< داوران 16 >

روزی سامسون به شهر فلسطینی غزه رفت و شب را با زن بدکاره‌ای به سر برد. 1
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
به‌زودی در همه جا پخش شد که سامسون به غزه آمده است. پس مردان شهر تمام شب نزد دروازه در کمین نشستند تا اگر خواست فرار کند او را بگیرند. آنها در شب هیچ اقدامی نکردند بلکه گفتند: «چون صبح هوا روشن شود، او را خواهیم کشت.» 2
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
اما سامسون تا نصف شب خوابید؛ سپس برخاسته بیرون رفت و دروازهٔ شهر را با چارچوبش از جا کند و آن را بر دوش خود گذاشته، به بالای تپه‌ای که در مقابل حبرون است برد. 3
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
مدتی بعد، سامسون عاشق زنی از وادی سورق، به نام دلیله شد. 4
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
پنج رهبر فلسطینی نزد دلیله آمده، به او گفتند: «سعی کن بفهمی چه چیزی او را اینچنین نیرومند ساخته است و چطور می‌توانیم او را بگیریم و ببندیم. اگر این کار را انجام دهی هر یک از ما هزار و صد مثقال نقره به تو پاداش خواهیم داد.» 5
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
پس دلیله به سامسون گفت: «خواهش می‌کنم به من بگو که رمز قدرت تو چیست؟ چگونه می‌توان تو را بست و ناتوان کرد؟» 6
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
سامسون در جواب او گفت: «اگر مرا با هفت زه کمانِ تازه که خشک نشده باشد ببندند، مثل هر کس دیگر ناتوان خواهم شد.» 7
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
پس رهبران فلسطینی هفت زه کمان برای دلیله آوردند و دلیله با آن هفت زه کمان او را بست. 8
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
در ضمن، او چند نفر فلسطینی را در اتاق مجاور مخفی کرده بود. دلیله پس از بستن سامسون فریاد زد: «سامسون! فلسطینی‌ها برای گرفتن تو آمده‌اند!» سامسون زه را مثل نخ کتانی که به آتش برخورد می‌کند، پاره کرد و راز قدرتش آشکار نشد. 9
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
سپس دلیله به وی گفت: «سامسون، تو مرا مسخره کرده‌ای! چرا به من دروغ گفتی؟ خواهش می‌کنم به من بگو که چطور می‌توان تو را بست؟» 10
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
سامسون گفت: «اگر با طنابهای تازه‌ای که هرگز از آنها استفاده نشده، بسته شوم، مانند سایر مردان، ناتوان خواهم شد.» 11
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
پس دلیله طنابهای تازه‌ای گرفته، او را بست. این بار نیز فلسطینی‌ها در اتاق مجاور مخفی شده بودند. دلیله فریاد زد: «سامسون! فلسطینی‌ها برای گرفتن تو آمده‌اند!» ولی او طنابها را مثل نخ از بازوان خود گسست. 12
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
دلیله به وی گفت: «باز هم مرا دست انداختی و به من راست نگفتی! حالا به من بگو که واقعاً چطور می‌توان تو را بست؟» سامسون گفت: «اگر هفت گیسوی مرا در تارهای دستگاه نساجی‌ات ببافی مانند مردان دیگر، ناتوان خواهم شد.» 13
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
پس وقتی او در خواب بود، دلیله موهای او را در تارهای دستگاه نساجی بافت و آنها را با میخ دستگاه محکم کرد. سپس فریاد زد: «سامسون! فلسطینی‌ها آمدند!» او بیدار شد و با یک حرکت سر، دستگاه را از جا کند! 14
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
دلیله به او گفت: «چگونه می‌گویی مرا دوست داری و حال آنکه به من اعتماد نداری؟ سه مرتبه است که مرا دست انداختی و به من نمی‌گویی راز قدرتت در چیست؟» 15
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
دلیله هر روز با اصرارهای خود سامسون را به ستوه می‌آورد، تا اینکه سرانجام راز قدرت خود را برای او فاش ساخت. سامسون به وی گفت: «موی سر من هرگز تراشیده نشده است. چون من از بدو تولد نذیره بوده و وقف خدا شده‌ام. اگر موی سرم تراشیده شود، نیروی من از بین رفته، مانند هر شخص دیگری ناتوان خواهم شد.» 16
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
دلیله فهمید که این بار حقیقت را گفته است. پس به دنبال آن پنج رهبر فلسطینی فرستاد و به آنها گفت: «بیایید، این دفعه او همه چیز را به من گفته است.» پس آنها پولی را که به وی وعده داده بودند، با خود برداشته، آمدند. 18
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
دلیله سر سامسون را روی دامن خود گذاشت و او را خواباند. سپس به دستور دلیله موی سرش را تراشیدند. بدین ترتیب، دلیله سامسون را درمانده کرد و نیروی او از او رفت. 19
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
آنگاه دلیله فریاد زد: «سامسون! فلسطینی‌ها آمده‌اند تو را بگیرند!» او بیدار شد و با خود اینطور فکر کرد: «مانند دفعات پیش به خود تکانی می‌دهم و آزاد می‌شوم!» اما غافل از این بود که خداوند او را ترک کرده است. 20
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
در این موقع فلسطینی‌ها آمده، او را گرفتند و چشمانش را از کاسه درآورده، او را به غزه بردند. در آنجا سامسون را با زنجیرهای مفرغین بسته به زندان انداختند و وادارش کردند گندم دستاس کند. 21
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
اما طولی نکشید که موی سرش دوباره بلند شد. 22
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
رهبران فلسطینی جمع شدند تا جشن مفصلی بر پا نمایند و قربانی بزرگی به بت خود داجون تقدیم کنند، چون پیروزی بر دشمن خود، سامسون را مدیون بت خود می‌دانستند. آنها با دیدن سامسون خدای خود را ستایش می‌کردند و می‌گفتند: «خدای ما، دشمن ما را که زمینمان را خراب کرد و بسیاری از فلسطینی‌ها را کشت، اکنون به دست ما تسلیم کرده است.» 23
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
جماعت نیمه مست فریاد می‌زدند: «سامسون را از زندان بیاورید تا ما را سرگرم کند.» سامسون را از زندان به داخل معبد آورده، او را در میان دو ستون که سقف معبد بر آنها قرار گرفته بود بر پا داشتند. سامسون به پسری که دستش را گرفته، او را راهنمایی می‌کرد گفت: «دستهای مرا روی دو ستون بگذار، چون می‌خواهم به آنها تکیه کنم.» 25
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
در این موقع معبد از مردم پر شده بود. پنج رهبر فلسطینی همراه با سه هزار نفر در ایوان‌های معبد به تماشای سامسون نشسته، او را مسخره می‌کردند. 27
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
سامسون نزد خداوند دعا کرده، چنین گفت: «ای خداوند، خدای من، التماس می‌کنم مرا به یاد آور و یک بار دیگر نیرویم را به من بازگردان، تا انتقام چشمانم را از این فلسطینی‌ها بگیرم.» 28
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
آنگاه سامسون دستهای خود را بر ستونها گذاشت و گفت: «بگذار با فلسطینی‌ها بمیرم.» سپس با تمام قوت بر ستونها فشار آورد و سقف معبد بر سر رهبران فلسطینی و همهٔ مردمی که در آنجا بودند فرو ریخت. تعداد افرادی که او هنگام مرگش کشت بیش از تمام کسانی بود که او در طول عمرش کشته بود. 29
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
بعد برادران و سایر بستگانش آمده، جسد او را بردند و در کنار قبر پدرش مانوح که بین راه صرعه و اِشتائُل قرار داشت، دفن کردند. سامسون مدت بیست سال رهبر قوم اسرائیل بود. 31
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< داوران 16 >