< یوحنا 16 >
«این امور را از هم اکنون به شما میگویم تا وقتی با مشکلات روبرو میشوید، ایمان خود را از دست ندهید. | 1 |
“Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
شما را از کنیسهها بیرون خواهند راند و حتی زمانی فرا خواهد رسید که مردم شما را خواهند کشت به خیال اینکه خدا را خدمت میکنند. | 2 |
Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
به این علّت با شما اینچنین رفتار خواهند کرد که نه پدر را میشناسند، و نه مرا. | 3 |
Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
پس در آن موقع به یاد داشته باشید که خبر تمام این پیشآمدها را از قبل به شما دادهام. علّت اینکه این موضوع را زودتر به شما نگفتم این است که خودم با شما بودم. | 4 |
Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
«اما اکنون نزد کسی میروم که مرا فرستاد، و هیچیک از شما نمیپرسید:”به کجا میروی؟“ | 5 |
“Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
در عوض غمگین و محزونید. | 6 |
Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
رفتن من به نفع شماست، چون اگر نروم، آن روح تسلیبخش نزد شما نخواهد آمد. ولی اگر بروم او خواهد آمد، زیرا من او را نزد شما خواهم فرستاد. | 7 |
Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
وقتی او بیاید، جهان را در رابطه با گناه، عدالت خدا و داوری آینده محکوم خواهد کرد. | 8 |
Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
گناهِ جهان آن است که نمیخواهد به من ایمان بیاورد. | 9 |
Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
عدالت خدا ظاهر میشود زیرا من نزد پدر میروم و دیگر مرا نخواهید دید. | 10 |
Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
داوری خواهد آمد، زیرا رئیس این جهان هم اکنون تحت محکومیت قرار دارد. | 11 |
Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
«بسیار چیزهای دیگر دارم که بگویم، ولی افسوس که حال نمیتوانید بفهمید. | 12 |
“Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
ولی وقتی روحالقدس که سرچشمۀ همهٔ راستیها است بیاید، تمام حقایق را بر شما آشکار خواهد ساخت. زیرا از جانب خود سخن نخواهد گفت، بلکه آنچه را که از من شنیده است، بیان خواهد کرد. او از آینده نیز شما را باخبر خواهد ساخت. | 13 |
Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
او جلال و بزرگی مرا به شما نشان خواهد داد و با این کار باعث عزت و احترام من خواهد شد. | 14 |
Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
تمام بزرگی و جلال پدرم از آن من است. وقتی گفتم جلال و بزرگی مرا به شما نشان میدهد، منظورم همین بود. | 15 |
Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
«بهزودی خواهم رفت و دیگر مرا نخواهید دید. ولی بعد از مدت کوتاهی باز میگردم و دوباره مرا خواهید دید.» | 16 |
Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
بعضی از شاگردان او از یکدیگر پرسیدند: «استاد چه میگوید؟ منظورش از این سخن چیست که میگوید:”دیگر مرا نخواهید دید، ولی بعد از مدت کوتاهی دوباره مرا خواهید دید؟“ | 17 |
Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
منظورش از”نزد پدر میروم“چیست؟» | 18 |
Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
عیسی متوجه شد که شاگردان میخواهند از او سؤال کنند. پس فرمود: «میپرسید منظورم چیست که گفتم:”دیگر مرا نخواهید دید، ولی بعد از مدت کوتاهی خواهید دید؟“ | 19 |
Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
مردم دنیا از رفتن من شاد خواهند شد، ولی شما محزون خواهید گردید و خواهید گریست. ولی وقتی دوباره مرا ببینید، گریهٔ شما تبدیل به شادی خواهد شد. | 20 |
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
همچون زنی که درد میکشد تا نوزادی به دنیا آورد؛ ولی بعد از زایمان، رنج او به شادی تبدیل میشود و درد را فراموش میکند، زیرا انسان جدیدی به دنیا آورده است. | 21 |
Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
شما نیز اکنون غمگین میباشید، ولی دوباره شما را خواهم دید. آنگاه شاد خواهید شد و کسی نمیتواند آن شادی را از شما بگیرد. | 22 |
Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
در آن هنگام دیگر از من چیزی نخواهید خواست. من واقعیت را به شما میگویم، شما خودتان هر چه از پدرم به نام من بخواهید، به شما خواهد داد. | 23 |
Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
تا به حال به نام من چیزی نخواستهاید. بخواهید تا بیابید و شاد شوید و شادیتان کامل گردد. | 24 |
Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
«این چیزها را با مَثَلها به شما گفتم. ولی زمانی فرا میرسد که دیگر نیازی به این کار نخواهد بود و همه چیز را به روشنی دربارهٔ پدرم به شما خواهم گفت. | 25 |
“Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
آنگاه به نام من درخواست خواهید کرد. البته لازم نیست که من سفارش شما را به پدر بکنم تا آنچه را که میخواهید به شما بدهد؛ | 26 |
Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
چرا که خودِ پدر، شما را دوست دارد، زیرا شما مرا دوست دارید و ایمان دارید که من از نزد پدرم آمدهام. | 27 |
Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
بله، من از نزد پدرم خدا به این دنیا آمدهام، و حال دنیا را میگذارم و نزد او باز میگردم.» | 28 |
Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
شاگردان گفتند: «اکنون آشکارا با ما سخن میگویی و نه با مَثَل. | 29 |
Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
اکنون پی بردیم که همه چیز را میدانی و حتی نیاز نداری کسی سؤالش را با تو در میان بگذارد. همین برای ما کافی است تا ایمان بیاوریم که شما از نزد خدا آمدهاید.» | 30 |
Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
عیسی پرسید: «آیا سرانجام به این موضوع ایمان آوردید؟ | 31 |
Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
ولی وقتی میرسد، و یا بهتر بگویم همین الان رسیده است که شما مانند کاه پراکنده میشوید و هر یک به خانۀ خود برمیگردید و مرا تنها میگذارید. ولی من تنها نیستم، چون پدرم با من است. | 32 |
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
این چیزها را گفتم تا خیالتان آسوده باشد. در این دنیا با مشکلات و زحمات فراوان روبرو خواهید شد؛ با این حال شجاع باشید، چون من بر دنیا پیروز شدهام.» | 33 |
“Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”