< داوران 10 >

پس از مرگ ابیملک، «تولع» (پسر فواه و نوهٔ دودا) برای رهایی اسرائیل به پا خاست. او از قبیلهٔ یساکار بود، ولی در شهر شامیر واقع در کوهستان افرایم سکونت داشت. 1
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
وی مدت بیست و سه سال رهبری اسرائیل را به عهده داشت. وقتی مرد، او را در شامیر دفن کردند 2
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
و «یائیر» جانشین وی شد. یائیر از اهالی جلعاد بود و بیست و دو سال رهبر اسرائیل بود. 3
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
او سی پسر داشت که دسته جمعی بر سی الاغ سوار می‌شدند. آنها در سرزمین جلعاد سی شهر داشتند که هنوز آنها را «شهرهای یائیر» می‌نامند. 4
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
وقتی یائیر مرد، او را در قامون دفن کردند. 5
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
آنگاه مردم اسرائیل بار دیگر از خداوند روگردان شده، به پرستش بعل و عشتاروت و خدایان سوریه، صیدون، موآب، عمون و فلسطین پرداختند و خداوند را ترک گفته، دیگر او را پرستش نکردند. 6
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
پس خشم خداوند بر اسرائیل افروخته شد و او فلسطینی‌ها و عمونی‌ها را بر اسرائیل مسلط ساخت. آنها بر اسرائیلی‌هایی که در سمت شرقی رود اردن در سرزمین اموری‌ها (یعنی در جلعاد) بودند، ظلم می‌کردند. همچنین عمونی‌ها از رود اردن گذشته، به قبایل یهودا، بنیامین و افرایم هجوم می‌بردند. اسرائیل مدت هجده سال زیر ظلم و ستم قرار داشت. 7
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
سرانجام بنی‌اسرائیل به سوی خداوند بازگشت نموده، التماس کردند که ایشان را نجات بخشد. آنها اعتراف نموده، گفتند: «خداوندا نسبت به تو گناه ورزیده‌ایم، زیرا تو را ترک نموده، بتهای بعل را پرستش کرده‌ایم.» 10
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
ولی خداوند به ایشان فرمود: «مگر من شما را از دست مصری‌ها، اموری‌ها، عمونی‌ها، فلسطینی‌ها، 11
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
صیدونی‌ها، عمالیقی‌ها، و معونی‌ها نرهانیدم؟ مگر به هنگام تمام سختیها به داد شما نرسیدم؟ 12
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
با وجود این، شما مرا ترک نموده، به پرستش خدایان دیگر پرداختید. پس من دیگر شما را رهایی نخواهم بخشید. 13
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
بروید و از خدایانی که برای خود انتخاب کرده‌اید کمک بطلبید! بگذارید در این هنگام سختی، آنها شما را برهانند!» 14
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
اما ایشان به خداوند گفتند: «ما گناه کرده‌ایم. هر چه صلاح می‌دانی با ما بکن، ولی فقط یکبار دیگر ما را از دست دشمنانمان نجات بده.» 15
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
آنگاه خدایان بیگانهٔ خود را ترک گفته، تنها خداوند را عبادت نمودند و خداوند به سبب سختیهای اسرائیل اندوهگین شد. 16
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
در آن موقع سپاهیان عمونی در جلعاد اردو زده، آماده می‌شدند که به اردوی اسرائیلی‌ها در مصفه حمله کنند. 17
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
رهبران اسرائیلی از یکدیگر می‌پرسیدند: «کیست که فرماندهی نیروهای ما را به عهده بگیرد و با عمونی‌ها بجنگد؟ هر کس که داوطلب شود رهبر مردم جلعاد خواهد شد!» 18
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

< داوران 10 >