< ارمیا 17 >

«ای قوم یهودا، گناهان شما با قلم آهنین و با نوک الماس بر دلهای سنگی‌تان نوشته شده و بر گوشه‌های مذبحهایتان کنده‌کاری شده است. 1
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
جوانانتان یک دم از گناه غافل نمی‌مانند، زیر هر درخت سبز و روی هر کوه بلند بت می‌پرستند؛ پس به سبب گناهانتان، تمام گنجها و بتخانه‌هایتان را به تاراج خواهم داد، 2
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
و مجبور خواهید شد این سرزمین را که به میراث به شما داده بودم ترک کنید و دشمنانتان را در سرزمینهای دور دست بندگی نمایید، چون آتش خشم مرا شعله‌ور ساخته‌اید، آتشی که هرگز خاموش نخواهد شد! 4
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
«لعنت بر کسی که به انسان تکیه می‌کند و چشم امیدش به اوست و بر خداوند توکل نمی‌نماید. 5
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
او مثل بوته‌ای است که در بیابان خشک و سوزان و در شوره‌زارها می‌روید، جایی که هیچ گیاه دیگری وجود ندارد؛ او هرگز خیر و برکت نخواهد دید! 6
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
«خوشا به حال کسی که بر خداوند توکل دارد و تمام امید و اعتمادش بر اوست! 7
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
او مانند درختی خواهد بود که در کنار رودخانه است و ریشه‌هایش از هر طرف به آب می‌رسد درختی که نه از گرما می‌ترسد و نه از خشکسالی! برگش شاداب می‌ماند و از میوه آوردن باز نمی‌ایستد! 8
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
«هیچ چیز مانند دل انسان فریبکار و شرور نیست؛ کیست که از آنچه در آن می‌گذرد آگاه باشد؟ 9
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
تنها من که خداوند هستم می‌دانم در دل انسان چه می‌گذرد! تنها من از درون دل انسان آگاهم و انگیزه‌های او را می‌دانم و هر کس را مطابق اعمالش جزا می‌دهم.» 10
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
شخصی که ثروتش را از راه نادرست به دست می‌آورد، همانند پرنده‌ای است که لانهٔ خود را از جوجه‌های دیگران پر می‌سازد. همان‌گونه که این جوجه‌ها خیلی زود او را واگذاشته می‌روند، او نیز به‌زودی ثروتش را از دست خواهد داد و سرانجام چوب حماقتش را خواهد خورد. 11
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
اما ما در برابر تاج جاودانی، رفیع و پرجلال تو ستایش می‌کنیم. 12
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
ای خداوند، ای امید اسرائیل، تمام کسانی که از تو برگردند، رسوا و شرمسار می‌شوند؛ آنها مانند نوشته‌های روی خاک محو خواهند شد، چون خداوند را که چشمۀ آب حیات است، ترک کرده‌اند. 13
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
خداوندا، تنها تو می‌توانی مرا شفا بخشی، تنها تو می‌توانی مرا نجات دهی و من تنها تو را ستایش می‌کنم! 14
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
مردم با تمسخر به من می‌گویند: «پس هشدارهای خداوند که مدام دربارهٔ آنها سخن می‌گفتی چه شد؟ اگر آنها واقعاً از سوی خدا هستند، پس چرا انجام نمی‌شوند؟» 15
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
خداوندا، من هیچگاه از تو نخواسته‌ام که بر آنها بلا نازل کنی و هرگز خواستار هلاکت ایشان نبوده‌ام؛ تو خوب می‌دانی که من تنها هشدارهای تو را به ایشان اعلام کرده‌ام. 16
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
خداوندا، مرا به وحشت نیانداز! تنها امید من در روز مصیبت، تو هستی! 17
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
تمام کسانی را که مرا آزار می‌دهند، به رسوایی و هراس گرفتار بساز، ولی مرا از هر بلایی محفوظ بدار. آری، بر ایشان دو چندان بلا بفرست و نابودشان کن! 18
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
آنگاه خداوند فرمود که بروم و در کنار دروازهٔ قوم که پادشاهان یهودا از آن عبور می‌کنند و در کنار سایر دروازه‌های اورشلیم بایستم، 19
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
و در آنجا خطاب به همۀ مردم بگویم که خداوند چنین می‌فرماید: «ای پادشاهان و مردم یهودا، ای ساکنان اورشلیم و همۀ کسانی که از این دروازه‌ها عبور می‌کنید، 20
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
به این هشدار توجه کنید تا زنده بمانید: نباید در روز شَبّات کار کنید بلکه این روز را به عبادت و استراحت اختصاص دهید. به اجدادتان هم همین دستور را دادم، 21
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
ولی آنها گوش ندادند و اطاعت نکردند بلکه با سرسختی به دستور من بی‌توجهی نمودند و اصلاح نشدند. 23
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
«حال، اگر شما از من اطاعت نمایید و روز شَبّات را مقدّس بدارید و در این روز کار نکنید، 24
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
آنگاه پادشاهانی که بر تخت داوود می‌نشینند، سوار بر ارابه‌ها و اسبان، همراه با صاحبمنصبان و مردمان یهودا و ساکنان اورشلیم از دروازه‌های این شهر داخل خواهند شد، و این شهر تا به ابد مسکون خواهد ماند. 25
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
از اطراف اورشلیم و از شهرهای یهودا و سرزمین بنیامین و از دشتها و کوهستانها و جنوب یهودا مردم همه خواهند آمد و قربانیهای گوناگون به خانۀ خداوند تقدیم خواهند نمود. 26
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
«اما اگر از من اطاعت نکنید و روز شَبّات را به عبادت و استراحت اختصاص ندهید، و اگر در این روز همچون روزهای دیگر، از دروازه‌های اورشلیم کالا به شهر وارد کنید، آنگاه این دروازه‌ها را به آتش خواهم کشید، آتشی که به کاخهایتان سرایت کند و آنها را از بین ببرد و هیچ‌کس نتواند شعله‌های آن را خاموش کند.» 27
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”

< ارمیا 17 >