< لاویان 18 >
سپس خداوند به موسی فرمود: | 1 |
Yehova anawuza Mose kuti,
«این دستورها را به بنیاسرائیل بده: من یهوه خدای شما هستم. | 2 |
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
پس مانند بتپرستان رفتار نکنید یعنی مانند مصریهایی که در کشورشان زندگی میکردید و یا مانند کنعانیهایی که میخواهم شما را به سرزمینشان ببرم. | 3 |
Musamachite zomwe amachita anthu a ku Igupto kumene munkakhala kuja, ndiponso musamachite zomwe amachita anthu a ku Kanaani kumene ndikukupititsani. Musatsatire miyambo yawo.
شما باید از دستورهای من پیروی کنید و قوانین مرا نگاه دارید و آنها را بجا آورید، چون من یهوه، خدای شما هستم. | 4 |
Inu muzimvera malamulo anga ndipo muzisamalitsa kutsatira malangizo anga. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
پس دستورها و قوانین مرا نگاه دارید، زیرا از طریق اطاعت از احکام شریعت است که شخص از حیات برخوردار میشود. من یهوه هستم. | 5 |
Choncho sungani malangizo ndi malamulo anga, popeza munthu amene amvera zimenezi adzakhala ndi moyo. Ine ndine Yehova.
«هیچکس از شما نباید با محارمِ خود همبستر شود. من یهوه هستم. | 6 |
“‘Munthu aliyense asagonane ndi wachibale wake. Ine ndine Yehova.
با مادر خود همبستر نشو، زیرا با این کار به او و به پدرت بیاحترامی میکنی. | 7 |
“‘Usachititse manyazi abambo ako pogonana ndi amayi ako. Iwo ndi amayi ako. Usagonane nawo.
با هیچکدام از زنان پدرت همبستر نشو، چون با این کار به پدرت بیاحترامی میکنی. | 8 |
“‘Usagonane ndi mkazi wa abambo ako (osakhala amayi okubala). Ukatero ukuchititsa manyazi abambo ako.
همچنین با خواهر تنی یا با خواهر ناتنی خود، چه دختر پدرت باشد چه دختر مادرت، چه در همان خانه به دنیا آمده باشد چه در جای دیگر، همبستر نشو. | 9 |
“‘Usagonane ndi mlongo wako, mwana wamkazi wa abambo ako, kapena mwana wamkazi wa amayi ako, kaya anabadwira mʼnyumba mwanu kapena kwina.
«با دختر پسرت یا دختر دخترت همبستر نشو، چون با این کار خود را رسوا میکنی. | 10 |
“‘Usagonane ndi mdzukulu wako: mwana wa mwana wako wamwamuna kapena mwana wa mwana wako wamkazi. Kutero nʼkudzichotsa ulemu.
با دختر زن پدرت همبستر نشو، چون او خواهر ناتنی توست. | 11 |
“‘Usagonane ndi mwana wamkazi wa mkazi wa abambo ako, amene abambo akowo anabereka; popeza ameneyo ndi mlongo wako.
با عمهٔ خود همبستر نشو، چون از بستگان نزدیک پدرت میباشد. | 12 |
“‘Usagonane ndi mlongo wa abambo ako; popeza ameneyo ndi thupi limodzi ndi abambo ako.
با خالهٔ خود همبستر نشو، چون از بستگان نزدیک مادرت است. | 13 |
“‘Usagonane ndi mchemwali wa amayi ako chifukwa ameneyo ndi thupi limodzi ndi amayi ako.
با زن عموی خود همبستر نشو، چون او مثل عمهٔ توست. | 14 |
“‘Usachititse manyazi mchimwene wa abambo ako pogonana ndi mkazi wake popeza amenewo ndi azakhali ako.
«با عروس خود همبستر نشو، چون زن پسر توست. | 15 |
“‘Usagonane ndi mpongozi wako popeza ameneyo ndi mkazi wa mwana wako. Choncho usamuchititse manyazi.
با زن برادرت همبستر نشو، چون با این کار به برادرت بیاحترامی میکنی. | 16 |
“‘Usagonane ndi mkazi wa mchimwene wako popeza potero ukuchititsa manyazi mʼbale wakoyo.
با یک زن و دختر او یا نوهاش همبستر نشو، چون آنها بستگان نزدیک همدیگرند و این عمل قبیحی است. | 17 |
“‘Usagonane ndi mkazi ndiponso mwana wake wamkazi. Usagonane ndi mwana wamkazi wa mwana wake wamwamuna, kapena mwana wamkazi wa mwana wake wamkazi. Amenewo ndi thupi limodzi ndi mkaziyo. Kutero ndikuchita chinthu choyipa kwambiri.
مادامی که زنت زنده است نباید خواهر او را هم به زنی بگیری و با او همبستر شوی. | 18 |
“‘Usakwatire mchemwali wa mkazi wako ndi kumagonana naye mkazi wakoyo ali moyo ngati wopikisana naye.
«با زنی به هنگام عادت ماهانهاش همبستر نشو. | 19 |
“‘Usamuyandikire mkazi kuti ugonane naye pa nthawi yake yosamba.
با زنی که همسر مرد دیگری است همبستر نشو و خود را با او نجس نساز. | 20 |
“‘Usagonane ndi mkazi wa mnzako ndi kudziyipitsa naye.
«هیچکدام از فرزندان خود را به بت مولک هدیه نکن و آنها را بر مذبح آن نسوزان زیرا با این کار نام خداوند، خدای خود را بیحرمت خواهی کرد. | 21 |
“‘Usapereke mwana wako aliyense kuti akhale nsembe yamoto kwa Moleki ndi kuyipitsa dzina la Yehova. Ine ndine Yehova.
«هیچ مردی نباید با مرد دیگری نزدیکی کند، چون این عمل، بسیار قبیح است. | 22 |
“‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa.
هیچ مرد یا زنی نباید با هیچ حیوانی نزدیکی کند و با این کار خود را نجس سازد. این عمل، بسیار قبیح است. | 23 |
“‘Usagonane ndi nyama ndi kudziyipitsa nayo. Mkazi asadzipereke kwa nyama kuti agonane nayo. Chimenecho ndi chisokonezo.
«با این کارها خود را نجس نسازید، چون این اعمالی است که بتپرستها انجام میدهند و به خاطر این کارهاست که میخواهم آنان را از سرزمینی که شما داخل آن میشوید بیرون کنم. | 24 |
“‘Musadzidetse ndi zinthu zimenezi chifukwa umo ndi mmene mitundu ina imene ndikuyithamangitsa pamaso panu inadzidetsera.
تمامی آن سرزمین با این نوع اعمال، نجس شده است. به همین دلیل است که مردمانی را که در آنجا ساکنند مجازات میکنم، و سرزمینشان آنها را قی میکند. | 25 |
Choncho dziko linayipa ndipo ndinalilanga chifukwa cha tchimo lake. Motero dzikolo linasanza anthu ake okhalamo.
شما باید از تمام قوانین و دستورهای من اطاعت کنید و هیچکدام از این اعمال قبیح را انجام ندهید. این قوانین هم شامل شما میشود و هم شامل غریبانی که در میان شما ساکنند. | 26 |
Koma inu mukasunge malangizo ndi malamulo anga. Mbadwa ndiponso alendo amene akukhala pakati panu asakachite china chilichonse cha zinthu zonyansazi,
«آری، تمامی این اعمال قبیح بهوسیلۀ مردمان سرزمینی که میخواهم شما را به آنجا ببرم به عمل آمده و آن سرزمین را نجس کرده است. | 27 |
pakuti zinthu zonsezi ndi zomwe ankachita anthu amene ankakhala mʼdzikomo inu musanafike, ndipo dziko linayipitsidwa.
شما این اعمال را انجام ندهید و گرنه شما را نیز مثل اقوامی که اکنون در آنجا ساکنند از آن سرزمین بیرون خواهم راند. | 28 |
Koma inu musachite zimenezi kuti dziko lingakusanzeni mutaliyipitsa monga linasanzira mitundu imene imakhalamo inu musanafike.
هر کس مرتکب یکی از این اعمال قبیح گردد، از میان قوم منقطع خواهد شد. | 29 |
“‘Aliyense wochita zinthu zonyansa zimenezi achotsedwe pakati pa anthu anzake.
پس احکام مرا اطاعت کنید و هیچیک از این عادات زشت را انجام ندهید. خود را با این اعمال قبیح نجس نکنید زیرا من یهوه، خدای شما هستم.» | 30 |
Choncho mverani malangizo anga oletsa kuchita miyambo yonyansayi imene ankatsatira anthu amene analipo inu musanafike ndi kudziyipitsa nayo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”