< جامعه 12 >

نگذار هیجان جوانی سبب شود آفرینندهٔ خود را فراموش کنی. او را در روزهای جوانی‌ات به یاد آور، قبل از اینکه روزهای سخت زندگی فرا رسد و تو پیر شده، بگویی: «زندگی دیگر لذت ندارد.» 1
Uzikumbukira mlengi wako masiku a unyamata wako, masiku oyipa asanafike, nthawi isanafike pamene udzanena kuti, “Izi sizikundikondweretsa.”
‏او را به یاد آور قبل از اینکه ابرهای تیره آسمان زندگی تو را فرا گیرند، و دیگر خورشید و ماه و ستارگان در آن ندرخشند. 2
Nthawi ya ukalamba wako, dzuwa ndi kuwala, mwezi ndi nyenyezi zidzada. Mitambo idzabweranso mvula itagwa.
او را به یاد آور قبل از اینکه پاهای تو که همچون محافظانِ خانه از بدنت نگهداری می‌کنند، بلرزند، و شانه‌هایت که مانند پهلوانان حمایتت می‌کند خم شوند. او را به یاد آور قبل از اینکه دندانهایت که خوراک را در دهانت آسیاب می‌کنند، کم شوند و دیگر نتوانند بجوند، و چشمانت که مانند کسانی هستند که از پنجره‌ها می‌نگرند، کم سو گردند و نتوانند چیزی را ببینند. 3
Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.
او را به یاد آور، قبل از اینکه گوشهایت، همچون درها، بسته شوند و نتوانند سر و صدای کوچه و صدای آسیاب و نغمهٔ موسیقی و آواز پرندگان را بشنوند. 4
Makutu ako adzatsekeka, ndipo sudzamva phokoso lakunja; sudzamvanso kusinja kwa pa mtondo kapena kulira kwa mbalame mmawa.
او را به یاد آور قبل از اینکه از هر بلندی بترسی؛ و از خطر راهها هراسان شوی؛ قبل از اینکه موهایت مانند شکوفۀ درخت بادام سفید شوند، و تو مانند ملخ بی‌جان خود را به سختی روی زمین بکشی، و آتش هیجان جوانی‌ات رو به خاموشی رود. او را به یاد آور قبل از اینکه به خانهٔ جاودانی بروی و مردم برای سوگواری تو جمع شوند. 5
Imeneyi ndiyo nthawi imene anthu amaopa kupita kumalo okwera, amaopa kuyenda mʼmisewu; Mutu umatuwa kuti mbuu, amayenda modzikoka ngati ziwala ndipo chilakolako chimatheratu. Nthawi imeneyo munthu amapita ku nyumba yake yamuyaya ndipo anthu olira maliro amayendayenda mʼmisewu.
بله، آفرینندهٔ خویش را به یاد آور، قبل از آنکه رشتهٔ نقره‌ای عمرت پاره شود و جام طلا بشکند، کوزه کنار چشمه خرد شود و چرخ بر سر چاه آب متلاشی گردد، 6
Kumbukira Iye chingwe cha siliva chisanaduke, kapena mbale yagolide isanasweke; mtsuko usanasweke ku kasupe, kapena mkombero usanathyoke ku chitsime.
بدن به خاک زمین که از آن سرشته شده برگردد و روح به سوی خداوند که آن را عطا کرده، پرواز کند. 7
Iyi ndi nthawi imene thupi lidzabwerera ku dothi, kumene linachokera, mzimu udzabwerera kwa Mulungu amene anawupereka.
«معلم» می‌گوید: «بیهودگی است! بیهودگی است! همه چیز بیهودگی است!» 8
“Zopanda phindu! Zopandapake!” akutero Mlaliki. “Zonse ndi zopandapake!”
«معلم» آنچه را که می‌دانست به مردم تعلیم می‌داد، زیرا مرد دانایی بود. او پس از تفکر و تحقیق، مثلهای بسیاری تألیف کرد. 9
Mlaliki sanali wozindikira zinthu kokha ayi, komanso ankaphunzitsa anthu. Iye ankasinkhasinkha ndi kufufuzafufuza ndi kulemba mwadongosolo miyambi yambiri.
«معلم» کوشش کرد با سخنان دلنشین، حقایق را صادقانه بیان کند. 10
Mlaliki anafufuzafufuza kuti apeze mawu oyenera, ndipo zimene analemba zinali zolondola ndiponso zoona.
گفتار حکیمان مانند سُکهای گاورانی دردآور اما مفید هستند. گنجینۀ سخنانشان همچون چوبی هستند که میخ بر سرش دارد و شبان با آن گوسفندان را می‌راند. 11
Mawu a anthu anzeru ali ngati zisonga, zokamba zawo zimene anasonkhanitsa zili ngati misomali yokhomera, yoperekedwa ndi mʼbusa mmodzi.
ولی پسرم، از همهٔ اینها گذشته، بدان که نوشتن کتب تمامی ندارد و مطالعهٔ آنها بدن را خسته می‌کند. 12
Samalira mwana wanga, za kuwonjezera chilichonse pa zimenezi. Kulemba mabuku ambiri sikutha, ndipo kuphunzira kwambiri kumatopetsa thupi.
در خاتمه، حاصل کلام را بشنویم: انسان باید از خداوند بترسد و احکام او را نگاه دارد، زیرا تمام وظیفهٔ او همین است. 13
Basi zonse zamveka; mathero a nkhaniyi ndi awa: uziopa Mulungu ndi kusunga malamulo ake, pakuti umenewu ndiwo udindo wa anthu onse.
خدا هر عمل خوب یا بد ما را، حتی اگر در خفا نیز انجام شود، داوری خواهد کرد. 14
Pakuti Mulungu adzaweruza zochita zonse, kuphatikizanso zinthu zonse zobisika, kaya zabwino kapena zoyipa.

< جامعه 12 >