< ایوب 39 >
آیا زمان زاییدن بز کوهی را میدانی؟ آیا وضع حمل آهو را با چشم خود دیدهای؟ | 1 |
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
آیا میدانی چند ماه طول میکشد تا بچههای خود را زاییده از بارداری فارغ شوند؟ | 2 |
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
بچههای آنها در صحرا رشد میکنند، سپس والدین خود را ترک نموده، دیگر نزدشان برنمیگردند. | 4 |
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
چه کسی خر وحشی را رها کرده است؟ چه کسی بندهای او را گشوده است؟ | 5 |
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
من بیابانها و شورهزارها را مسکن آنها ساختهام. | 6 |
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
از سر و صدای شهر بیزارند و کسی نمیتواند آنها را رام کند. | 7 |
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
دامنهٔ کوهها چراگاه آنهاست و در آنجا هر سبزهای پیدا کنند میخورند. | 8 |
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
آیا گاو وحشی راضی میشود تو را خدمت کند؟ آیا او کنار آخور تو میایستد؟ | 9 |
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
آیا میتوانی گاو وحشی را با طناب ببندی تا زمینت را شخم بزند؟ | 10 |
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
آیا صرفاً به خاطر قوت زیادش میتوانی به او اعتماد کنی و کار خودت را به او بسپاری؟ | 11 |
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
آیا میتوانی او را بفرستی تا محصول تو را بیاورد و در خرمنگاه جمع کند؟ | 12 |
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
شترمرغ با غرور بالهایش را تکان میدهد، ولی نمیتواند مانند لکلک پرواز کند. | 13 |
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
شترمرغ تخمهای خود را روی زمین میگذارد تا خاک آنها را گرم کند. | 14 |
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
او فراموش میکند که ممکن است کسی بر آنها پا بگذارد و آنها را له کند و یا حیوانات وحشی آنها را از بین ببرند. | 15 |
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
او نسبت به جوجههایش چنان بیتوجه است که گویی مال خودش نیستند، و اگر بمیرند اعتنایی نمیکند؛ | 16 |
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
زیرا من او را از فهم و شعور محروم کردهام. | 17 |
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
ولی هر وقت بالهایش را باز میکند تا بدود هیچ اسب و سوارکاری به پایش نمیرسد. | 18 |
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
آیا قوت اسب را تو به او دادهای؟ یا تو گردنش را با یال پوشانیدهای؟ | 19 |
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
آیا تو به او توانایی بخشیدهای تا چون ملخ خیز بردارد و با خُرناسِ مهیبش وحشت ایجاد کند؟ | 20 |
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
ببین چگونه سم خود را به زمین میکوبد و از قدرت خویش لذت میبرد. هنگامی که به جنگ میرود نمیهراسد؛ تیغ شمشیر و رگبار تیر و برق نیزه او را به عقب بر نمیگرداند. | 21 |
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
وحشیانه سم بر زمین میکوبد و به مجرد نواخته شدن شیپور حمله، به میدان کارزار یورش میبرد. | 24 |
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
با شنیدن صدای شیپور، شیهه برمیآورد و بوی جنگ را از فاصلهٔ دور استشمام میکند. از غوغای جنگ و فرمان سرداران به وجد میآید. | 25 |
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
آیا تو به شاهین یاد دادهای که چگونه بپرد و بالهایش را به سوی جنوب پهن کند؟ | 26 |
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
آیا به فرمان توست که عقاب بر فراز قلهها به پرواز در میآید تا در آنجا آشیانهٔ خود را بسازد؟ | 27 |
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
ببین چگونه روی صخرهها آشیانه میسازد و بر قلههای بلند زندگی میکند | 28 |
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
و از آن فاصلهٔ دور، شکار خود را زیر نظر میگیرد. | 29 |
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
ببین چگونه دور اجساد کشته شده را میگیرد و جوجههایشان خون آنها را میخورد. | 30 |
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”