< حِزِقیال 13 >

خداوند با من سخن گفت و فرمود: «ای پسر انسان، کلام مرا بر ضد انبیای دروغین اسرائیل اعلام نما، بر ضد انبیایی که افکار خود را به عنوان پیغام من بیان می‌کنند.» 1
Yehova anayankhulanso nane kuti,
2
“Iwe mwana wa munthu unenere modzudzula aneneri a Israeli amene akunenera za kukhosi kwawo. Uwawuze iwowa kuti, ‘Imvani mawu a Yehova!’
خداوند یهوه فرمود: «وای بر انبیای نادانی که خیالات خود را به جای کلام من بازگو می‌کنند، حال آنکه هیچ کلامی از جانب من بر ایشان نازل نشده است. 3
Ambuye Yehova akuti, ‘Tsoka kwa aneneri opusa amene amangonenera zopeka ngakhale kuti sanaone kanthu konse!’
«ای مردم اسرائیل، انبیای شما مانند روباهانی در خرابه‌ها هستند. ایشان هیچ نفعی به شما نرسانده‌اند. 4
Iwe Israeli, aneneri ako ali ngati nkhandwe pa mabwinja.
آنان هیچگاه خرابیهای حصار شهر را تعمیر نکردند تا بتوانید در آن روزی که خداوند مقرر کرده، در برابر دشمن بایستید. 5
Simunakwere khoma kuti mukakonze mʼmene munagumuka, kuti Aisraeli adziteteze kolimba pa nkhondo pa tsiku la Yehova.
رؤیاهای ایشان باطل است و پیشگویی‌هایشان دروغ! می‌گویند که پیغامشان از جانب من است، در حالی که من ایشان را نفرستاده‌ام. با وجود این، انتظار دارند که پیشگویی‌هایشان عملی شوند! 6
Masomphenya awo ndi achabe ndipo kuwombeza kwawo ndi kwabodza. Iwo amati, ‘Yehova akutero,’ pomwe Yehova sanawatume. Komabe iwo amayembekezera kuti zimene ayankhulazo zichitikadi.
ای پیام‌آوران دروغین، رؤیاها و پیامهایتان، همه دروغ است! می‌گویید که آنها از طرف من می‌باشد، در حالی که من هیچگاه با شما سخن نگفته‌ام!» 7
Koma Ine ndikuti masomphenya anu ngachabechabe ndi zimene mwawombedzazo nʼzabodza. Mumanena kuti, ‘Akutero Yehova,’ pamene sindinayankhule nʼkomwe.
از این رو خداوند یهوه می‌فرماید: «به سبب این رؤیاهای ساختگی و این دروغها، من بر ضد شما هستم، 8
“Tsono Ine Ambuye Wamphamvuzonse ndikukutsutsani chifukwa cha zoyankhula zanu zonama ndi masomphenya anu abodzawo. Ndikutero Ine Yehova.
و شما را مجازات خواهم نمود و از میان رهبران اسرائیل ریشه‌کن خواهم ساخت. نام شما را از دفتر خاندان اسرائیل پاک خواهم نمود و هیچ‌یک از شما به سرزمین اسرائیل باز نخواهد گشت، تا بدانید که من خداوند یهوه هستم. 9
Ndidzalanga aneneri amene amanenera zabodza za zinthu zimene amati anaziona mʼmasomphenya. Sadzakhala nawo mʼbwalo la anthu anga ndipo mayina awo sadzalembedwa mu kawundula wa nzika za Israeli. Sadzalowa nawo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
«این مردان شریر، قوم مرا فریب داده، می‌گویند که همه چیز در امن و امان است، حال آنکه چنین نیست. قوم من دیواری سست می‌سازند و این پیام‌آوران دروغگو نیز تشویقشان می‌نمایند و با گچ، آن دیوار را سفید می‌کنند. 10
“Popeza kuti aneneri asocheretsa anthu anga pomanena kuti, ‘Kuli mtendere’ pamene mtendere palibe; ndiponso anthu akamanga khoma iwo nʼkumalipaka njereza,
پس به این معمارها بگو که دیوارشان فرو خواهد ریخت. بارانی سیل‌آسا خواهم بارانید، تگرگی سخت خواهم آورد و طوفانی شدید خواهم فرستاد تا آن را ویران سازند؛ 11
choncho ufotokozere amene alipaka njerezawo kuti khomalo lidzagwa. Mvula idzagwa mwamphamvu, kudzagwa matalala akuluakulu, ndipo kudzawomba mphepo yamkuntho.
و آن هنگام که دیوار فرو افتد، مردم بر سر ایشان فریاد خواهند زد: «چرا به ما نگفتید که دیوار سست و ناپایدار است؟ چرا روی آن را گچ گرفتید و معایبش را پوشانیدید؟» 12
Pamene khomalo lagwa, kodi anthu sadzakufunsani kuti, ‘Kodi njereza yemwe munapaka uja ali kuti?’
بله، با طوفان عظیم خشم، با تگرگ و باران غضب خود، آن را از جا کنده، نابودش خواهم نمود. 13
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Mwa ukali ndidzakunthitsa mphepo ya mkuntho. Ndidzagwetsa matalala akuluakulu ndili ndi ukali ndipo ndidzavumbwitsa mvula yamphamvu ndi mkwiyo mpaka khomalo litawonongeka kotheratu.
دیوار گچکاری شدهٔ ایشان خراب و با خاک یکسان خواهد شد و بر سرشان فرو خواهد ریخت و در زیر آن له خواهند شد، تا بدانند که من خداوند یهوه هستم. 14
Ndidzagwetsa khoma limene munalipaka njerezalo. Ndidzaligumuliratu mpaka pansi kotero kuti maziko ake adzaoneka. Khomalo likadzagwa, inu mudzawonongekamo; ndipo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
زمانی که خشم من بر ضد این دیوار و معمارانش پایان یابد، اعلام خواهم کرد که نه دیواری مانده و نه معماری؛ 15
Kotero ndidzagwiritsa ntchito mkwiyo wanga pa khomali ndi pa amene analipaka njereza. Pambuyo pake ndidzakuwuzani kuti, ‘Khoma lagwa pamodzi ndi amene analipaka njereza.
زیرا معمارانش، انبیای دروغگویی بودند که می‌گفتند اورشلیم در امان خواهد بود، در حالی که چنین نبود. 16
Agwanso aneneri a Yerusalemu amene ankalosa za Yerusalemu nʼkumati anaona mʼmasomphenya za mtendere wa Yerusalemu pamene mtendere kunalibe konse, akutero Ambuye Wamphamvuzonse.’
«حال ای پسر انسان، کلام مرا بر ضد زنانی که افکار خود را به جای پیام من بیان می‌کنند، اعلام نما.» 17
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhulapo pa nkhani za akazi amene ali pakati pa anthu ako. Iwo amanenera zopeka za mʼmutu mwawo. Tsono adzudzule.
خداوند یهوه فرمود که به ایشان چنین بگویم: «وای بر شما که قوم مرا گمراه می‌کنید. به بازوهایشان طلسم و جادو می‌بندید و دستار افسون به آنها می‌فروشید تا بتوانند اختیار زندگی دیگران را به دست بگیرند. آیا می‌خواهید اختیار مرگ و زندگی قوم مرا در دست داشته باشید تا جیبتان را پر کنید؟ 18
Uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Tsoka kwa akazi amene amasoka zithumwa zapamkono, amenenso amasoka nsalu za kumutu za anthu. Kodi mufuna kukola mitima ya anthu anga, inuyo nʼkupulumutsa moyo wanu?
برای مشتی جو و چند لقمه نان، قومم را از من دور می‌سازید. کسانی را که باید زنده بمانند، به کشتن می‌دهید و آنانی را که نباید زنده بمانند، زنده نگه می‌دارید. به این ترتیب به قوم من دروغ می‌گویید و آنها نیز باور می‌کنند. 19
Ponamiza anthu anga amene amamva za mabodza anu, inu mwapha anthu amene sanayenera kufa ndipo mwasiya ndi moyo amene sanayenera kukhala ndi moyo.
«از این رو من بر ضد سحر و جادوی شما هستم که با آنها زندگی افراد قوم مرا طلسم کرده‌اید و مانند پرنده‌ای به دام انداخته‌اید. طلسمهای شما را باطل کرده، دعاهایتان را بی‌اثر خواهم ساخت و قوم خود را از دام شما رهایی خواهم بخشید. 20
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikudana ndi zithumwa zanu zimene mumakokera nazo mitima ya anthu ngati mbalame. Ndidzazingʼamba kudzichotsa pa mikono yanu. Choncho ndidzapulumutsa miyoyo ya anthu amene munawakola ngati mbalame.
دستارهای افسون را خواهم درید و قومم را از چنگ شما نجات خواهم بخشید. ایشان دیگر در دام شما نخواهند بود تا بدانید که من یهوه هستم. 21
Ndidzangʼamba nsalu zanu za matsengazo ndi kupulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu, ndipo simudzakhalanso ndi mphamvu yowakolera. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
شما با دروغهای خود، مردم درستکار را برخلاف میل من، دل شکسته و دردمند ساخته‌اید، ولی افراد شرور را تشویق کرده‌اید و باعث شده‌اید آنها از راههای گناه‌آلودشان توبه نکنند و رستگار نشوند. 22
Popeza kuti munatayitsa mtima anthu olungama ngakhale sindinafune kuti ataye mtima; ndipo munalimbitsa anthu oyipa kuti asaleka machimo awo motero sakutha kupulumutsa moyo wawo,
اما از این پس، دیگر رؤیاهای باطل نخواهید دید و غیبگویی‌های گمراه کننده نخواهید کرد، زیرا من قوم خود را از نفوذ قدرت شما رهایی خواهم داد تا بدانید که من یهوه هستم!» 23
choncho inu simudzaonanso masomphenya abodza kapena kuwombeza. Ine ndidzapulumutsa anthu anga mʼmanja mwanu. Ndipo pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< حِزِقیال 13 >