< عاموس 7 >
در رؤیایی که خداوند به من نشان داد دیدم برداشت محصول اول غله که سهم پادشاه بود تمام شده و محصول دوم، تازه سبز شده بود. سپس دیدم خداوند انبوهی ملخ فرستاد. | 1 |
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
ملخها هر چه سر راهشان بود، خوردند. آنگاه من گفتم: «ای خداوند، التماس میکنم قوم خود را ببخش و این آفت را از آنها دور کن، زیرا اسرائیل کوچک و ضعیف است و نمیتواند طاقت بیاورد.» | 2 |
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
خداوند نیز ترحم فرمود و گفت: «این بلا را نمیفرستم.» | 3 |
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
آنگاه خداوند، آتش بزرگی را که برای مجازات آنها تدارک دیده بود، به من نشان داد. این آتش آبهای عمیق دریا را بلعید و تمام زمین را سوزانید. | 4 |
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
گفتم: «ای خداوند، التماس میکنم این کار را نکن، زیرا اسرائیل کوچک و ضعیف است و نمیتواند طاقت بیاورد.» | 5 |
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
پس خداوند از این نقشه هم منصرف شد و فرمود: «این کار را نیز نخواهم کرد.» | 6 |
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
سپس، این رؤیا را به من نشان داد: خداوند در کنار دیوار راستی که با شاقول تراز شده بود ایستاده، با شاقول آن را امتحان میکرد تا ببیند تراز است یا نه. | 7 |
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
آنگاه خداوند به من فرمود: «عاموس، چه میبینی؟» گفتم: «یک شاقول.» خداوند فرمود: «من بهوسیلۀ شاقول، قومم را امتحان میکنم و این بار، دیگر از مجازات کردن آنها منصرف نخواهم شد. | 8 |
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
بتخانههای اسرائیل نابود خواهند شد و عبادتگاهایشان ویران خواهند گشت، و من بر ضد خاندان یِرُبعام، با شمشیر برخواهم خاست.» | 9 |
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
اما وقتی اَمَصیا، کاهن بیتئیل، آنچه را که عاموس میگفت شنید، با عجله این پیغام را برای یربعام پادشاه فرستاد: «عاموس به قوم ما خیانت میکند و علیه تو توطئه میچیند. سخنان او غیرقابل تحمل است. | 10 |
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
عاموس میگوید تو کشته میشوی و قوم اسرائیل به سرزمینهای دور دست به تبعید و اسارت برده میشوند.» | 11 |
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
آنگاه اَمَصیا به عاموس گفت: «ای نبی، از سرزمین ما خارج شو! به سرزمین یهودا بازگرد و در آنجا نبوّت کن و نان بخور. | 12 |
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
دیگر در بیتئیل برای ما نبوّت نکن، چون عبادتگاه پادشاه و مقر سلطنتی او در اینجا قرار دارد.» | 13 |
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
ولی عاموس جواب داد: «من نه نبی هستم، نه از نسل انبیا. کارم چوپانی و چیدن میوههای صحرایی بود، | 14 |
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
اما خداوند مرا از کار چوپانی گرفت و گفت:”برو و برای قوم من اسرائیل نبوّت کن.“ | 15 |
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
ولی تو به من میگویی که بر ضد اسرائیل پیشگویی نکنم، پس به پیامی که خداوند برای تو دارد گوش کن: | 16 |
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
”چون در کار خداوند دخالت کردی، زنت در همین شهر فاحشه خواهد شد، پسران و دخترانت کشته خواهند شد و املاکت تقسیم خواهد گردید. خودت نیز در سرزمین بیگانه خواهی مرد و قوم اسرائیل از وطن خود تبعید شده، به اسارت خواهند رفت.“» | 17 |
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”