< اشعیا 39 >
در آن روزها «مردوک بلدان» (پسر «بلدان») پادشاه بابِل، نامهای همراه با هدیهای برای حِزِقیا فرستاد، زیرا شنیده بود که پس از یک بیماری سخت اینک بهبود یافته است. | 1 |
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
حِزِقیا فرستادگان بابِلی را به خوشی پذیرفت و آنان را به کاخ سلطنتی برد و تمام خزانههای طلا و نقره، عطریات و روغنهای معطر، و نیز اسلحهخانهٔ خود را به ایشان نشان داد. بدین ترتیب، فرستادگان بابِلی تمام خزاین او را دیدند و چیزی از نظر آنان پوشیده نماند. | 2 |
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
آنگاه اشعیای نبی نزد حِزِقیای پادشاه رفت و از او پرسید: «این مردان از کجا آمده بودند و چه میخواستند؟» حِزِقیا جواب داد: «از جای دور! آنها از بابِل آمده بودند.» | 3 |
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
اشعیا پرسید: «در کاخ تو چه دیدند؟» حِزِقیا جواب داد: «تمام خزاین مرا.» | 4 |
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
اشعیا به او گفت: «پس به این پیام که از سوی خداوند لشکرهای آسمان است گوش کن: | 5 |
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
«زمانی میرسد که هر چه در کاخ داری و گنجهایی که اجدادت اندوختهاند به بابِل برده خواهد شد و چیزی از آنها باقی نخواهد ماند. | 6 |
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
بابِلیها برخی از پسرانت را به اسارت گرفته، آنان را خواجه خواهند کرد و در کاخ پادشاه بابِل به خدمت خواهند گماشت.» | 7 |
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
حِزِقیا جواب داد: «پیامی که از جانب خداوند به من دادی، نیکوست.» زیرا با خود فکر میکرد که: «دستکم تا وقتی که زندهام این اتفاق نخواهد افتاد و صلح و امنیت برقرار خواهد بود.» | 8 |
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”