< عِزرا 10 >

همان‌طور که عِزرا در مقابل خانهٔ خدا روی بر زمین نهاده بود و گریه‌کنان دعا و اعتراف می‌کرد، عدۀ زیادی از مردان و زنان و اطفال اسرائیلی نیز دورش جمع شدند و با او گریه کردند. 1
Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
سپس شکنیا پسر یحی‌ئیل که از طایفهٔ عیلام بود به عِزرا گفت: «ما اعتراف می‌کنیم که نسبت به خدای خود گناه ورزیده‌ایم، چون با زنان غیریهودی ازدواج کرده‌ایم. ولی با وجود این، باز امیدی برای بنی‌اسرائیل باقی است. 2
Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
اینک در حضور خدای خویش قول می‌دهیم که از زنان خود جدا شویم و آنها را با فرزندانشان از این سرزمین دور کنیم. ما در این مورد از دستور تو و آنانی که از خدا می‌ترسند پیروی می‌کنیم، و طبق شریعت عمل می‌نماییم. 3
Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
حال برخیز و به ما بگو چه کنیم. ما از تو پشتیبانی خواهیم کرد، پس ناامید نباش و آنچه لازم است انجام بده.» 4
Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
آنگاه عِزرا بلند شد و از سران کاهنان و لاویان و تمام بنی‌اسرائیل خواست تا قسم بخورند که هر چه شکنیا گفته است انجام دهند؛ و همه قسم خوردند. 5
Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
سپس عِزرا از برابر خانهٔ خدا برخاست و به اتاق یهوحانان (پسر الیاشیب) رفت و شب در آنجا ماند، ولی نه نان خورد و نه آب نوشید، چون به سبب گناه قوم ماتم گرفته بود. 6
Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
پس در سراسر یهودا و اورشلیم اعلام شد که تمام قوم باید در عرض سه روز در اورشلیم جمع شوند و اگر کسی از آمدن خودداری کند طبق تصمیم سران و بزرگان قوم اموال او ضبط خواهد گردید و خود او هم از میان قوم اسرائیل منقطع خواهد شد. 7
Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
8
Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
پس از سه روز که روز بیستم ماه نهم بود، تمام مردان یهودا و بنیامین در اورشلیم جمع شدند و در میدان جلوی خانهٔ خدا نشستند. آنها به سبب اهمیت موضوع و به خاطر باران شدیدی که می‌بارید، می‌لرزیدند. 9
Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
سپس عِزرای کاهن بلند شد و به ایشان چنین گفت: «شما مرتکب گناه شده‌اید، چون با زنان غیریهودی ازدواج کرده‌اید و با این کارتان به گناهان بنی‌اسرائیل افزوده‌اید. 10
Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
حال در حضور خداوند، خدای اجدادتان به گناهان خود اعتراف کنید و خواست او را به جا آورید. خود را از قومهایی که در اطراف شما هستند دور نگه دارید و از این زنان بیگانه جدا شوید.» 11
Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
همه با صدای بلند جواب دادند: «آنچه گفته‌ای انجام می‌دهیم. 12
Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
ولی این کار یکی دو روز نیست. چون عدهٔ کسانی که به چنین گناهی آلوده شده‌اند زیاد است. در ضمن باران هم به شدت می‌بارد و بیش از این نمی‌توانیم در اینجا بایستیم. 13
Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
بگذار سران ما در اورشلیم بمانند و به این کار رسیدگی کنند. سپس هر کس که زن غیریهودی دارد، در وقت تعیین شده با بزرگان و قضات شهر خود بیاید تا به وضعش رسیدگی شود و خشم خدای ما از ما برگردد.» 14
Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
کسی با این پیشنهاد مخالفت نکرد، جز یوناتان (پسر عسائیل) و یحزیا (پسر تقوه) که از پشتیبانی مشلام و شبتای لاوی برخوردار بودند. 15
Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
قوم این روش را پذیرفتند و عِزرای کاهن چند نفر از سران طایفه‌ها را انتخاب کرد و اسامی‌شان را نوشت. این گروه، روز اول ماه دهم تحقیق خود را شروع کردند، 16
Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
و در عرض سه ماه به وضع مردانی که همسران بیگانه داشتند رسیدگی نمودند. 17
Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
این است اسامی مردانی که زنان بیگانه داشتند: از کاهنان: از طایفۀ یهوشع پسر یهوصادق و برادرانش: معسیا، الیعزر، یاریب، جدلیا. 18
Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
این مردان قول دادند که از همسران بیگانهٔ خود جدا شوند و هر یک برای بخشیده شدن گناهش، یک قوچ برای قربانی تقدیم کرد. 19
Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
از طایفهٔ امیر: حنانی و زبدیا. 20
Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
از طایفۀ حاریم: معسیا، ایلیا، شمعیا، یحی‌ئیل، عزیا. 21
Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
از طایفۀ فشحور: الیوعینای، معسیا، اسماعیل، نتن‌ئیل، یوزاباد، العاسه. 22
Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
از لاویان: یوزاباد، شمعی، قلایا (معروف به قلیطا)، فتحیا، یهودا، الیعزر. 23
Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
از نوازندگان: الیاشیب. از نگهبانان خانۀ خدا: شلوم، طالم، اوری. 24
Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
از بقیۀ قوم: از طایفۀ فرعوش: رمیا، یزیا، ملکیا، میامین، العازار، ملکیا، بنایا. 25
Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
از طایفۀ عیلام: متنیا، زکریا، یحی‌ئیل، عبدی، یریموت، ایلیا. 26
A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
از طایفۀ زتو: الیوعینای، الیاشیب، متنیا، یریموت، زاباد، عزیزا. 27
A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
از طایفۀ ببای: یهوحانان، حَنَنیا، زبای، عتلای. 28
A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
از طایفهٔ بانی: مشلام، ملوک، عدایا، یاشوب، شآل، راموت. 29
A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
از طایفهٔ فحت موآب: عدنا، کلال، بنایا، معسیا، متنیا، بِصَلئیل، بنوی، منسی. 30
A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
از طایفهٔ حاریم: الیعزر، اشیاء، ملکیا، شمعیا، شمعون، بنیامین، ملوک، شمریا. 31
A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
32
Benjamini, Maluki ndi Semariya.
از طایفهٔ حاشوم: متنای، متاته، زاباد، الیفلط، یریمای، منسی، شمعی. 33
A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
از طایفۀ بانی: معدای، عمرام، اوئیل، بنایا، بیدیا، کلوهی، ونیا، مریموت، الیاشیب، متنیا، متنای، یعسو. 34
A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
35
Benaya, Bediya, Keluhi,
36
Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
37
Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
از طایفهٔ بنوی: شمعی، شلمیا، ناتان، عدایا، مکندبای، شاشای، شارای، عزرئیل، شلمیا، شمریا، شلوم، امریا، یوسف. 38
A fuko la Binuyi anali Simei,
39
Selemiya, Natani, Adaya,
40
Makinadebayi, Sasai, Sarai,
41
Azaleli, Selemiya, Semariya,
42
Salumu, Amariya ndi Yosefe.
از طایفۀ نبو: یعی‌ئیل، مَتّیتیا، زاباد، زبینا، یدو، یوئیل، بنایا. 43
A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
همهٔ این مردان، زنان بیگانه گرفته بودند و بعضی از ایشان از این زنان صاحب فرزندانی شده بودند. 44
Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.

< عِزرا 10 >