< خروج 38 >

مذبح قربانی سوختنی نیز با چوب اقاقیا به شکل چهارگوش ساخته شد. هر ضلع آن دو و نیم متر و بلندیش یک و نیم متر بود. 1
Anapanga guwa lansembe zopsereza lamatabwa amtengo wa mkesha. Linali lofanana mbali zonse. Msinkhu wake masentimita 137, mulitali mwake masentimita 229, mulifupi masentimita 229.
آن را طوری ساخت که در چهار گوشه‌اش چهار برجستگی به شکل شاخ بود. تمام مذبح و شاخها روکشی از مفرغ داشت. 2
Anapanga nyanga imodziimodzi pa ngodya zake zinayizo, kotero kuti nyangazo ndi guwalo zinali chinthu chimodzi, ndipo anakuta guwalo ndi mkuwa.
لوازم آن که شامل سطلها، خاک‌اندازها، کاسه‌ها، چنگکها و آتشدانها بود، همگی از مفرغ ساخته شد. 3
Anapanganso ziwiya zamkuwa izi zogwirira ntchito pa guwalo: miphika, mafosholo, mabeseni owazira magazi, ngowe zokowera nyama ndi zosonkhezera moto.
سپس یک منقل مشبک مفرغین برای مذبح ساخت و آن را تا نیمهٔ مذبح فرو برد تا روی لبه‌ای که در آنجا وجود داشت قرار گیرد. 4
Anapanga sefa yachitsulo chamkuwa ya guwa lansembelo kuti ikhale mmunsi mwa khoma la guwa lansembelo, kuchokera pansi mpaka pakati pa khoma la guwalo.
چهار حلقه برای چهار گوشۀ شبکۀ مفرغین ریخت تا چوبها را نگاه دارند. 5
Anapanga mphete zamkuwa zinayi ndipo anazilumikiza ku ngodya zinayi za sefa ija kuti zigwire nsichi zonyamulira.
چوبهایی از درخت اقاقیا با روکش مفرغ ساخت. 6
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndipo anazikuta ndi mkuwa.
چوبها را در حلقه‌هایی که در دو طرف مذبح نصب شده بود، فرو کرد. مذبح، درونش خالی بود و از تخته ساخته شده بود. 7
Iwo analowetsa nsichizo mʼmphetemo mbali zonse ziwiri za guwalo kuti azinyamulira. Guwalo linali lamatabwa ndi logoba mʼkati mwake.
حوض مفرغین و پایهٔ مفرغین‌اش را از آیینه‌های زنانی که در کنار در خیمۀ ملاقات خدمت می‌کردند، ساخت. 8
Anapanga beseni lamkuwa lokhala ndi miyendo yamkuwanso kuchokera ku magalasi oyangʼanira nkhope a amayi amene ankatumikira pa chipata cha tenti ya msonkhano.
سپس بِصَلئیل برای خیمۀ عبادت حیاطی درست کرد که دیوارهایش از پرده‌های کتان ریزبافت تابیده بود. طول پرده‌های سمت جنوب پنجاه متر بود. 9
Kenaka anapanga bwalo la chihema. Mbali yakummwera inali yotalika mamita 46 ndipo kunali nsalu yotchinga yofewa yosalala yolukidwa bwino.
بیست ستون مفرغین برای پرده‌ها ساخت و برای این ستونها پایه‌های مفرغین و قلابها و پشت‌بندهای نقره‌ای درست کرد. 10
Anapanganso mizati makumi awiri, matsinde makumi awiri amkuwa ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
برای سمت شمالی حیاط نیز همین کار را کرد. 11
Mbali yakumpoto inalinso yotalika mamita 46 ndipo inali ndi mizati makumi awiri, matsinde amkuwa makumi awiri, ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
طول دیوار پرده‌ای سمت غربی بیست و پنج متر بود. ده ستون با ده پایه برای پرده‌ها ساخت و برای هر یک از این ستونها قلابها و پشت‌بندهای نقره‌ای درست کرد. 12
Mbali yakumadzulo inali yotalika mamita 23 ndipo inali ndi nsalu yotchinga, mizati khumi ndi matsinde khumi. Inalinso ndi ngowe zasiliva ndi zingwe za mizatiyo.
طول دیوار پرده‌ای سمت شرقی هم بیست و پنج متر بود. 13
Mbali yakummawa, kotulukira dzuwa, inalinso yotalika mamita 23.
مدخل خیمۀ عبادت در انتهای جنوبی قرار داشت و از دو پرده تشکیل شده بود. پردۀ سمت راست هفت و نیم متر بود و بر سه ستون با سه پایه آویزان بود. 14
Mbali imodzi yachipata kunali nsalu yotchinga yotalika mamita asanu ndi awiri, mizati itatu ndi matsinde atatu,
پردۀ سمت چپ نیز هفت و نیم متر بود و بر سه ستون با سه پایه آویزان بود. 15
polowera mʼbwalo panali nsalu yotchinga ya mamita asanu ndi awiri pamodzi ndi mizati itatu ndi matsinde atatu.
تمام پرده‌های دیوار حیاط خیمه از کتان ریز‌بافت تابیده بود. 16
Katani yonse yotchinga kuzungulira chihema inali yofewa, yosalala ndi yolukidwa bwino.
پایه‌های ستونها از مفرغ، و قلابها و پشت‌بندها و روکش سر ستونها از نقره بود. تمام ستونهای اطراف حیاط با پشت‌بندهای نقره‌ای به هم مربوط شدند. 17
Matsinde amizati anali amkuwa. Ngowe ndi zingwe za mizati zinali zasiliva, ndipo pamwamba pa mizatiyo anakutapo siliva. Choncho mizati yonse ya bwalolo inalumikizidwa ndi zingwe zasiliva.
پردهٔ مدخل خیمه از کتان ریزبافت تابیده تهیه گردید و با نخهای آبی، ارغوانی و قرمز گلدوزی شد. طول این پرده ده متر و بلندیش مانند پرده‌های دیوار حیاط، دو و نیم متر بود. 18
Nsalu yotchinga ya pa chipata inali yamtundu wa mtambo, yapepo ndi yofiira, yofewa yosalala ndi yopangidwa ndi anthu aluso. Nsaluyo inali yotalika mamita asanu ndi anayi, molingana ndi nsalu zotchinga bwalo. Msinkhu wake unali masentimita 229,
چهار ستون برای پرده ساخت. پایه‌های ستونها از مفرغ، و قلابها و پشت‌بندها و روکش سر ستونها از نقره بود. 19
pamodzi ndi mizati yake inayi ndi matsinde amkuwa anayi. Ngowe ndi zingwe zake zinali za siliva, ndipo pamwamba pake pa mzati anakutapo ndi siliva.
تمام میخهایی که در بنای خیمه و حیاط آن به کار رفت، از مفرغ بود. 20
Zikhomo za chihema ndi zina zonse zozungulira chihemacho zinali zamkuwa.
این است صورت مقدار فلزی که در ساختن خیمهٔ عبادت به کار رفت. این صورت به دستور موسی، به‌وسیلۀ لاویان و زیر نظر ایتامار پسر هارون کاهن تهیه شد. 21
Chiwerengero cha zipangizo zimene anagwiritsa ntchito popanga chihema, chihema chaumboni, zimene Mose analamulira Alevi kuti alembe motsogozedwa ndi Itamara mwana wa Aaroni, wansembe, chinali ichi:
(بِصَلئیل پسر اوری و نوهٔ حور از قبیلهٔ یهودا، آنچه را که خداوند به موسی دستور داده بود، ساخت. 22
Bezaleli mwana wa Uri, mwana wa Huzi wa fuko la Yuda anapanga chilichonse Yehova analamulira Mose,
دستیار او در این کار اهولیاب پسر اخیسامک از قبیلهٔ دان بود که در کار طراحی، نساجی و طرازی پارچه‌های آبی، ارغوانی، قرمز و کتان ریزبافت مهارت داشت.) 23
pamodzi ndi Oholiabu mwana wa Ahisamaki, wa fuko la Dani, wa luso la zopangapanga ndi kulemba mapulani, ndi wopanga nsalu zolukidwa bwino za mtundu wa mtambo, yapepo ndi zofiira, zofewa ndi zosalala.
بنی‌اسرائیل جمعاً حدود هزار کیلوگرم طلا به مقیاس مثقال عبادتگاه هدیه کردند که تمام آن صرف ساختن خیمۀ عبادت شد. 24
Golide yense wochokera ku nsembe yoweyula amene anagwiritsa ntchito pa ntchito yonse yopanga malo wopatulika anali wolemera makilogalamu 1,000 potsata miyeso ya kumalo wopatulika.
جماعت اسرائیل جمعاً سه هزار و چهارصد و سی کیلوگرم نقره که به مقیاس عبادتگاه وزن می‌شد، هدیه دادند. 25
Siliva wochokera ku gulu lonse la anthu anali wolemerera makilogalamu 3,430, potsata miyeso ya ku malo wopatulika.
این مقدار نقره از همۀ کسانی که اسمشان در سرشماری نوشته شده بود، به عنوان مالیات دریافت گردید. (مالیات هر فرد یک بِکا بود که بر اساس مقیاس عبادتگاه، معادل ۶ گرم است). این مالیات از ۶۰۳٬۵۵۰ نفر که سنشان بیست سال به بالا بود، دریافت شده بود. 26
Munthu aliyense amapereka beka imodzi, kufanana ngati makilogalamu 6, potsata muyeso wa ku malo wopatulika. Kuchokera kwa aliyense amene anawerengedwa kuyambira zaka 20 kapena kuposerapo, amuna onse analipo 603,550.
برای پایه‌های چوب‌بست خیمهٔ عبادت و پایه‌های ستونهای پردهٔ داخل آن، سه هزار و چهارصد کیلوگرم نقره مصرف شد، یعنی برای هر پایه سی و چهار کیلوگرم. 27
Anagwiritsa ntchito siliva wolemera makilogalamu 3,400 kupanga matsinde 100 a ku malo wopatulika ndi makatani, ndipo makilogalamu 34 kupanga tsinde limodzi.
باقیماندهٔ نقره که سی کیلوگرم بود برای قلابهای ستونها، پشت‌بندها و روکش سر ستونها مصرف شد. 28
Makilogalamu otsalawo anagwiritsa ntchito popanga ngowe zamzati kukutira pamwamba pa mizati ndiponso kupanga zingwe zake.
بنی‌اسرائیل همچنین هدیۀ مخصوصی که دو هزار و چهارصد و بیست و پنج کیلوگرم مفرغ بود، آوردند. 29
Mkuwa ochokera ku nsembe yoweyula unali makilogalamu 2,425.
این مقدار مفرغ برای پایه‌های ستونهای مدخل خیمۀ ملاقات، مذبح مفرغین، منقل مشبک و سایر لوازم مذبح، همچنین برای پایه‌های ستونهای دور حیاط و پایه‌های مدخل آن، و نیز برای میخهای خیمه و پرده‌های دور حیاط به کار رفت. 30
Iwo anawugwiritsa ntchito popanga matsinde a pa chipata cha tenti ya msonkhano, guwa la mkuwa pamodzi ndi sefa yake ndiponso ziwiya zonse,
31
matsinde ozungulira bwalo ndiponso a pa chipata pake, ndi zikhomo zonse za tentiyo ndi matsinde a malo wozungulirapo.

< خروج 38 >