< اشعیا 60 >

ای اورشلیم برخیز و بگذار نور تو بدرخشد، زیرا جلال خداوند بر تو تابان است! 1
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
تمام قومهای جهان در تاریکی فرو خواهند رفت، اما نور جلال خداوند بر تو خواهد تابید، 2
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
و پادشاهان و قومها به سوی تو خواهند آمد تا نور جلال خداوند را که بر تو تابان است مشاهده کنند. 3
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
به اطراف خود نگاه کن و ببین چگونه قوم تو جمع شده به سوی تو می‌آیند. ایشان پسران و دخترانت را در آغوش گرفته، از راه دور به وطن باز می‌گردند. 4
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
تو این را به چشم خواهی دید و شاد خواهی شد و از شدت هیجان خواهی لرزید. گنجهای جهان از راه دریا به سوی تو خواهد آمد و ثروت قومها نزد تو جمع خواهد شد. 5
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
کاروانهای شتر از مِدیان و عیفه و صبا خواهند آمد و با خود طلا و بخور خواهند آورد. مردم خداوند را ستایش خواهند کرد و کارهای او را بشارت خواهند داد. 6
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
تمام گله‌های قیدار و نبایوت را نزد تو خواهند آورد تا بر مذبح خانهٔ خداوند قربانی کنند. در آن روز خداوند خانهٔ پرشکوه خود را زینت خواهد داد. 7
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
اینها کیستند که مانند ابر به سوی سرزمین اسرائیل در حرکتند؟ ایشان به کبوترهایی می‌مانند که به لانه‌های خود باز می‌گردند. 8
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
اینها قوم خدا هستند که سوار بر کشتی از سرزمینهای دور دست به وطن باز می‌گردند و با خود طلا و نقره می‌آورند، زیرا خدای مقدّس اسرائیل که در تمام دنیا مشهور است، قوم خود را در نظر همهٔ قومها عزت و احترام بخشیده است. 9
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
خداوند به اورشلیم می‌گوید: «بیگانگان آمده، دیوارهای تو را بازسازی خواهند کرد و پادشاهان آنها تو را خدمت خواهند نمود، زیرا هر چند در خشم خود تو را مجازات کردم، اما به لطف خویش بر تو رحم خواهم کرد. 10
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
روز و شب، دروازه‌هایت باز خواهد بود تا پادشاهان جهان ثروت کشورهای خود را نزد تو بیاورند. 11
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
هر قومی که نخواهد تو را خدمت کند، هلاک شده، از بین خواهد رفت. 12
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
«از جنگل لبنان چوبهای درختان صنوبر و کاج و چنار را برای تو ای اورشلیم خواهند آورد تا تو را بازسازی کنند و خانهٔ مرا تزئین نمایند و شهر مرا باشکوه سازند. 13
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
پسران کسانی که بر تو ظلم کرده‌اند خواهند آمد و در مقابل تو زانو زده، تعظیم خواهند کرد و کسانی که تو را تحقیر کرده‌اند بر پاهایت خواهند افتاد و تو را سجده خواهند کرد. آنها تو را شهر خداوند و صَهیون قدوس اسرائیل خواهند نامید. 14
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
«تو زمانی متروک و مطرود بودی و کسی از تو عبور نمی‌کرد، اما اینک تو را برای همیشه باشکوه می‌سازم و تو تا ابد محل شادمانی خواهی بود. 15
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
قومها و پادشاهان جهان نیازهای تو را برآورده خواهند ساخت و مانند یک مادر از تو مراقبت خواهند نمود. آنگاه خواهی فهمید که من یهوه خدای قادر اسرائیل، حامی و نجا‌ت‌دهندۀ تو هستم. 16
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
«من مفرغ تو را به طلا تبدیل می‌کنم و آهن تو را به نقره، چوب تو را به مفرغ، و سنگ تو را به آهن. رهبران و حاکمانی به تو خواهم داد که با صلح و عدالت بر تو حکومت کنند. 17
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
ظلم و خرابی را از تو دور خواهم کرد و مانند دیواری محافظ، تو را احاطه خواهم نمود و تو مرا سپاس خواهی گفت چرا که تو را نجات داده‌ام. 18
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
«تو دیگر به روشنایی خورشید و ماه احتیاج نخواهی داشت، زیرا من که خداوند هستم نور جاودانی تو و زیبایی تو خواهم بود. 19
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
آفتاب تو هرگز غروب نخواهد کرد و ماه تو زوال نخواهد پذیرفت، زیرا من نور جاودانی تو خواهم بود، و روزهای سوگواریت پایان خواهند یافت. 20
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
همهٔ افراد قوم تو مردمانی درستکار خواهند بود و سرزمین خود را تا ابد حفظ خواهند کرد. من ایشان را با دستان خود در آنجا خواهم کاشت تا عظمت و جلال خود را ظاهر کنم. 21
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
حتی کوچکترین و ضعیفترین خاندان تو بزرگ شده، به قومی نیرومند تبدیل خواهد شد. هنگامی که زمان معین فرا رسد من که یهوه هستم این را بی‌درنگ انجام خواهم داد.» 22
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< اشعیا 60 >