< ایوب 28 >
مردم میدانند چگونه نقره را از معدن استخراج نمایند، طلا را تصفیه کنند، | 1 |
Pali mgodi wa siliva ndiponso malo oyengerapo golide.
آهن را از زمین بیرون آورند و مس را از سنگ جدا سازند. | 2 |
Chitsulo amachikumba pansi, ndipo mkuwa amawusungunula ku miyala yamkuwa.
آنها میدانند چطور معادن تاریک را روشن کنند و در جستجوی سنگهای معدن تا عمقهای تاریک زمین فرو روند. | 3 |
Munthu amalowa mu mdima atatenga nyale, amafunafuna miyala mpaka ku malire a mgodiwo, kufuna mkuwa mu mdima wandiweyani.
آنها در نقاطی دور دست، جایی که پای بشری بدان راه نیافته، در دل زمین نقب میزنند و از طنابها آویزان شده، به عمق معادن میروند. | 4 |
Amakumba njira zapansi mu mgodimo, kutali ndi kumene kumakhala anthu, kumalo kumene phazi la munthu silinapondeko; iye amakhala ali lende pansipo namazungulira uku ndi uku.
مردم میدانند چگونه از روی زمین غذا تهیه کنند، در حالی که در زیر پوستهٔ همین زمین، آتش نهفته است. | 5 |
Nthaka, imene imatulutsa zakudya, kunsi kwake kumachita ngati kwasandulizika ndi moto;
آنها میدانند چگونه از سنگهای آن یاقوت و طلا به دست بیاورند. | 6 |
miyala ya safiro imachokera mʼmatanthwe ake, ndipo mʼfumbi lake mumakhala miyala yagolide.
حتی پرندگان شکاری راه معادن را نمیدانند و چشم هیچ عقابی آن را نمیتواند ببیند؛ | 7 |
Palibe mbalame yodya zinzake imene imadziwa njira yobisikayi, palibe kamtema amene anayiona.
پای شیر یا جانور درندهٔ دیگری به این معادن نرسیده است؛ | 8 |
Zirombo zolusa sizipondamo mʼnjiramo, ndipo mkango sudzeranso mʼmenemo.
ولی مردم میدانند چطور سنگهای خارا را تکهتکه نموده، کوهها را از بیخ و بن برکنند، | 9 |
Munthu amaphwanya matanthwe olimba, ndipo amagubuduza mapiri kuyambira mʼtsinde.
صخرهها را بشکافند و به سنگهای قیمتی دست یابند. | 10 |
Amabowola njira mʼmatanthwewo; ndipo amaona chuma chonse cha mʼphirimo.
آنها حتی سرچشمهٔ رودها را کاوش میکنند و گنجهای مخفی از آن بیرون میآورند. | 11 |
Amaletsa mitsinje ya pansipo kuti isayendenso, motero amatulutsira poyera zinthu zobisika.
مردم همهٔ اینها را میدانند، ولی نمیدانند فهم و حکمت را در کجا بیابند. | 12 |
“Koma nzeru zingapezeke kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
حکمت در بین انسانها پیدا نمیشود و هیچکس ارزش آن را نمیداند. | 13 |
Munthu sadziwa kufunika kwake kwa nzeruzo; nzeruyo sipezeka pa dziko lino la anthu amoyo.
اقیانوسها میگویند: «در اینجا حکمت نیست.» و دریاها جواب میدهند: «در اینجا هم نیست.» | 14 |
Phompho likuti, ‘Sizipezeka mwa ine muno.’ Nyanja ikuti, ‘Mwa ine munonso ayi.’
حکمت را با طلا و نقره نمیتوان خرید، | 15 |
Nzeru sungazigule ndi golide wabwino kwambiri, mtengo wake sungawuyerekeze ndi siliva wambiri.
و نه با طلای خالص و سنگهای قیمتی. | 16 |
Nzeru singagulidwe ndi golide wa ku Ofiri, kapena ndi miyala ya onikisi kapena ya safiro.
حکمت از طلا و الماس بسیار گرانبهاتر است و آن را نمیتوان با جواهرات خریداری کرد. | 17 |
Nzeru sungayiyerekeze ndi golide kapena mwala wa galasi, sungayigule ndi zokometsera zagolide.
مرجان و بلور در برابر حکمت هیچ ارزشی ندارند. قیمت آن از لعل بسیار گرانتر است. | 18 |
Miyala ya korali ndi krisitali siyoyeneranso ndi kuyitchula nʼkomwe; mtengo wa nzeru ndi woposa miyala ya rubi.
نه میتوان آن را با زبرجد مرغوب خرید و نه با طلای ناب. | 19 |
Nzeru sungayiyerekeze ndi miyala ya topazi ya ku Kusi; nzeru singagulidwe ndi golide wabwino kwambiri.
پس حکمت را از کجا میتوان به دست آورد؟ در کجا پیدا میشود؟ | 20 |
“Kodi tsono nzeru zimachokera kuti? Kodi kumvetsa zinthu kumakhala kuti?
زیرا از چشمان تمامی افراد بشر پنهان است. حتی از چشمان تیزبین پرندگان هوا نیز مخفی است؛ | 21 |
Malo ake ndi obisika kwa zamoyo zonse, ndi obisika ngakhale kwa mbalame zamlengalenga.
هلاکت و مرگ میگویند: «ما فقط شایعاتی در مورد مکان حکمت شنیدهایم.» | 22 |
Chiwonongeko ndi imfa zikuti, ‘Tangomva mphekesera chabe ya zimenezo!’
فقط خدا میداند که حکمت را کجا میتوان پیدا کرد؛ | 23 |
Mulungu yekha ndiye amadziwa njira yake yopita kumeneko, ndipo Iye yekha amadziwa kumene nzeru imakhala,
زیرا او تمامی زمین را زیر نظر دارد و آنچه را که در زیر آسمان است مشاهده میکند. | 24 |
pakuti Iye amayangʼana mpaka ku malekezero a dziko lapansi ndipo amaona zonse za kunsi kwa thambo.
او باد را به حرکت درمیآورد و حدود اقیانوسها را تعیین میکند. | 25 |
Iye atapatsa mphepo mphamvu zake, nayeza kuzama kwa nyanja,
به باران فرمان میدهد که ببارد و مسیر برق آسمان را تعیین میکند. | 26 |
atakhazikitsa lamulo loti mvula izigwa ndi kukonza njira ya chingʼaningʼani cha bingu,
پس او میداند حکمت کجاست. او آن را آزمایش کرده و تأیید نموده است، | 27 |
pamenepo ndi pamene anayangʼana nzeruzo naziyeza mtengo wake; nazikhazikitsa ndi kuzisanthula bwino lomwe.
و به افراد بشر میگوید: «بدانید که ترس از خداوند، حکمت واقعی، و دوری نمودن از شرارت، فهم حقیقی میباشد.» | 28 |
Ndipo Iye anati kwa munthu, ‘Taonani, kuopa Ambuye, ndiye nzeru zimenezo ndipo kuthawa zoyipa ndiye kumvetsa zinthu kumeneko.’”