بی‌عیب، یک گوساله و دو قوچ به عنوان قربانی سوختنی با هدایای آردی و نوشیدنی آنها به خداوند تقدیم کنید. این هدایا، هدایای مخصوص و خوشبو برای خداوند خواهند بود. 18
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
همچنین یک بز نر به عنوان قربانی گناه و دو برهٔ نر یک ساله به عنوان قربانی سلامتی ذبح کنید. 19
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
«کاهن، این دو برهٔ ذبح شده را با نانهای پخته شده از آخرین برداشت محصول شما به عنوان هدیهٔ مخصوص در حضور خداوند تکان دهد. این هدایا برای خداوند مقدّسند و باید برای خوراک به کاهنان داده شوند. 20
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
در آن روز اعلان شود که مردم از کارهای معمول خود دست کشیده، برای عبادت جمع شوند. این قانونی است همیشگی برای نسلهای شما در هر جا که باشید. 21
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
«وقتی که محصولات خود را درو می‌کنید، گوشه‌های مزرعهٔ خود را تماماً درو نکنید و خوشه‌های بر زمین افتاده را جمع نکنید. آنها را برای فقرا و غریبانی که در میان شما ساکنند، بگذارید. من یهوه، خدای شما هستم.» 22
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
خداوند به موسی فرمود: 23
Yehova anawuza Mose kuti,
«این دستورها را به بنی‌اسرائیل بده: روز اول ماه هفتم هر سال، روز استراحت است و همهٔ قوم اسرائیل باید با شنیدن صدای شیپورها، برای عبادت جمع شوند. 24
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
در آن روز هدیه‌ای بر آتش به خداوند تقدیم کنید و هیچ کار دیگری انجام ندهید.» 25
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
خداوند به موسی فرمود: 26
Yehova anawuza Mose kuti,
«روز دهم ماه هفتم هر سال، روز کفاره است. در آن روز تمام قوم باید برای عبادت جمع شوند و روزه بگیرند و هدیه‌ای بر آتش به خداوند تقدیم کنند. 27
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
در روز کفاره کار نکنید، زیرا روزی است که باید برای گناهان خود از یهوه خدایتان طلب آمرزش نمایید. 28
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
هر شخصی که آن روز را در روزه به سر نبرد، از میان قوم خود منقطع خواهد شد. 29
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
من هر کسی را که در آن روز دست به هرگونه کاری بزند، از میان شما هلاک خواهم ساخت. 30
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
از غروب روز نهم ماه هفتم تا غروب روز بعد، روز مخصوص کفاره است و باید در آن روز روزه بگیرید و استراحت کنید.» 32
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
خداوند به موسی فرمود: 33
Yehova anawuza Mose kuti,
«این دستورها را به بنی‌اسرائیل بده. روز پانزدهم ماه هفتم، عید سایبانها آغاز می‌شود و باید تا مدت هفت روز در حضور خداوند جشن گرفته شود. 34
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
در روز اول تمامی قوم اسرائیل را برای عبادت جمع کنید و از کارهای معمول خود دست بکشید. 35
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
در هر هفت روز عید، هدیه‌ای بر آتش به خداوند تقدیم نمایید. در روز هشتم دوباره تمامی قوم را برای عبادت جمع کنید و هدیه‌ای بر آتش به خداوند تقدیم نمایید. این روز، آخرین روز عید است و نباید هیچ کاری انجام دهید. 36
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
«(این است اعیاد مقدّسی که در آنها باید تمامی قوم برای عبادت جمع شده، قربانیهای سوختنی، هدایای آردی، هدایای نوشیدنی و سایر قربانیها را بر آتش به خداوند تقدیم کنند. 37
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
این اعیاد مقدّس غیر از روزهای مخصوص شَبّات است. هدایایی که در این اعیاد تقدیم می‌کنید غیر از هدایای روزانه، نذری و داوطلبانه‌ای است که به خداوند تقدیم می‌کنید.) 38
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
«از روز پانزدهم ماه هفتم که پایان برداشت محصول است، این عید هفت روزه را در حضور خداوند جشن بگیرید. به یاد داشته باشید که روزهای اول و آخر این عید، روزهای استراحت می‌باشند. 39
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
در روز اول، از درختان خود میوه‌های خوب بچینید و شاخه‌های نخل و شاخه‌های درختان پربرگ و شاخه‌های بید را گرفته با آنها سایبان درست کنید و هفت روز در حضور یهوه خدایتان شادی کنید. 40
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
برگزاری این عید هفت روزه در ماه هفتم برای خداوند، فریضه‌ای ابدی است که باید نسل اندر نسل انجام گیرد. 41
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
در طول آن هفت روز همهٔ شما اسرائیلی‌ها باید در سایبانها به سر برید. 42
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
هدف از این عید آن است که نسلهای شما بدانند هنگامی که من بنی‌اسرائیل را از مصر بیرون آوردم، آنها را در زیر سایبانها سکونت دادم. من خداوند، خدای شما هستم.» 43
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
بدین ترتیب موسی قوانین اعیاد خداوند را به اطلاع قوم اسرائیل رسانید. 44
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.

< لاویان 23 >