< عِزرا 3 >

در ماه هفتم سال، تمام کسانی که به سرزمین یهودا بازگشته بودند از شهرهای خود آمده در اورشلیم جمع شدند. 1
Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
آنگاه یهوشع کاهن پسر یهوصادق و سایر کاهنان، و زروبابِل پسر شئلتیئیل و خاندان او مذبح خدای اسرائیل را دوباره بنا کردند. سپس همان‌طور که در کتاب تورات موسی، مرد خدا، دستور داده شده بود، قربانیهای سوختنی تقدیم نمودند. 2
Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
گرچه یهودیانی که به سرزمین خود بازگشته بودند از مردمی که در آن سرزمین بودند می‌ترسیدند، با این حال مذبح را در جای سابق خود بنا کردند و روی آن، قربانیهای سوختنی صبح و عصر را به خداوند تقدیم نمودند. 3
Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
آنها عید خیمه‌ها را همان‌طور که در کتاب تورات موسی نوشته شده بود، برگزار کردند و در طول روزهای عید، قربانیهایی را که برای هر روز تعیین شده بود، تقدیم نمودند. 4
Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
از آن پس، آنها به طور مرتب قربانیهای سوختنی روزانه، قربانیهای مخصوص جشن ماه نو و جشنهای سالیانهٔ خداوند را تقدیم می‌کردند. علاوه بر این قربانیها، هدایای داوطلبانه هم به خداوند تقدیم می‌شد. 5
Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
روز اول ماه هفتم، حتی قبل از گذاشتن پایه‌های خانهٔ خداوند، کاهنان شروع به تقدیم قربانیهای سوختنی برای خداوند کردند. 6
Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
سپس برای بازسازی خانهٔ خدا عده‌ای بنا و نجار استخدام کردند و به اهالی صور و صیدون مواد غذایی، شراب و روغن زیتون دادند و از آنها چوب سرو گرفتند. این چوبها از لبنان، از طریق دریا، به یافا حمل می‌شد. تمام اینها با اجازهٔ کوروش، پادشاه پارس، انجام می‌گرفت. 7
Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
در ماه دوم از سال دوم ورود یهودیان به اورشلیم، زروبابِل، یهوشع، کاهنان، لاویان و تمام کسانی که به سرزمین یهودا بازگشته بودند کار بازسازی خانهٔ خدا را شروع کردند. لاویانی که بیست سال یا بیشتر سن داشتند، تعیین شدند تا بر این کار نظارت کنند. 8
Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
نظارت بر کار کارگران به عهدۀ یشوع و پسران و برادرانش و قدمی‌ئیل و پسرانش (از نسل هودویا) گذاشته شد. (لاویان طایفۀ حیناداد نیز در این کار به ایشان کمک می‌کردند.) 9
Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
وقتی پایه‌های خانۀ خداوند گذاشته شد، کاهنان لباس مخصوص خود را پوشیدند و شیپورها را نواختند و لاویان طایفهٔ آساف سنجهای خود را به صدا درآوردند تا مطابق رسم داوود پادشاه، خداوند را ستایش کنند. 10
Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
ایشان با این کلمات در وصف خداوند می‌سراییدند: «خداوند نیکوست و محبتش برای اسرائیل بی‌پایان!» سپس برای پایه‌گذاری خانهٔ خداوند، تمام قوم با صدای بلند، خدا را شکر کردند. 11
Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
اما بسیاری از کاهنان و لاویان و سران قوم که پیر بودند و خانه‌ای را که سلیمان برای خداوند ساخته بود دیده بودند، وقتی پایه‌های خانهٔ خداوند را که گذاشته می‌شد دیدند، با صدای بلند گریستند، در حالی که دیگران از شادی فریاد برمی‌آوردند. 12
Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
کسی نمی‌توانست صدای گریه را از فریاد شادی تشخیص دهد، زیرا این صداها چنان بلند بود که از فاصلۀ دور نیز به گوش می‌رسید. 13
Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.

< عِزرا 3 >