< یوشع 21 >

بزرگان قبیلهٔ لاوی به شیلوه آمدند و به العازار کاهن، یوشع و بقیهٔ رهبران قبایل گفتند: «خداوند به موسی فرمود که شهرهایی برای سکونت و چراگاههایی برای گله‌ها به قبیلهٔ ما داده شود.» 1
Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli,
2
ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.”
پس بنی‌اسرائیل طبق فرمان خداوند از ملک خود شهرهایی را با چراگاههای اطرافشان به قبیلهٔ لاوی دادند. 3
Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:
خاندان قهات نخستین گروه از قبیلهٔ لاوی بودند که قرعه به نامشان درآمد. به آن دسته از قهاتی‌ها که از نسل هارون و کاهن بودند، سیزده شهر از شهرهای قبایل یهودا، شمعون و بنیامین داده شد. 4
Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini.
به بقیهٔ خاندان قهات، ده شهر از شهرهای افرایم، دان و نصف قبیلهٔ منسی داده شد. 5
Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.
به خاندان جرشون، سیزده شهر از شهرهای قبایل یساکار، اشیر، نفتالی و نصف قبیلهٔ منسی که در باشان قرار داشت، داده شد. 6
Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.
به خاندان مراری، دوازده شهر از شهرهای قبایل رئوبین، جاد و زبولون داده شد. 7
Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.
بدین ترتیب آنچه که خداوند به موسی فرموده بود، انجام پذیرفت و شهرها و چراگاهها برای قبیلهٔ لاوی به حکم قرعه تعیین گردید. 8
Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.
این است اسامی شهرهایی که از ملک قبایل یهودا و شمعون به نسل هارون که از طایفهٔ قهات (پسر لاوی) بودند، داده شد (طایفهٔ قهات نخستین گروهی بودند که قرعه به نامشان درآمد): 9
Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni,
10
ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.
شهر حبرون که همان قریهٔ اربع باشد (اربع پدر عناق بود) در کوهستان یهودا با چراگاههای اطرافش به ایشان تعلق گرفت. 11
Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira.
(مزارع و روستاهای اطراف آن، قبلاً به کالیب پسر یفنه داده شده بود.) 12
Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.
علاوه بر شهر حبرون که از شهرهای پناهگاه بود، این شهرها نیز به نسل هارون که کاهن بودند داده شد: لبنه، 13
Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina,
یتیر، اشتموع، 14
Yatiri, Esitemowa,
حولون، دبیر، 15
Holoni, Debri,
عین، یوطه و بیت‌شمس، جمعاً نه شهر با چراگاههای اطراف از قبیلهٔ یهودا و شمعون. 16
Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.
از ملک قبیلهٔ بنیامین، این چهار شهر با چراگاههای اطراف داده شد: جبعون، جبع، عناتوت و علمون. 17
Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba,
18
Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
پس جمعاً سیزده شهر با چراگاههای اطراف، به نسل هارون که کاهن بودند تعلق گرفت. 19
Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.
از طرف قبیلهٔ افرایم، چهار شهر و چراگاههای اطراف آنها به بقیهٔ خاندان قهاتی از لاویان، داده شد. این شهرها عبارت بودند از: شکیم (یکی از شهرهای پناهگاه که در کوهستان افرایم واقع بود)، جازر، قبصایم و بیت‌حورون. 20
Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:
21
Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu.
22
Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
از طرف قبیلهٔ دان چهار شهر با چراگاههای اطراف آنها به ایشان بخشیده شد. این شهرها عبارت بودند از: التقی، جِبَتون، اَیَلون و جَت‌رِمون. 23
Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni,
24
Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
نصف قبیلهٔ منسی، شهرهای تعنک، جت‌رمون و چراگاههای اطراف آنها را به ایشان بخشید. 25
Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.
به این ترتیب، جمعاً ده شهر با چراگاههای اطراف آنها به باقیماندهٔ خاندان قهات داده شد. 26
Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.
به خاندان جرشون نیز که یکی دیگر از گروه‌های قبیله لاوی بود این شهرها داده شد: از طرف نصف قبیلهٔ منسی، جولان در باشان (یکی از شهرهای پناهگاه) و بَعَشتره، جمعاً دو شهر با چراگاههای اطراف. 27
Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri kuchokera ku theka la Manase wa kummawa, Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.
از طرف قبیلهٔ یساکار؛ شهرهای قشیون، دابره، 28
Fuko la Isakara linapereka mizinda ya Kisoni, Daberati,
یرموت و عین‌جنیم، جمعاً چهار شهر با چراگاههای اطراف. 29
Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
از قبیلهٔ اشیر؛ شهرهای مش‌آل، عبدون، 30
Fuko la Aseri linapereka mizinda ya Misali, Abidoni,
حلقات و رحوب، جمعاً چهار شهر با چراگاههای اطراف. 31
Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
از قبیلهٔ نفتالی؛ شهرهای قادش در جلیل (یکی از شهرهای پناهگاه)، حموت دُر و قرتان، جمعاً سه شهر با چراگاههای اطراف. 32
Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
پس سیزده شهر با چراگاههای اطراف آنها به خاندان جرشون داده شد. 33
Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.
به بقیهٔ قبیله لاوی که خاندان مراری را تشکیل می‌دادند، این شهرها داده شد: از قبیلهٔ زبولون؛ شهرهای یُقنعام، قَرته، 34
Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni: Yokineamu, Karita,
دمنه و نحلال، جمعاً چهار شهر با چراگاههای اطراف. 35
Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
از قبیلهٔ رئوبین؛ شهرهای باصر، یهصه، 36
Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira Bezeri, Yahaza,
قدیموت و میفعت، چهار شهر با چراگاههای اطراف. 37
Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.
از قبیلهٔ جاد؛ شهرهای راموت در جلعاد (یکی از شهرهای پناهگاه)، محنایم، 38
Kuchokera ku fuko la Gadi analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi.
حشبون و یعزیر، چهار شهر با چراگاههای اطراف. 39
Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.
روی‌هم‌رفته دوازده شهر به حکم قرعه به خاندان مراری که بقیهٔ قبیله لاوی را تشکیل می‌دادند، داده شد. 40
Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.
بدین ترتیب از سرزمینی که متعلق به بنی‌اسرائیل بود چهل و هشت شهر با چراگاههای اطراف آنها به قبیلهٔ لاوی داده شد. 41
Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto.
42
Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.
پس خداوند، تمام سرزمینی را که به اجداد قوم اسرائیل وعده فرموده بود به بنی‌اسرائیل بخشید و ایشان آن را تصرف نموده، در آن ساکن شدند. 43
Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo.
خداوند چنانکه به اجداد آنها وعده داده بود در سرزمین اسرائیل صلح برقرار نمود و کسی را یارای مقاومت با آنها نبود. خداوند ایشان را یاری نمود تا دشمنان خود را نابود کنند. 44
Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo.
او به تمام وعده‌های نیکویی که به قوم اسرائیل داده بود وفا کرد. 45
Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.

< یوشع 21 >