< استر 1 >

خشایارشا، پادشاه پارس، بر سرزمین پهناوری سلطنت می‌کرد که از هند تا حبشه را در بر می‌گرفت و شامل ۱۲۷ استان بود. او در سال سوم سلطنت خود، در کاخ سلطنتی شوش جشن بزرگی بر پا نمود و تمام بزرگان و مقامات مملکتی را دعوت کرد. فرماندهان لشکر پارس و ماد همراه با امیران و استانداران در این جشن حضور داشتند. 1
Izi ndi zimene zinachitika pa nthawi ya ufumu wa Ahasiwero, amene analamulira zigawo 127 kuyambira ku India mpaka ku Kusi.
2
Pa nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Ahasiwero atakhazikika pa mpando wake wa ufumu mu mzinda wa Susa,
3
ndipo mʼchaka chachitatu cha ufumu wake anakonza phwando la olemekezeka ndi nduna zake. Atsogoleri a nkhondo a ku Peresiya ndi Mediya, anthu olemekezeka pamodzi ndi nduna za mʼzigawo zonse anasonkhana kwa iye.
در طی این جشن که شش ماه طول کشید، خشایارشا تمام ثروت و شکوه و عظمت سلطنت خود را به نمایش گذاشت. 4
Pa nthawi yomweyi kwa masiku 180 a phwando mfumu inkaonetsa kulemera kwa ulemerero wa ufumu wake ndiponso kukongola ndi kukula kwa ufumu wake.
پس از پایان جشن، خشایارشا برای تمام کسانی که در شوش زندگی می‌کردند، فقیر و غنی، میهمانی هفت روزه‌ای در باغ کاخ سلطنتی ترتیب داد. 5
Atatha masiku amenewa, kwa masiku ena asanu ndi awiri mfumu inakonzanso phwando la anthu onse okhala mu mzinda wa Susa kuyambira anthu olemekezeka mpaka anthu wamba ku bwalo la munda la nyumba yake yaufumu.
محل میهمانی با پرده‌هایی از کتان سفید و آبی تزیین شده بود. این پرده‌ها با ریسمانهای سفید و ارغوانی که داخل حلقه‌های نقره‌ای قرار داشتند از ستونهای مرمر آویزان بود. تختهای طلا و نقره روی سنگفرشهایی از سنگ سماک، مرمر، صدف مروارید و فیروزه قرار داشت. 6
Bwalo la mundali analikongoletsa ndi makatani a nsalu zoyera ndi za mtundu wamtambo zimene anazimangirira ndi zingwe za nsalu zoyera ndi zapepo ku mphete za siliva zimene anazikoloweka pa nsanamira za maburo. Anayika mipando yopumirapo yagolide ndi siliva pabwalo la miyala yoyala yamtengowapatali yofiira, ya marabulo, ndi yonyezimira.
از سخاوت پادشاه، شراب شاهانه فراوان بود و در جامهای طلایی که شکلهای گوناگون داشت، صرف می‌شد. 7
Anapereka zakumwa mʼchikho zagolide zamitundumitundu, ndipo vinyo waufumu anali wochuluka kwambiri monga mwa kukoma mtima kwa mfumu.
پادشاه به پیشخدمتهای دربار دستور داده بود میهمانان را در نوشیدن آزاد بگذارند، پس ایشان به دلخواه خود، هر قدر که می‌خواستند شراب می‌نوشیدند. 8
Monga mwa lamulo la mfumu aliyense anamwa mʼmene anafunira, pakuti mfumu inawuza otumikira ake kuti apatse aliyense monga mwa kukonda kwake.
در همان هنگام، ملکه وشتی هم برای زنان دربار خشایارشا ضیافتی ترتیب داده بود. 9
Mkazi wa mfumu Vasiti nayenso anakonzera phwando amayi ku nyumba ya ufumu ya mfumu Ahasiwero.
در آخرین روز میهمانی، پادشاه که از باده‌نوشی سرمست شده بود، هفت خواجهٔ حرمسرا یعنی مهومان، بزتا، حربونا، بغتا، ابغتا، زاتر و کرکس را که خادمان مخصوص او بودند احضار کرد. 10
Pa tsiku la chisanu ndi chiwiri, pamene mfumu Ahasiwero inaledzera ndi vinyo, inalamula adindo ofulidwa asanu ndi awiri amene ankamutumikira: Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, Abagita, Zetara, ndi Karikasi
او به آنان دستور داد ملکه وشتی را که بسیار زیبا بود با تاج ملوکانه به حضورش بیاورند تا زیبایی او را به مقامات و مهمانانش نشان دهد. 11
kuti abwere naye mfumukazi Vasiti pamaso pa mfumu atavala chipewa chaufumu. Cholinga cha mfumu chinali choti adzamuonetse kwa anthu onse ndi olemekezeka, chifukwa anali wokongola kwambiri.
اما وقتی خواجه‌سرایان فرمان پادشاه را به ملکه وشتی رساندند، او از آمدن سرباز زد. پادشاه از این موضوع بسیار خشمناک شد؛ 12
Koma antchito atapereka uthenga wa mfumu kwa mfumukazi, Vasiti anakana kubwera. Tsono mfumu inakwiya ndi kupsa mtima.
اما پیش از آنکه اقدامی کند، اول از مشاوران خود نظر خواست، چون بدون مشورت با آنها کاری انجام نمی‌داد. مشاوران او مردانی دانا و آشنا به قوانین و نظام دادگستری پارس بودند و پادشاه به قضاوت آنها اعتماد داشت. نام این دانشمندان کرشنا، شیتار، ادماتا، ترشیش، مرس، مرسنا و مموکان بود. این هفت نفر جزو مقامات عالی رتبهٔ پارس و ماد و از امیران ارشد مملکتی بودند. 13
Mfumu inayankhula ndi anthu anzeru ndi ozindikira choyenera kuchita popeza chinali chikhalidwe chake kufunsa uphungu kwa akatswiri pa nkhani za malamulo ndi kuweruza kolungama.
14
Anthu amene ankakhala pafupi ndi mfumu anali awa: Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena ndi Memukani, olemekezeka asanu ndi awiri a ku Peresiya ndi Medina amene ankaloledwa mwapadera kuonana ndi mfumu ndipo anali pamwamba kwambiri mu ufumuwo.
خشایارشا از ایشان پرسید: «در مورد ملکه وشتی چه باید کرد؟ زیرا از فرمان پادشاه که به او ابلاغ شده، سر باز زده است. قانون چه مجازاتی برای چنین شخصی تعیین کرده است؟» 15
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi titani naye mfumukazi Vasiti mwa lamulo, popeza sanamvere lamulo la ine mfumu Ahasiwero limene adindo ofulidwa anakamuwuza?”
مموکان خطاب به پادشاه و امیران دربار گفت: «ملکه وشتی نه فقط به پادشاه بلکه به امیران دربار و تمام مردم مملکت خشایارشای پادشاه اهانت کرده است. 16
Ndipo Memukani anayankha pa maso pa mfumu ndi olemekezeka anzake kuti, “Mfumukazi Vasiti sanalakwire mfumu yokha, koma walakwiranso olemekezeka onse ndi anthu onse okhala mʼzigawo zonse za mfumu Ahasiwero.
هر زنی که بشنود که ملکه وشتی از آمدن به حضور پادشاه سرپیچی کرده است، او نیز از دستور شوهرش سرپیچی خواهد کرد. 17
Pakuti amayi onse adzadziwa zimene wachita mfumukazi ndipo kotero adzapeputsa amuna awo ndi kunena kuti, ‘Mfumu Ahasiwero analamulira kuti abwere naye mfumukazi Vasiti kwa iye koma sanapite.’
وقتی زنانِ امیرانِ دربارِ پارس و ماد بشنوند که ملکه چه کرده، آنان نیز با شوهرانشان چنین خواهند کرد و این بی‌احترامی و سرکشی به همه جا گسترش خواهد یافت. 18
Lero lomwe lino amayi olemekezeka a ku Peresiya ndi Mediya amene amva zimene wachita mfumukazi adzaganiza zochita chimodzimodzi kwa nduna zonse za mfumu. Ndipo kupeputsana ndi kukongola zidzapitirira.”
بنابراین، اگر پادشاه صلاح بدانند، فرمانی صادر کنند تا در قوانین ماد و پارس که هرگز تغییر نمی‌کند ثبت گردد و بر طبق آن فرمان، ملکه وشتی دیگر به حضور پادشاه شرفیاب نشود. آنگاه زن دیگری که بهتر از او باشد به جای وی به عنوان ملکه انتخاب شود. 19
“Choncho, ngati chikukomerani mfumu, lamulirani kuti Vasiti asadzaonekerenso pamaso pa mfumu Ahasiwero. Lamuloli lilembedwe mʼmabuku a malamulo a Aperezi ndi Amedi kuti lisadzasinthike. Pamalo pa Vasiti ngati mfumukazi payikidwepo mkazi wina amene ali bwino kuposa iye.
وقتی این فرمان در سراسر این سرزمین پهناور اعلام شود آنگاه در همه جا شوهران، هر مقامی که داشته باشند، مورد احترام زنانشان قرار خواهند گرفت.» 20
Ndipo lamulo la mfumuli lilengezedwa mʼdziko lake lonse ngakhale lili lalikulu, amayi onse adzapereka ulemu kwa amuna awo, amuna olemekezeka mpaka amuna wamba.”
پیشنهاد مموکان مورد پسند پادشاه و امیران دربار واقع شد و خشایارشا مطابق صلاحدید او عمل کرد 21
Mfumu ndi nduna zake anakondwera ndi uphungu uwu, kotero mfumu inachita monga momwe ananenera Memukani.
و به تمام استانها، هر یک به خط و زبان محلی، نامه فرستاده، اعلام داشت که هر مرد باید رئیس خانهٔ خود باشد. 22
Mfumu inatumiza makalata ku madera onse a ufumu wake, chigawo chilichonse mʼzilembo zawo ndi ku mtundu uliwonse mʼchiyankhulo chawochawo kulengeza kuti mwamuna ayankhule chilichonse chimene chikumukomera.

< استر 1 >