< ایوب 37 >
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
گوش دهید و غرش صدای خدا را بشنوید. | 2 |
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
او برق خود را به سراسر آسمان میفرستد. | 3 |
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
سپس غرش صدای او شنیده میشود، غرش مهیب رعد به گوش میرسد و باز برق، آسمان را روشن میکند. | 4 |
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
صدای او در رعد باشکوه است. ما نمیتوانیم عظمت قدرت او را درک کنیم. | 5 |
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
وقتی او برف و باران شدید بر زمین میفرستد، | 6 |
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
مردم از کار کردن باز میمانند و متوجه قدرت او میشوند، | 7 |
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
حیوانات وحشی به پناهگاه خود میشتابند و در لانههای خویش پنهان میمانند. | 8 |
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
از جنوب طوفان میآید و از شمال سرما. | 9 |
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
خدا بر آبها میدمد، به طوری که حتی وسیعترین دریاها نیز یخ میبندد. | 10 |
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
او ابرها را از رطوبت، سنگین میکند و برق خود را بهوسیلۀ آنها پراکنده میسازد. | 11 |
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
آنها به دستور او به حرکت در میآیند و احکام او را در سراسر زمین به جا میآورند. | 12 |
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
او ابرها را برای مجازات مردم و یا برای سیراب کردن زمین و نشان دادن رحمتش به ایشان، میفرستد. | 13 |
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
ای ایوب، گوش بده و دربارهٔ اعمال شگفتآور خدا تأمل و تفکر کن. | 14 |
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
آیا تو میدانی که خدا چگونه تمام طبیعت را اداره نموده، برق را از ابرها ساطع میکند؟ | 15 |
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
آیا تو میدانی چگونه ابرها در هوا معلق میمانند؟ آیا تو عظمت این کار خدا را میتوانی درک کنی؟ | 16 |
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
آیا وقتی زمین زیر وزش باد گرم جنوب قرار دارد و لباسهایت از گرما به تنت چسبیده است، | 17 |
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
تو میتوانی به خدا کمک کنی تا وضع آسمان را که مانند فلز سخت است تغییر دهد؟ | 18 |
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
آیا تو میتوانی به ما بگویی چگونه باید با خدا مواجه شد؟ ما با این فکر تاریکمان نمیدانیم چگونه با او سخن گوییم. | 19 |
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
من با چه جرأتی با خدا صحبت کنم؟ چرا خود را به کشتن دهم؟ | 20 |
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
همانطور که در یک روز آفتابی بیابر، نمیتوانیم به تابش خورشید نگاه کنیم، | 21 |
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
همچنان نیز نمیتوانیم به جلال پرشکوه خدا که از آسمان با درخشندگی خیرهکنندهای بر ما نمایان میشود خیره شویم. | 22 |
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
ما نمیتوانیم به قدرت خدای قادر مطلق پی ببریم. او نسبت به ما عادل و رحیم است و بر کسی ظلم نمیکند، | 23 |
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
و تحت تأثیر داناترین مردم جهان نیز قرار نمیگیرد، از این جهت ترس و احترام او در دل همهٔ مردم جا دارد. | 24 |
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”