< اول سموئیل 24 >

وقتی شائول از جنگ با فلسطینی‌ها مراجعت نمود، به او خبر دادند که داوود به صحرای عین جدی رفته است. 1
Sauli atabwera kuchokera kumene amathamangitsa Afilisti anamva kuti, “Davide ali mʼchipululu cha Eni Gedi.”
پس او با سه هزار نفر از بهترین سربازان خود به صحرای عین جدی رفت و در میان «صخره‌های بز کوهی» به جستجوی داوود و افرادش پرداخت. 2
Tsono Sauli anatenga asilikali 3,000 odziwa kumenya bwino nkhondo kuchokera pakati pa Aisraeli onse ndipo anapita kukafunafuna Davide ndi anthu ake ku Matanthwe a Mbalale.
بر سر راه به آغل گوسفندان رسید. در آنجا غاری بود. شائول وارد غار شد تا رفع حاجت نماید. اتفاقاً داوود و مردانش در انتهای غار مخفی شده بودند! 3
Iye anafika ku makola a nkhosa amene anali mʼmbali mwa njira. Kumeneko kunali phanga, ndipo Sauli analowa mʼphangamo kuti akadzithandize. Davide ndi anthu ake ankabisala mʼkati mwenimweni mwa phangalo.
افراد داوود آهسته در گوش او گفتند: «امروز همان روزی است که خداوند وعده داده دشمنت را به دست تو تسلیم نماید تا هر چه می‌خواهی با او بکنی!» پس داوود آهسته جلو رفت و گوشهٔ ردای شائول را برید. 4
Tsono anthu a Davide anamuwuza kuti, “Tsiku lija lafika limene Yehova anakuwuzani kuti, ‘Ndidzapereka mdani wanu mʼmanja mwanu, ndi kumuchita chimene chidzakukomereni.’” Koma Davide anapita mwakachetechete ndi kukadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
ولی بعد وجدانش ناراحت شد که این کار را کرده است 5
Atachita izi, Davide anatsutsika mu mtima chifukwa anadula msonga ya mkanjo wa Sauli.
و به افراد خود گفت: «کار بدی کردم. وای بر من اگر کوچکترین آسیبی از طرف من به پادشاهم برسد، زیرا او برگزیدهٔ خداوند است.» 6
Tsono anawuza anthu ake kuti, “Yehova asalole kuti ndimuchite choyipa mbuye wanga, wodzozedwa wa Yehova. Ndisamupweteke pakuti ndi wodzozedwa wa Yehova.”
داوود با این سخنان افرادش را سرزنش کرد و نگذاشت به شائول آسیبی برسانند. پس از اینکه شائول از غار خارج شد، داوود بیرون آمد و فریاد زد: «ای پادشاه من!» وقتی شائول برگشت، داوود او را تعظیم کرد 7
Choncho Davide anabweza mitima ya anthu ake ndi mawu amenewa, ndipo sanawalole kuti aphe Sauli. Pambuyo pake Sauli anatuluka mʼphangamo ndipo anachoka.
8
Kenaka Davide anatuluka mʼphanga muja ndipo anayitana Sauli, “Mbuye wanga!” Sauli atayangʼana mʼmbuyo, Davide anawerama ndi kugunditsa nkhope yake pansi.
و گفت: «چرا به حرف مردم گوش می‌دهی که می‌گویند من قصد جان توا را دارم؟ امروز به تو ثابت شد که این سخن حقیقت ندارد. خداوند تو را در این غار به دست من تسلیم نمود و بعضی از افرادم گفتند که تو را بکشم، اما من این کار را نکردم. به آنها گفتم که او پادشاه برگزیدهٔ خداوند است و من هرگز به او آسیبی نخواهم رساند. 9
Anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani mumamvera mawu a anthu kuti, ‘Davide wakukonzerani chiwembu?’
10
Lero lino inu mwadzionera nokha kuti Yehova anakuperekani mʼmanja mwanga mʼphanga muja. Ena anandiwuza kuti ndikupheni, koma ndakusiyani. Ndinati, ‘Sindidzapha mbuye wanga pakuti ndiye wodzozedwa wa Yehova.’
ببین ای پدر من، قسمتی از ردایت در دست من است. من آن را بریدم، ولی تو را نکشتم! آیا همین به تو ثابت نمی‌کند که من قصد آزار تو را ندارم و نسبت به تو گناه نکرده‌ام، هر چند تو در تعقیب من هستی تا مرا نابود کنی؟ 11
Tsono abambo anga, onanitu kansalu ka mkanjo wanu kali mʼdzanja langali! Popeza kuti ndinatha kudula msonga ya mkanjo wanu koma osakuphani, pamenepo mudziwe kuti ine ndilibe maganizo woti ndikuchiteni choyipa kapena kukuwukirani. Sindinakulakwireni ngakhale kuti inu mukufuna moyo wanga kuti mundiphe.
خداوند در میان من و تو حکم کند و انتقام مرا خودش از تو بگیرد. ولی از طرف من هیچ بدی به تو نخواهد رسید. چنانکه مَثَلی قدیمی می‌گوید:”بدی از آدم بد صادر می‌شود.“پس مطمئن باش من به تو آسیبی نمی‌رسانم. 12
Yehova aweruze pakati pa inu ndi ine, akulangeni chifukwa cha zoyipa zimene mukundichitazi, koma dzanja langa silidzakukhudzani.
13
Paja anthu akale anati, ‘Munthu woyipa, ntchito zakenso ndi zoyipa.’ Kotero dzanja langa silidzakukhudzani.
پادشاه اسرائیل در تعقیب چه کسی است؟ آیا حیف نیست که پادشاه وقتش را برای من که به اندازهٔ یک سگ مرده یا یک کک ارزش ندارم تلف نماید؟ 14
“Kodi mfumu ya Israeli yadzalondola yani. Inu mukuthamangitsa yani? Galu wakufa kodi? Nsabwe kodi?
خداوند خودش بین ما داوری کند تا معلوم شود مقصر کیست. خداوند خودش از حق من دفاع کند و مرا از چنگ تو برهاند!» 15
Nʼchifukwa chake Yehova agamule, inde aweruze pakati pa inu ndi ine ndi kupeza wolakwa. Yehova anditeteze ndi kundipulumutsa mʼdzanja lanu.”
وقتی داوود صحبت خود را تمام کرد، شائول گفت: «پسرم داوود، آیا این صدای توست؟» و گریه امانش نداد. او به داوود گفت: «تو از من بهتر هستی. چون تو در حق من خوبی کرده‌ای، ولی من نسبت به تو بدی کرده‌ام. 16
Davide atatsiriza kuyankhula mawu awa, Sauli anafunsa kuti, “Kodi mawu amenewa ndi akodi mwana wanga Davide?” Sauli anayamba kulira mokweza.
17
Anawuza Davide kuti, “Ndiwe wolungama kuposa ine. Iwe wandikomera mtima pamene ine ndakuchitira zoyipa.
آری، تو امروز نشان دادی که نسبت به من مهربان هستی، زیرا خداوند مرا به تو تسلیم نمود، اما تو مرا نکشتی. 18
Iweyo lero lino wandifotokozera zabwino zimene wandichitira. Yehova anandipereka mʼdzanja lako koma iwe sunandiphe.
کیست که دشمن خود را در چنگ خویش بیابد، ولی او را نکشد؟ به خاطر این لطفی که تو امروز به من کردی، خداوند به تو پاداش خوبی بدهد. 19
Kodi munthu atapeza mdani wake angamulole kuti apite wosamuvulaza? Motero Yehova akuchitire iwe zabwino chifukwa cha zimene wandichitira lerozi.
حال مطمئنم که تو پادشاه اسرائیل خواهی شد و حکومت خود را تثبیت خواهی کرد. 20
Ona tsono, Ine ndikudziwa kuti udzakhala mfumu ndithu ndipo ufumu wa Israeli udzakhazikika mʼmanja mwako.
به خداوند قسم بخور که وقتی به پادشاهی رسیدی، خاندان مرا از بین نبری و بگذاری اسم من باقی بماند.» 21
Tsopano undilonjeze molumbira lero mʼdzina la Yehova kuti sudzapha zidzukulu zanga ine nditamwalira kapena kufuta dzina langa pa banja la makolo anga.”
پس داوود برای او قسم خورد و شائول به خانهٔ خود رفت، ولی داوود و همراهانش به مخفیگاه خود برگشتند. 22
Choncho Davide analumbira pamaso pa Sauli. Pambuyo pake Sauli anabwerera kwawo, koma Davide ndi anthu ake anapitanso ku phanga kuja.

< اول سموئیل 24 >