< اشعیا 23 >

پیامی برای صور: ای کشتی‌های ترشیش که از سرزمینهای دور دست باز می‌گردید، برای صور گریه کنید، زیرا چنان ویران شده که نه خانه‌ای و نه بندرگاهی برایش باقی مانده است! آنچه در قبرس درباره‌اش شنیدید حقیقت دارد. 1
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
زمانی بندر صور مرکز تجارت دنیا محسوب می‌شد. کشتیهای صیدون که از مصر غله و از رود نیل حصاد می‌آوردند تا تاجران صیدون با آن با تمام دنیا تجارت کنند، در این بندر لنگر می‌انداختند. اما اینک صور در سکوت مرگبار فرو رفته است! 2
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
شرم بر تو باد ای صیدون، ای فرزند مستحکم دریا! زیرا دریا می‌گوید: «من هرگز درد نکشیده و نزاییده‌ام و کودکی پرورش نداده‌ام.» 4
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
چون خبر خرابی صور به مصر رسد او نیز سخت خواهد ترسید. 5
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
ای مردم فنیقیه، گریه‌کنان به ترشیش فرار کنید! 6
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
آیا این همان شهر تاریخی و پرشکوه شما، صور است که چنین ویران گشته؟ زمانی مردم صور به جاهای دور می‌رفتند تا سرزمینها را تصاحب کرده آنها را محل سکونت خود سازند. 7
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
چه کسی این مصیبت را بر سر این شهر سلطنتی که تجار و بازرگانانش در تمام جهان معروفند، آورده است؟ 8
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
خداوند لشکرهای آسمان این کار را کرده تا غرور صور را بشکند و آنانی را که در جهان معروفند خوار سازد. 9
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
ای مردم ترشیش، سرزمین خود را مثل کناره‌های رود نیل حاصلخیز کنید، زیرا دیگر مانعی بر سر راه شما نیست. 10
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
خداوند دست خود را بر دریا دراز کرده ممالک دنیا را تکان می‌دهد. او دستور داده که شهرهای تجاری فنیقیه را ویران کنند. 11
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
ای مردم بلا دیدهٔ صیدون، شما دیگر از آسایش برخوردار نخواهید شد. اگر به قبرس نیز فرار کنید در آنجا راحت نخواهید بود. 12
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
به بابِل نگاه کنید! ببینید چگونه مردم این سرزمین از بین رفتند! آشوری‌ها بابِل را به محلی جهت وحوش صحرا تبدیل کردند؛ آنها شهر را محاصره کرده، با منجنیقهایشان کاخهایش را در هم کوبیدند و این سرزمین را با خاک یکسان کردند. 13
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
ای کشتی‌های ترشیش که در دریا هستید زاری کنید، زیرا بندرگاه شما ویران شده است. 14
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
صور مدت هفتاد سال، که طول عمر یک پادشاه است، به فراموشی سپرده خواهد شد. پس از آن هفتاد سال، صور مانند فاحشهٔ آن سرودی خواهد بود که کلماتش چنین است: 15
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
«ای فاحشهٔ فراموش شده، چنگ را به دست بگیر و در شهر بگرد. خوش بنواز و آوازهای بسیار بخوان، تا مردم دوباره تو را به یاد آورند.» 16
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
بله، پس از گذشت آن هفتاد سال، خداوند اجازه خواهد داد صور دوباره رونق یابد و با مشتریان خود در تمام دنیا تجارت کند. 17
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
اما سودی که عاید صور شود در خزانهٔ او ذخیره نخواهد شد، بلکه وقف خداوند خواهد گردید تا به مصرف خوراک و پوشاک پیروان راه خداوند برسد. 18
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

< اشعیا 23 >