< جامعه 11 >
از مال خود با سخاوتمندی به دیگران ببخش، چون بخشش تو بدون عوض نمیماند. | 1 |
Ponya chakudya chako pa madzi, udzachipezanso patapita masiku ambiri.
مالی را که میخواهی ببخشی به چندین نفر ببخش، زیرا نمیدانی چه پیش خواهد آمد. | 2 |
Ndalama zako uzisungitse kwa anthu asanu ndi awiri, inde kwa anthu asanu ndi atatu, pakuti sudziwa ndi tsoka lanji limene likubwera pa dziko.
درخت به هر طرف که سقوط کند در همان جا نیز روی زمین خواهد افتاد. وقتی ابر از آب پر شود، بر زمین خواهد بارید. | 3 |
Ngati mitambo yadzaza ndi madzi, imagwetsa mvula pa dziko lapansi. Mtengo ukagwera cha kummwera kapena cha kumpoto, ndiye kuti udzagonera kumene wagwerako.
کشاورزی که برای کار کردن منتظر هوای مساعد بماند، نه چیزی خواهد کاشت و نه چیزی درو خواهد کرد. | 4 |
Amene amayangʼana mphepo sadzadzala; amene amayangʼana mitambo sadzakolola.
همانطور که نمیدانی باد چگونه میوزد و یا بدن کودک چگونه در رحم مادرش شکل میگیرد، همچنین نمیتوانی کارهای خدا را که خالق همه چیز است درک کنی. | 5 |
Momwe sudziwira mayendedwe a mphepo, kapena momwe mzimu umalowera mʼthupi la mwana mʼmimba mwa amayi, momwemonso sungathe kudziwa ntchito za Mulungu, Mlengi wa zinthu zonse.
تو روز و شب بذر خود را بکار، چون نمیدانی کدام قسمت از بذرها ثمر خواهد داد؛ شاید هر چه کاشتهای ثمر بدهد. | 6 |
Dzala mbewu zako mmawa ndipo madzulo usamangoti manja lobodo, pakuti sudziwa chimene chidzapindula, mwina ichi kapena icho, kapena mwina zonse ziwiri zidzachita bwino.
نور، شیرین است؛ چه لذتبخش است دیدن طلوع آفتاب! | 7 |
Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.
انسان تا میتواند باید از سالهای عمرش لذت ببرد و نیز بداند که سرانجام خواهد مرد و روزهای بسیاری در تاریکی و بیهودگی به سر خواهد برد. | 8 |
Munthu akakhala wa zaka zambiri, mulekeni akondwerere zaka zonsezo, koma iye azikumbukira masiku a mdima, pakuti adzakhala ochuluka. Chilichonse chimene chikubwera ndi chopanda phindu.
ای جوان، روزهای جوانیت را با شادی بگذران و از آن لذت ببر و هر چه دلت میخواهد انجام بده، ولی به یاد داشته باش که برای هر کاری که انجام میدهی باید به خدا پاسخ دهی. | 9 |
Kondwera mnyamata iwe, pamene ukanali wamngʼono, ndipo mtima wako usangalale pa nthawi ya unyamata wako. Tsatira zimene mtima wako ukufuna, ndiponso zimene maso ako akuona, koma dziwa kuti pa zinthu zonsezo Mulungu adzakuweruza.
روزهای جوانی زود میگذرد، پس نگذار جوانیت با غم و سختی سپری شود. | 10 |
Choncho uchotse zokusautsa mu mtima mwako, upewe zokupweteka mʼthupi mwako, pakuti unyamata ndi ubwana ndi zopandapake.